Text
stringlengths
292
6.6k
labels
int64
0
19
Boma Lati Lilemba Ntchito Madotolo Ochuluka Boma lati lilemba ntchito anamwino ndi madotolo ambiri oti azithandiza anthu odwala mzipatala zonse mdziko muno. Walonjeza zolemba ntchito madotolo ambiri-Mhango Nduna yoona za umoyo mdziko muno Dr. Jappie Mhango anena izi lachisanu pambuyo poyendera chipatala chachikulu cha Zomba ndinso cha anthu odwala matenda a misala cha Zomba Mental mu mzinda-wu. Iwo ati apeza kuti mzipatalazi muli anthu ambiri amene akusowa thandizo la madokotala komanso anamwino ndipo ndi chifukwa chake boma lili ndi malingaliro olemba ntchito madotolo ambiri kuti anthu azithandizika mosavuta.
6
Kodi Chipuwa wabwerera kumalonda? Luso la Richard Chipuwa, goloboyi wa Flames komanso Mighty Be Forward Wanderers ndi losayamba. Pa 15 January chaka chino adachoka mdziko muno ulendo ku Mozambique koma sadapatsidweko mwayi wosewera mpaka wabwerera kumudzi sabata yathayi. Kodi zatani? Msika wasowa? BOBBY KABANGO adacheza naye kuti amve zambiri motere: Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Manja antchito: Chipuwa akuti ayese nawo ku Wanderers Kodi mwabwera, mfumu? Tafikatu amwene, tasowanatu koma mfumu. Mwalemeratu, mpaka mwabwera ndi galimoto? Hahaha nanunsotu musayambe apa Mwafika liti, mfumu? Sabata yathayi, koma ndilipo chifukwa ndikufuna ndisewere mdziko momwemuno kwa chaka chino ndipo ndibwerera chaka chamawa. Ku Mozambique kwataninso? Mwathawa nkhondo kapena? Ma documents ondiloleza kusewera mpira kumeneko sakuoneka mu system. Federation ya ku Maputo idandiuza kuti ma documents sakuoneka ngakhale Wanderers idatumiza. Izi zapangitsa kuti Chingale FC isandigwiritse ntchito. Chichokereni muja palibe chatheka ndiye ndaganiza kuti ndibwerere kumudzi kaye. Vuto nchiyani kuti asaoneke? Nanenso sindikumvetsa, koma Wanderers idanditsimikizira kuti yatumiza. Osati wathawa nkhondo? Hahaha! Mayazi, amwene, sizikukhudzananso. Ukutanthauza kuti sumasewera chichokereni kuno? Ayi ndithu, ngati ndimasewera ndi magemu opimana mphamvu komanso ku training. Apa simwatheratu, mfumu? Mumaka koma? Ndine wampira, ndimadziwa ntchito yanga ndipo kupatsidwa mpata muonanso, mfumu. Panopa ndiye ulowera timu iti? Ndikufuna ndikambirane ndi Wanderers, zikatheka mwina ndisewera kumeneko. Zikakanika ndiye ndisewerera timu iliyonse yomwe timvane. Komatu pochoka zimamveka ngati mwakangana ndi a Wanderers Ayi, padangokhala kusamvetsetsana koma zonse tidakambirana.
15
Kachali apepesa: Kulankhula motumbwa kuthe Anthu, a mabungwe omwe siaboma, katswiri pandale kudzanso mfumu ina ati andale asamaledzere ndi maudindo nkufika poiwala kulemekeza anthu omwe adawaika mmipando. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Izi zatuluka msabatayi wachiwiri kwa pulezidenti wa dziko lino Khumbo Kachali atapalamula chitedze potsekulira malo otumizira mauthenga a Lupaso Telecentre ku Karonga sabata yathayi. Pamwambowo, ati pothira mphepo odzudzula boma kuti iye pamodzi ndi mtsogoleri wa dziko lino Joyce Banda aonjeza maulendo ndipo uku nkuononga chuma cha boma, Kachali adati ulamuliro sungatule pansi udindo chifukwa cha chidzudzulocho, ati samayenda mmakomo mwa abambo ndi amayi awo a odzudzulawo kapena kuyendera ndalama zawo. Tsopano ngakhale Kachali wapepesa payekha kuonjezera pa kupepesa kudzera mwa mneneri wa boma yemwenso ndi ndunda yofalitsa nkhani Moses Kunkuyu, ena akuti Kachali kupepesako nkosakwana komanso kuti Kachali saali ndi mtima wofuna kulemekeza anthu ake. Kachali asadapepese payekha, mkulu wa bungwe loona ufulu wa anthu la Malawi Watch, Billy Banda komanso mfumu ina adati Kachali apite kwa Amalawi omwe adawalankhulira mawuwo kukawapepesa. Banda adati uku nkulankhula kodzimva komanso kosalemekeza anthu omwe amaika andale mmaudindo kotero mtsogoleri wa dziko lino achite kanthu ndi Kachali, ati akapanda kutero zisonyeza kuti akugwirizana ndi zomwe adalankhulazo. Ngakhale Kachali sadasankhidwe ndi anthu, akuyenera kuwalemekeza. Ziwatengera anthu nthawi kuti aiwale komanso kuzamukhulupiriranso, adatero Banda. Mfumu ina ku Mwanza, yomwe sidafune kutchulidwa, yati mawu a Kachali angachotsere anthu chidwi mwa utsogoleri wake. Uku nkunyazitsa ena ndipo sindidayembekezere kuti mawuwa angachokere pakamwa pawo, idatero mfumuyo. Mkulu wa bungwe loona ufulu wa ogula la Consumers Association of Malawi (Cama), John Kapito, wati mawu a Kachali ngolakwika kotero achotsedwe. Mtsogoleri wa dziko lino, yemwe adasankha Kachali paudindowu, akuyenera achitepo kanthu mwachangu pomuchotsa, adatero Kapito mchikalata chodzudzula Kachali. Naye katswiri pa ndale, Blessings Chinsinga wati atsogoleri athu alekerera chifukwa kukadakhala kumaiko ena monga Kenya, Kachali anakayankha mlandu kubwalo lamilandu. Sikale [pomwe] timakhala limodzi ndi Kachali kudzudzula malankhulidwe otere; kumva kuti lero iye akulankhula zotere zikusonyeza kuti anthuwa amayiwala pomwe ali pabwino. Amalawi tisalekerere malankhulidwe otere; tidzudzulepo, ndipo chipani cha PP chilankhule ndi Kachali, adatero Chinsinga. Kagemulo Kanyenda wa mmudzi mwa Mwaswa kwa T/A Kyungu mboma la Karonga wati Kachali akapepese yekha. Edward Chimkwita wa mmudzi mwa Malika kwa T/A Mpama mboma la Chiradzulu wati kulankhula kwa Kachali kwasonyezeratu kuti kutsogoloku sangadzathandie dziko lino. Wangolowa kumene koma tikumva zimenezi, apa ife sitingataye nthawi pa iye chifukwa tawona kuti sangatithandize, adatero Chimkwita. Koma mneneri wa boma, Moses Kunkuyu wati anthu amvetse kuti kupepesa kwa Kachali kukuchokera pansi pamtima. Kulankhula mokhadzula mosakomera anthu si kwachilendo mwa atsogoleri a ndale mdziko muno. Posachedwapa, mkazi wa mtsogoleri wakale wa dziko lino, Callista Mutharika, adanyanyulanso anthu pomwe adati atsogoleri amabungwe omwe siaboma akagwere chifukwa akumudzi sasowa ndalama zakunja/mafuta agalimoto. Uko kunali ku Mzimba pa 2 Ogasiti 2011 pomwe amatsekulira chipatala cha Matuli cha K50 miliyoni. Iye adati boma likudziwa zamavuto a kusowa kwa mafuta agalimoto komanso ndalama zakunja koma amabungwe akagwere chifukwa izi sizikhudza anthu akumudzi. Kachali adasankhidwa mu Epulo kukhala wachiwiri kwa pulezidenti potsatira imfa ya yemwe adali mtsogoleri wa dziko lino, Bingu wa Mutharika. Malinga ndi malamulo, Banda, yemwe panthawiyo adali wachiwiri, adakhala pulezidenti ndipo adasankha Kachali kukhala wachiwiri wake.
11
Mmera watuluka koma samalani, atero katswiri Mmera watuluka ndipo momwe zikuonekera alimi ambiri akhoza kuchita mphumi chaka chino zinthu zikapanda kusintha, makamaka pakagwedwe ka mvula. Koma katswiri wa zamalimidwe wati mvula ili apo, mpofunikanso kutsatira njira zoyenera paulimi. Mkulu woyanganira za ulangizi ndi njira zamakono zamalimidwe, Dr Wilfred Lipita, wati mmene mvula yayambira ndi mwayi wa alimi kutsata njira zoti asadzakumane ndi zomwe zidaoneka chaka chatha. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Poyankhula ndi Uchikumbe, mkuluyu adati, mwa zina, ino ndiye nthawi yabwino yoti alimi akhoza kukolola ndi kusunga madzi ambiri kuti kutabwera ngamba mwadzidzidzi asadzanongoneze bondo mmera wawo omwe watuluka kale bwinowu ukufota. Tiyeni tichilimike panopa pomwe mvula ikugwamu. Tiyeni tikolole madzi ambiri kudzera mnjira zosiyanasiyana zomwe timadziwa zija nkusunga madzi ambiri chifukwa njira yokolola madzi ndi imodzi mwa njira zodalirika tsopano, adatero Lipita. Iye adati alimi asalole udzu kapena zitsamba kutasa mminda chifukwa zimaononga chakudya cha mbewu mmalo moti mbewu zidye chakudya chokwanira ndi kukula msanga mothamangitsana ndi mvula. Mvula ndi yosadalirika iyi masiku ano moti ikamagwa chonchi ndi nthawi yoti alimi tiigwiritse ntchito osalola kuti mwayi utiphonye. Mmunda mukangooneka udzu kapena zitsamba, lowamoni msangamsanga nkupalira kuti chakudya chomwe chili mnthaka chikhale cha mbewu zanu zokha, adatero Lipita. Mkuluyu adatinso pomwe pali mwayi wa manyowa kapena feteleza, alimi asazengereze kuthira koma motsatira malangizo ochokera kwa alangizi komanso momwe unduna wa zamalimidwe umanenera. Nthawi zambiri mvula ikachuluka, mizere ndi mbewu zimakokoloka kaamba kosowa chitetezo monga chimzere chotchinga mmbalimmbali mwa munda, milaga ndi kukwezera mizere msanga. Mukaona kuti madzi akuchuluka mmunda dziwani kuti nthawi iliyonse mizere ndi mbewu zanu zikhoza kukokoloka ndiye njira yabwino nkuunda chimzere chachikulu mmphepete mwa mundawo, kuika milaga kapena kukwezera mizereyo msanga madzi asadachuluke mphamvu. Malangizo a mtundu uwu amaperekedwa mwaulere ndipo ngati anthu akuona kuti pali vuto lililonse mmunda mwawo, kudera kwawoko kuli alangizi a zamalimidwe omwe ndi okonzeka kuwathandiza nthawi iliyonse, adatero Lipita. Mu Uchikumbe wathu sabata yatha, katswiriyu adalangiza alimi kuti abzale mbewu zocha msanga komanso zopirira ku ngamba ndipo sabata ino wawonjezerapo kuti mmapando momwe mbeu zidakanika kumera ndi mofunika kupakizamo msanga. Iye adati kupakiza msanga kumathandiza kuti mbewu zisasiyane kwambiri mmunda kuti zizilandira dzuwa ndi kuwala kofanana kuopa kuti zina zingatchingike ndi zinzake kaamba kochedwa kumera. Ndikhulupirira pano alimi amadziwa kuti kupatula mchere wa mnthaka ndi madzi, mbewu zimafunanso dzuwa ndi kuwala kuti zizibiriwira bwino. Mbewu zokulira pamthunzi zimakhala zonyozoloka ndi zachikasu ndiye pachifukwachi, sipafunika kuti mbewuzo zizisiyana makulidwe ake, adatero katswiriyu.
4
Anatchezera Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Ndimukhulupirirebe? Agogo, Ndili pachibwenzi ndi mtsikana wina wake ndipo ndakhala naye mwezi umodzi. Vuto ndi loti iye ali ndi mimba ya miyezi iwiri. Kwathu sakudziwa. Ndiye nditani, agogo? Malizani, Blantyre A Malizani, Funso lako ndi lovuta kukuyankha chifukwa sukufotokoza bwinobwino chomwe chidachitika kuti bwenzi lako wakhala nalo mwezi umodzi koma akupezeka kuti ali ndi pathupi pamiyezi iwiri. Ndiye ukuti utani pamenepa? Ndikuyankha pokufunsa kaye mafunso awa: Kodi iwe ndi dokotala kuti udziwe kuti mimba ya bwenzi lakolo ndi yamiyezi iwiri? Kodi udadziwa bwanji kuti ali ndi pathupi? Adachita kukuuza ndi iyeyo kapena udachita kumva kwa ena? Nanga pathupipo ndi pa yani? Kodi iweyo, Malizani, udayamba wakhala malo amodzi ndi mtsikanayo? Ndafunsa dala mafunso amenwa chifukwa mayankho ukuwadziwa ndiwe. Ngati zili zoona kuti chibwenzi chanu chatha mwezi umodzi koma mtsikanayo akupekeza kuti ndi wodwala kale, miyezi iwiri, monga ukunenera, ndiye kuti adachimwitsana ndi wina wake, osati iwe. Tsono zili ndi iwe kuvomereza kuti mimba ili apo, ngakhale si yako, umukondabe ndipo mwana akadzabadwa udzamulera ndi kumusamalira. Koma nkutheka? Iwe ndinu Yosefe kuti uvomereze kuti udzatero popanda vuto lililonse? Ganiza mofatsa ndipo chilungamo choti uchite chioneka chokha. Inde, nkutheka kuti bwenzi lakolo ndi lachilungamo ndipo lidakuuza za pathupipo. Ndi ochepa amene angatero. Ndiye zili ndi iwe kupitiriza chibwenzi chanu kapena kuchithetsa mwamtendere. Ndazama mchikondi Agogo, Ndimadziwa kuti kukhala pachibwenzi uli pasukulu ndi zolakwika, koma nanga ine nditani? Ine ndine mtsikana wa zaka 16 ndipo ndili mchikondi ndi mnyamata wina yemwe timakondana kwambiri ndipo timathandizana nkhani za sukulu, za kutchalitchi ndi zina zotero ndipo tinalonjezana kuti sitidzagonana mpaka titakwatirana. Koma vuto ndi loti kwathu amandikaniza kupanga chibwenzi ati zimalakwitsa sukulu ndipo utha kutenga mimba. Ndimayesetsa kuti ndithetse chibwenzichi koma ndimakanika chifukwa ndimamukonda kwambiri, ndiye nditani ine? Amene akukuuza zoti kukhala ndi chibwenzi uli pasukulu sakulakwa, mwanawe. Uwamvere! Poyamba zimayamba choncho, malonjezo, kuthandizana, izi ndi izi, kenaka mutu umaima ndipo pamene uzidzati hii! ndapanga chiyani? zako zitada. Ndithu, mwana iwe, nthawi yokhala ndi chibwenzi siinakwane chifukwa udakali wamngono ndipo uli iwe apo ndi pamsinkhu wovuta zedi. Samala, ungadzanongoneze bondo. Zinazi ndi bwino kuzipewa. Panopo ukuona ngati mnzakoyo akukukonda mchoona pamene ali ndi kampeni kumphasa. Amayamba kukulowa pangonopangono ngati thekenya kenaka udzangozindikira zinthu zalakwika, wakuchimwitsa! Limbikira sukulu kaye, zachibwenzi pambuyo. Sukulu ndi zibwenzi siziyenderana. Imva izi, mwana iwe, mawu a akulu amakoma akagonera. Ofuna Mabanja Ndikufuna mkazi wa zaka pakati pa 18 ndi 21. Ndine mphunzitsi. Amene angasangalatsidwe aimbe pa 0881 939 676. Zachibwana ayi, koma zasiliyasi. Ndine mwamuna wa zaka 27 ndipo ndikufuna mkazi wokongola woti ndimkwatire. Mkaziyo akhale wosachepera zaka pakati pa 21 ndi 24, woti adalemba kale mayeso ake a MSCE komanso wopanda mwana. Ngati ali pantchito zitha kukhalanso bwino kwambiri. Omwe angandifune andiyimbire pa 0884 322 798. Ndine mtsikana wa zaka 19 ndipo ndikufuna mwamuna womanga naye banja. Akhale wa zaka zosapitirira 27. Wotsimikiza aimbe pa 0885 552 045. Ndili ndi zaka 28 ndipo ndili ndi ana awiri. Ndikufuna mwamuna woti ndimange naye banja koma akhale woti adayezetsapo magazi ndipo adapezeka ndi kachilombo ka HIV. Wasiliyasi aimbe pa 0881496 409.
12
Boma lilonga mafumu 250 Boma kudzera muunduna wa za maboma aangono latsimikiza kuti mafumu 250 aikidwa pamndandanda wolandira nawo mswahara kupangitsa kuti ndalama zopita ku thumba la mafumuwa zikwere. Nduna ya maboma aangono, Kondwani Nankhumwa, wati nkhani ya mafumu ili choncho chifukwa ntchitoyi idayambika kale ndi mtsogoleri wakale Joyce Banda ndipo boma la DPP likungopitiriza ndondomekoyi. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Mafumuwa adawakweza ndi mtsogoleri wakale Joyce Banda koma adali asadawaike pamndandanda wolandira ndalama komanso ena adali asadalamulidwe kuti ayambe kugwira ntchito yawo. Chomwe boma la DPP lapanga, ndi kuwalonga mafumuwa kuti ayambe kugwira ntchito komanso kuwaika pamndandanda woti ayambe kulandira mswahara, adatero Nankhumwa, pocheza ndi Tamvani pafoni. Nankhumwa wati boma la DPP lakweza mafumu awiri okha omwe ndi Ngolongoliwa ndi Toleza koma ena onse adakwezedwa ndi Banda. Ma Paramount amalandira K50 000, Senior Chief K30 000, T/A K18 000, Sub T/A K8 000, magulupu K5 000 ndi nyakwawa K2 500. Nankhumwa akuti pakadali pano K1.7 biliyoni ndiyo ikugwiritsidwa ntchito kulipirira mswahara wa mafumuwa ndipo wati ndi kuonjezereka kwa enaku kupangitsa kuti ndalamazi zifike pafupifupi K2.5 biliyoni. Izi zikudza pamene maunduna ena ofunika monga a zamaphunziro ndi zaumoyo alandidwa ndalama zina kupangitsa kuti maundunawa alephere kulemba aphunzitsi ndi anamwino ena. Yemwe amathirira ndemanga pa nkhani zaumoyo ndi zipatala, Martha Kwataine, komanso kadaulo pa ndale Henry Chingaipe adzudzula izi ndipo ati kulibwino ndalamazi zipite maunduna. Dziko lino lili pampanipani wa zachuma, zomwe zachititsa kuti boma lichepetse ndondomeko ya zachuma ndi K23 biliyoni chifukwa chomanidwa thandizo ndi maiko amene akhala akulithandiza. Nankhumwa adavomereza akuti ndalama zomwe ziyambe kupita kwa mafumuwo ndi zambiri ndipo zidakathandizadi maunduna ena amene ali pampanipani monga unduna wa zaumoyo komanso wa zamaphunziro. Timanenedwa ndipo mafumuwo amati mwina sitikuwapatsa malipiro chifukwa adakwezedwa ndi boma la Peoples Party (PP). Ndiye taona kuti nkofunika kuti tiwaike pamndandanda woti azilandira mswahara kuyambira tsopano, adaonjeza Nankhumwa. Apapa zidalakwika kale ndiye sitingachitire mwina. Inde tilibe ndalama, koma nanga tikadatani? Chifukwa izi zikadapereka mavuto ena achikhala kuti tidawasiya kuti mafumuwo asamalandire [mswahara]. Mafumu ena ayamba kale mwezi wathawu kulandira mswahara wawo malinga ndi ganizo la boma lowaika pamndandandawu. Mafumu 20 akwezedwa kale mwezi wa February mchigawo cha kummwera. Koma Kwataine akuti boma lidziwe kuti kulakwitsa kuwiri sikungabweretse mayankho kwa anthu, ndipo yati boma likadaganiza kawiri. Anthu akusowa mankhwala ndi zakudya mzipatala ndiye boma likuchotsa ndalama ku unduna wa zaumoyo kukapatsa mafumu? Boma litaunikapo bwino pamenepa, adatero Kwataine. Iye adati sikulakwitsa kusiya kaye kukweza mafumu bola nthambi zina zinthu zikuyenda bwino malinga ndi mavuto a zachuma omwe dziko lino likukumana nawo pakalipano. Anthu akulipa nkhuku ndi mbuzi kubwalo la mfumu, kodi zimenezi si zokwanira kwa mafumuwa? Ngakhale kuwasiya osamawapatsa ndalama palibe vuto chifukwa malipiro awo amapezeka kumudzi komweko. Panopa mmidzi anthu akungophana pena kumenya anthu okalamba kusonyeza kuti anthu adataya chikhulupiriro mwa mafumu. Ndiye palinso chifukwa chowapatsira ndalama zambiri ngati zimenezi? adafunsa Kwataine. Naye Chingaipe wati kulakwika kudachitika ndi boma la PP komabe boma la DPP likadaona nthawi yochitira izi. Si zobisa, dziko lino lili pamavuto a zachuma, ndiye nchifukwa chiyani boma laganiza kuti achite izi lero pamene zinthu sizilibwino? Panopa mafumu akukhudzidwa ndi ndale, nchifukwa chake ndikufuna kuti bwanji boma laganiza zowaika pa mndandanda wolandira ndalama mafuwa lero? adatero Chingaipe. Mneneri mu undunawu, Muhlabase Mughogho wati ntchitoyi sidayambe lero ndipo ili mkati mpaka mafumu otsalawa atathananawo. Sitinganene kuti mafumu otsalawo tithananawo liti koma ntchito ili mkati, adatero mneneriyu. Iye adati mafumu 41 900 ndi amene akhala akulandira mswahara mwa mafumu 42 150 amene ali mdziko muno, kusonyeza kuti mafumu 250 ndi amene sadayambe kulandira. Mafumu amene akwezedwa mwezi wa February ndi T/A Nchiramwera wa ku Thyolo; Senior Chief Ngolongoliwa ya mboma la Thyolo; Senior Chief Kuntaja wa mboma la Blantyre; Senior Chief Kanduku ya mboma la Mwanza; T/A Ngowe ya mboma la Chikwawa komwe ufumuwu waima kaye pamene nkhani yapita kubwalo. Ena amene akwezedwa ndi T/A Ndamera ya mboma la Nsanje; Sub T/A Toleza ya mboma la Balaka; Sub T/A Phalula ya mboma la Balaka; ku Machinga kuli Sub T/A Sale, T/A Nkoola, T/A Nkula, kudzanso Sub T/A Lulanga ndi Mtonda a mboma la Mangochi. Chigawo chapakati ndi kumpoto kwakwezedwanso mafumu 11 ndipo ena akwezedwa miyezi ikudzayi.
8
Ulimi wa njuchi ndi ofesi yonona Kodi ulimi wa njuchi mudayamba liti? Ulimiwu ndidayamba mu 2017. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Nanga chidakukopani nchiyani? Nditalingalira mozama ndidaona kuti ulimi wa njuchi sulira zinthu zambiri monga kulima, kugula feteleza, mankhwala ndi zina zochuluka kuti utheke. Chinthu china chomwe chidandikopa nchoti anthu masiku ano akukonda kugwiritsa ntchito uchi ngati chotsekemeretsa kusiyana ndi shuga malingana ndi zovuta zosiyanasiyana za mthupi choncho ndidaona kuti msika wake ndiosasowa komanso ndalama yake ndiyolemelera. Manduwa: Uchi wanga ndiika mmabotolo Kodi ulimiwu mukuuchitira kuti? Ku Balaka, Lilongwe ndi Blantyre. Kodi muli ndi mingoma ingati? Ndidayamba ndi mingoma 10 koma padakali pano yafika 130. Ku Balaka kuli mingoma 70, ku Lilongwe 50 ndipo ku Blantyre 10. Nanga mumapeza uchi wochuluka bwanji pa mngoma uliwonse? Ikakhala miyezi yozizira ndimapeza makilogalamu 30 pa mngoma uliwonse pomwe nthawi yotentha umatsika kufika pa 20. Uchi umachuluka nyengo yozizira chifukwa tikamafika nthawiyi njuchi zimakhala zapanga chakudya chokwanira ndi cholinga choti zizingokhala mnyumba mwawo muja ndikumadya. Chinthu china chomwe chimachititsa kuti uchuluke motere nchoti timakhala tikuchokera mu nyengo ya mvula yomwe zipangizo zogwiritsa ntchito popanga uchi monga madzi ndi maluwa zimakhala zochuluka. Kodi mukagulitsa mumapeza ndalama zochuluka bwanji pa mngoma umodzi? Mngoma umatulutsa K100 000, zikavutitsita K60 000. Kodi misika ya uchi mumaipeza motani? Msika wa uchi ndi wosasowa chifukwa alimi tilipo ochepa, koma akuugwiritsa ntchito ndiochuluka. Makampani ochuluka akhala akundipeza kuti ndiziwagulitsa uchi koma chifukwa cha kuchuluka kwa makasitomala anga sindingakwanitse. Chifukwa cha ichi, ndimaukonza, kuika mmabotolo ndikumagulitsa ndekha kwa anthu. Kodi upangiri wa ulimiwu mudauphunzira kuti? Palibe yemwe adandiphunzitsa kapena komwe ndidakaphunzira ulimi wa njuchi. Ndili mwana ndimakonda kufula njuchi choncho lunsoli lidangokhala ngati landilowerera. Nditapita ku Lilongwe ndidaona anthu akuchita ulimiwu pogwiritsa ntchito miphika ndi mateyala ndipo nditaonetsetsa momwe amachitira maganizo woyamba kukhoma mingoma adandibwerera. Ndidachita mwayi pamene bungwe la World Vision lidandipatsa bisinesi yoti ndiwapangire mingoma choncho nthawi imeneyo ndidaphunzira zinthu zambiri zokhudzana ndi ulimiwu. Kodi ndi zinthu zotani zomwe zimafunika pa ulimiwu? Zinthu zofunikira kwambiri pa ulimiwu ndi malo komanso mingoma. Mlimi amayenera akhale ndi malo womwe ali ndi chilengedwe chokwanira monga mitengo ndi madzi. Ngati alibe malo woterewa koma akufunitsitsa atachita ulimiwu, akuyenera abzale mitengo yokula msanga monga mapapaya ndi moringa ndipo akhoza kuika chitsime kuti njuchi zizipeza madzi mosavuta. Malowa akuyenera akhale wotalikirana ndi nyumba za anthu mosachepera masentimita 100. Ulimiwu sulira malo aakulu chifukwa ndi ekala imodzi yokha mlimi ukhoza kuchitapo zazikulu. Tafotokozani mwachidule momwe mumachitira ulimiwu? Choyambirira, timapaka phula mkati mwa mngoma wathu, pakhomo ndi timitengo tomwe timasanja pamwamba pa mingoma ija. Phula limathandizira kukopanga njuchi mu mngoma muja choncho zikamva fungo lake, zimalowa nkukhazikika. Tikachoka apo, timamangirira mngoma wathu ku nthambi za mtengo pogwiritsa ntchito mawaya omwe timawapakanso phula. Tikatero timati tamaliza koma timayenera tiziyendera mingoma ija kufikira njuchi zitalowa ndikukhazikika. Zinthu monga nyerere, kangaude ndi mbewa zimadana ndi njuchi choncho chimodzi mwa icho chikapezeka mu mngoma, palibe chomwe mlimi angaphule. Alimi akapeza zoterezi mu mngoma, amayenera achotse. Nanga mukamangirira mingoma mumatenga nthawi yotalika bwanji kuti mukolole? Timakolola pakapita miyezi itatu, koma nthawi zina imafika 6 malingana ndi momwe njuchi zikuchitira. Kodi ndi mavuto wotani omwe mumakumana nawo ku ulimiwu? Vuto lalikulu ku ulimiwu ndi kusowa kwa chilengedwe. Chifukwa cha ichi, ndikulimbana ndikubwezeretsa chilengedwechi ndicholinga choti ulimiwu upite patsogolo.
4
Lingalirani bwino musanathane ndi fodya Akatswiri komanso alimi ati dziko la Malawi likuyenera kulingalira mozama lisadagonjere khumbo la bungwe la zaumoyo padziko lonse la World Health Organization (WHO) pa nkhani ya malonda a fodya. Bungwe la WHO lili pa kampeni yolimbana ndi mchitidwe osuta fodya zomwe zikutanthauza kuti kampeniyi ikadzatheka, mayiko omwe amadalira malonda a fodya ngati Malawi adzapeze njira zina zopezera chuma. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Dziko lonse lapansi likhala likukumbukira tsiku lolimbana ndi mchitidwe osuta fodya pa 31 May ndipo mutu waukulu udzakhala kulingalira mavuto omwe kusuta kumabweretsa ku mtima wa munthu. Unduna wa zaumoyo wati umagwirizana kwatunthu ndi kampeni yolimbana ndi mchitidwe osuta fodya moti uli kalikiliki kukambirana ndi nthambi zina za boma kuti zimvetsetse ubwino wa kampeniyi. Ngati unduna, sitikuyenda tokha ayi tikuyendera limodzi ndi maiko anzathu komanso mabungwe ngati la WHO pa nkhani imeneyi ndipo tikugwirizana nayo kwathunthu, watero Joshua Malango mneneri wa undunawu. Koma katswiri wa zachuma Dalitso Kubalasa yemwenso ndi wamkulu wa bungwe lowona za momwe chuma chikuyendera la Malawi Economic Justice Network (Mejn) wati pakufunika kulingalira mwakuya potsatira kampeniyi. Iye wati ngakhale kampeniyi idayamba kale, fodya akadali nsanamira ya Malawi pa chuma chake komanso maziko a Amalawi ambiri makamaka mmidzi kotero tsogolo la dziko komanso Amalawi lagona pa zomwe boma lingatsate. Tikati tibwerere mmbuyo, tiona kuti fodya ndiye wakhala akutibweretsera chuma chambiri ndipo ndi mbewu yomwe sitingangoti lero ndi lero basi tiyisiye. Na pankhani ya chuma cha dziko lathu, kumeneko nkudzikhweza, adatero Kubalasa. Iye waunikira kuti fodya yekha amabweretsa K25 pa K100 iliyonse imene boma limapeza munjira zosiyanasiyana kuphatikizapo thandizo lochoka kunja ndipo kuti anthu ambiri amapeza chochita mu fodya. Padakali pano, tikudziwa kuti anthu 7 mwa 10 aliwonse amagwira ntchito yokhudzana ndi fodya. Tsono kutaya fodya anthu amenewa angadzagwire mtengo wanji, adatero Kubalasa. Mkulu wa bungwe loyanganira za ulimi ndi malonda a fodya la Tobacco Control Commission (TCC) Kaisi Sadala wati dziko la Malawi likuyenera kuyangana za malonda afodya kupyola pa nkhani ya zaumoyo. Iye wati mokonda dziko lathu, Amalawi sitikuyenera kuvomereza zoletsa malonda a fodya koma kuti tikuyenera kumalingalira za mbeu kapena zochita zina zomwe zingamathandizane ndi fodya pobweretsa chuma msika wafodya ukamatsika. Maloto amenewo ngosagwira ku Malawi kuno kunena chilungamo. Tikuyenera kuyangana malonda a fodya pa nkhani ya umoyo inde komanso tiunikirane za chuma cha dziko lathu kuti zikhala motani, adatero Sadala. Iye wati cholimbitsa mtima nchoti ngakhale kampeniyi ili mkati, zikuoneka kuti malonda a fodya akuyendako bwino kuyerekeza ndi momwe zidalili mzaka zingapo zapitazi kusonyeza kuti Malawi ikadali ndi chiyembekezo mu fodya.
2
Lingalirani zobzala mitengo Mvula masiku ano ikugwa mwanjomba, kutentha kukuonjeza, madzi sachedwa kuuma komanso nthaka ikukokoloka modetsa nkhawa. Awa ndi ena mwa mavuto omwe akatswiri akuti akudza chifukwa chilengedwe chikuonongedwa ndi kusasamala makamaka mmene anthu akudulira mitengo. Chaka ndi chaka mdzinja, Amalawi amalimbikitsidwa kubzala mitengo pofuna kubwezeretsa chilengedwe. STEVEN PEMBAMOYO adacheza ndi mkulu wa bungwe la mgwirizano wa alimi la Farmers Union of Malawi (FUM) Prince Kapondamgaga zokhudza ntchitoyi. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Kodi a Kapondamgaga nchifukwa ninji masiku ano nyengoyi ikuoneka kuti siikupanganika? Pamenepa anthu akhoza kuzungulirapo kwambiri koma nkhani yeniyeni ndi yakuti anthu adaononga chilengedwe kwambiri ndiye momwe zinthu zimayendera kale si momwe zingamayenderenso panopa ayi. Mukutanthauzanji pamenepa? Kapondamgaga kubzala mtengo chaka chatha Apa ndikutanthauza kuti momwe mvula inkagwera kale si momwe ingagwerenso pano chifukwa mwachitsanzo tonse tikudziwa kuti mvula imabwera chifukwa cha mitengo yomwe imasefa mpweya malingana ndi mmene zimakhalira mlengalenga. Panopa mitengo ija idatha ndiye mpweyawo usefedwa bwa? Nanga ngati mpweya si usefedwa, mvula ichokera kuti? Mukakamba za kutentha ndiye musachite kufunsa chifukwa mpweya wotentha omwe anthu ndi zinyama komanso mafakitale zimatulutsa, mitengo imayamwa nkumapangira chakudya ndipo imatulutsa mpweya womwe timapuma nkumanyadirawu koma tsopano mitengoyo kulibe nchifukwa chake kumatentha motere. Ndiye inu mwati alimi azibzala mitengo yambiri, ndiye kuti nkhani ya mitengoyi imakhudza alimi okha? Ayi, si ntchito ya alimi okha koma munthu aliyense kungoti ambiri mwa mavuto omwe tatchulawa akukwapula kwambiri ntchito za ulimi. Chifukwa cha kutha kwa mitengo, nthaka lero ili pamtetete zomwe zikuchititsa kuti mvula ikangogwa ngakhale pangono, madzi azithamanga kwambiri nkumakokolola nthakayo moti pano chonde chambiri chidapita. Ndiye mwati njira yake nkubzala mitengo basi? Basitu ndiye njira yake imeneyo. Komanso sikuti kubzala mitengoko ndiye kuti mukukonza kapansi muulimi okha ayi chifukwa pali ntchito zambiri za mitengo monga kutchisira fodya kwa alimi a fodya, kumangira zigafa, kuchita mapaso a nyumba, kupangira mosungira zokolola monga nkhokwe, kumangira makola a ziweto, nkhuni ndi ntchito zina zambirimbiri. Kodi mitengoyo ikhoza kubzalidwanso mwa mthirira? Palibe vuto bola ngati munthu ali ndi madzi komanso nthawi yothirira mitengoyo koma nthawi yabwino ndi nyengo ya mvula nchifukwa chake chaka ndi chaka nyengo ya mvula kumakhala nyengo yobzala mitengo. Nyengoyi ndi yabwino chifukwa kuthirira kwake nkosavuta madzi amakhala ambiri, ntchito imakhala yongolambulira basi. Mvula ikamadzati ikutha, mitengo yambiri imakhala itagwira moti siivuta chifukwa munthu akhoza kukhala sabata zingapo osathirira koma mitengo osafa. Kodi mitengoyo nkungobzalapo kuti bola mitengo kapena bwanji? Ayi ndithu mpofunika kuona posankha mitengo yobzala. Kusankha kumatengera ndi malo ake monga pali mitengo ina yoteteza ku mphepo ya mkuntho yomwe imafunika kukhala yamizu yozama kuti izipirira ku mphamvu ya mphepoyo. Palinso mitengo ina yoteteza nthaka yomwe imafunika kukhala ya mizu yoyanza bwino kuti madzi asamathamange kwambiri. Koma pankhani ya ulimi timalimbikitsanso kubzala mitengo yachonde yomwe alimi angakambirane ndi alangizi mmadera mwawo. Mlimi wamba angapeze bwanji mbande za mitengo? Eya, pali njira zambiri zopezera mbande za mitengo. Njira yoyamba ndi kugwirizana pamudzi nkuona vuto lomwe lilipo ndipo mukatero mukhoza kukauza alangizi kuti akuthandizeni komwe mungapeze mbande. Njira yomweyo mukhoza kupanga pakalabu kapena munthu aliyense payekha. Kutengera upangiri wa alangiziwo, mukhoza kuona kuti muchita bwanji chifukwa pali mbande zina zomwe alimi ena amafesa nkumagulitsa zomeramera komanso mukhoza kungogula mbewu kapena kutola mnkhalango nkufesa nokha kuti pofika nyengo ya mvula mudzakhale ndi mbande. Inuyo a bungwe la mgwirizano wa alimi mumatengapo mbali yanji pantchitoyi? Ifeyo ndi amodzi mwa magulu omwe ali patsogolo kulimbikitsa ntchitoyi moti chaka chilichonse timakhala ndi tsiku lomwe timakabzala mitengo kumalo ena ake malingana ndi pologalamu yathu. Kupatula apo, timakhalanso tikubzala mitengo patokhapatokha mmadera momwe timakhala komanso alimi ndi mabungwe ena akatiyitana kuti tikakhale nawo akakonza mwambo wobzala mitengo ife timakhala okonzeka. Nanga monse tidayambira kubzala mitengo muja siidakwanebe? Ambuye musadzakhale ndi maganizo amenewo. Mmene anthu akudulira mitengomu mungamati yobwezeretsapo yakwana zoona? Ndiponso kunenna mosapsatira pakufunika kubzala mitengo yambiri zedi kuyerekeza ndi yomwe imabzalidwa chaka ndi chaka. Osayiwalanso kuti mitengo yomwe imabzalidwa siyonse yomwe imakula; ina imafa ndiye imafunika kubwezeretsa.n Kapondamgaga kubzala mtengo chaka chathandiwo akulima.
18
Chilango cha kunyonga chiutsa mapiri pachigwa Ndawala yofuna kubwezeretsa chilango choti wopha mnzake naye aphedwe yavumbulutsa maganizo osiyanasiyana pakati pa mafumu, anthu ndi boma. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Ndawalayi idachitika Lachinayi lapitali mumzinda wa Lilongwe pomwe phungu wa kummwera kwa boma la Mulanje Bon Kalindo adatsogolera khamu la anthu kukapereka chikalata ku Nyumba ya Malamulo chopempha kuti chilangochi chibwerere. Kumayambiriro a sabata yathayi, ndawalayi isadachitike, nduna ya zofalitsa nkhani Patricia Kaliati idanenetsa kuti boma lilibe maganizo obwezeretsa chilangochi potengera pangano la maiko onse. Kaumba akaseweza moyo wake wonse kundende Dziko la Malawi lidasayina nawo mapangano ambirimbiri okhudza za ufulu wa anthu ndiye sitingabwerere mmbuyo nkuyamba kuphwanya pangano lomwe tidasayina tokha, adatero Kaliati polankhula ndi atolankhani ku Nyumba ya Malamulo. Koma mafumu ena akuluakulu monga Chindi wa ku Mzimba mchigawo cha kumpoto ndi Kabudula wa chigawo cha pakati adati iwo akuona kuti munthu wopha mnzake akuyenera nayenso aphedwe, osanyengerera. Chindi adati koma mpofunika kulingalira mofatsa pogamula milandu yotereyi kuti chilungamo chioneke kuti kodi adapha mwangozi kapena dala kuti zilangozo ziperekedwe. Kupha kuli pawiri-mwadala ndi mwangozi. Apapa tikhazikike pa wopha mwadala monga momwe opha maalubino amachitira. Amenewa akuyenera kuphedwa basi, osawanyengerera, ayi, chifukwa nawonso sadanyengerere mnzawoyo, adatero Chindi. Naye Kabudula adati palibe njira ina yoposa kupha anthu otere chifukwa moyo wawo uli ngati zilombo zolusa zomwe zingaononge mtundu. Onsewa adasemphana ndi mfumu Chapananga ya ku Chikwawa mchigawo cha kummwera yomwe idati chilango chakupha si chilango chabwino, bola ndende moyo onse. Kwa ine zakuphazo ayi, bola atati opha mnzake azikakhala kundende moyo wake wonse basi, adatero Chapananga. Anthu osiyanasiyana omwe adacheza ndi Msangulutso adaperekaso maganizo osiyanasiyana pa nkhani ya chilangochi. Bernadette Kaonga, wa ku Area 49 mumzinda wa Lilongwe, adati iye sangavomereze kuti anthu aziphedwa. Iye adati njira yabwino nkupeza njira yoti zophanazo zitheretu kapena, apo ayi, kundende moyo wonse. Mnzake yemwe adali naye limodzi panthawiyo, Mary Molosi, adati iye akuganiza kuti njira yomwe ingathetse zophanazo ndi chilango chophedwa, basi.
10
Bwanankubwa wa Boma la Chitipa Wamwalira ndi COVID-19 Bwanamkubwa wa boma la Chitipa, Humphreys Kapalamula Gondwe wamwalira kaamba ka nthenda ya COVID-19. Mneneri wa mu unduna woona za maboma aangono ndi chitukuko cha madera akumidzi Mushawase Mughogho watsimikiza za nkhaniyi polankhula ndi Radio Maria Malawi. Iye wati thupi la bwanamkubwayu layikidwa kale mmanda madzulo a lero ku Zolozolo mu mzinda wa Mzuzu. A Humpreys Gondwe amwaliradi ndi Coronavirus koma zambiri zinenedwabe. Padakalipano malirowo ayikidwa lero lomwe ku Zolozolo motsatira ndondomeko za chipatala, anatero Mughogho. Pali chiopsezo kuti ma ofesi a bwanankubwayu atha kutsekedwa kuti muthiridwe mankhwala othandiza kupewa kachilombo ka Coronavirus. Izi zadza pamene patsala masiku ochepa chabe kuti kuchitike chisankho cha mtsogoleri ndipo ma ofesi a bwanamkubwa mboma lililonse amayenera kugwiritsidwa ntchito powerengera ma voti.
6
Ulimi wa fodya usafe Maiko asanu ndi awiri a kummawa ndi kummwera kwa Africa agwirizana zogwirira ntchito limodzi pofuna kutukula ulimi wa fodya womwe pakali pano ukukumana ndi zokhoma. Nthumwi zochokera mmaikowa zidakumana Lolemba ndi Lachiwiri mkati mwa sabatayi ku Lilongwe komwe zidakambirana njira zotukulira ulimi wa fodya ndi mbewu zina zomwe zingalowe mmalo mwa fodya kutabwera chiletso cholima mbewuyi. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Potsegulira msonkhanowo Lolemba, nduna ya zamalimidwe, mthirira ndi chitukuko cha madzi, Allan Chiyembekeza, adati nkhondo yolimbana ndi kusuta fodya ndi imodzi mwa nkhondo zomwe zingalowetse pansi ulimi wa fodya. Iye adati mpofunika kuti pokambirana za momwe maiko, makamaka omwe amadalira fodya pachuma, angatetezere ulimiwu, nthumwizo zilingalirenso za mbewu zomwe zingalowe mmalo mwa fodya ataletsedwa. Pakalipano tikulimbikitsa alimi a fodya kuti azilima kwambiri chifukwa palibe chiletso chilichonse koma polingalira kuti tsiku lina akhoza kudzangoti fodya asalimidwenso, tidzakhale kuti tili kale ndi pena podalira, adatero Chiyembekeza. Iye adati mavuto omwe fodya amabweretsa pamoyo wa munthu nchimodzimodzi mavuto omwe amayamba kaamba ka zipatso zina za ulimi monga shuga, mafuta, ndi zakudya zosiyanasiyana koma chodandaulitsa nchakuti fodya yekha ndiye amalozedwa chala. Chiyembekeza adati kupha ulimi wa fodya nkufinya maiko omwe akutukuka kumene ndipo amadalira ulimi wa fodya pachuma. Maiko ambiri omwe akutukuka kumene, chiyembekezo chawo chili pafodya. Mwachitsanzo, 60 peresenti ya chuma cha Malawi gwero lake ndi ulimi wa fodya. Si maiko omwe akutukuka kumene okha ngakhalenso maiko ambiri omwe adatukuka kale monga America, Canada, maiko a ku Ulaya ndi Brazil fodya adatengapo gawo lalikulu, adatero chiyembekeza. Iye adauza nthumwizo kuti kuleka kumenyerera ufulu wa ulimi wa fodya pano kukhoza kudzapangitsa kuti mtsogolo muno mbewu zinanso zomwe timadalira zidzayambe kusalidwa momwe akusalidwira fodya. Mkulu wa bungwe la kayendetsedwe ka nkhani za fodya la Tobacco Control Commission (TCC), yemwenso adali nawo mukomiti yokonza za nkhumanoyi, Bruce Munthali, adati cholinga cha nkhumanoyo chidali kupanga mfundo zomwe maiko omwe amadalira fodya angagwiritse ntchito pofuna kuteteza mbewuyi. Munthali adati magulu omwe amalimbikitsa zothetsa mchitidwe osuta fodya monga la World Health Organization (WHO) akunka nalimbikitsa zolinga zawo ndiye ngati maiko omwe amadalira fodya sangachitepo kanthu ndiye kuti tsogolo lawo lada.
4
Zitukuko zothandiza Amalawi zisamafe Patha zaka 50 kuchokera pamene dziko lino lidalandira ufulu wodzilamulira. Tikaunikira bwino momwe chuma chikuyendera mdziko muno poyerekeza ndi momwe zili mmaiko ena amene tidalandira nawo ufulu limodzi, zimakhala zomvetsa chisoni kuti tili kumbuyo zedi. Dziko lino lakhala lili ndi atsogoleri atatu ndipo aliyense amabwera ndi nzeru zake za momwe angatukulire dziko lino. Koma zimakhala zomvetsa chisoni kuti ntchito zina zabwino zimaimitsidwa mtsogoleri akachoka kubwera wina. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Izi zimakhala choncho makamaka chifukwa amene walowa pampando amafuna kuonetsa kuti amene adalipo iye asadalowe pampando adalephera kutukula dziko lino. Tigwirizane ndi amene akunena kuti izi zikuchititsa kuti chuma cha boma chisakazike, chifukwa pofika poimika chitukukocho, ndalama zimakhala zitalowapo kale. Vuto lalikulu likumakhalanso chifukwa chakuti nthawi zambiri atsogoleri amangoyamba ntchitozi mwa okha, osachita kudutsa ku Nyumba ya Malamulo, zimene zimasonyeza kuti ntchitozo ndi maloto awo chabe. Nchifukwa chake tikuti, ntchito za chitukuko zosalingalira Amalawi zili chabe. Ntchito zongofuna kuti atsogoleri aoneke ngati ndi achitukuko koma zili zopanda tsogolo lenileni zilibe phindu.
2
Mfumu yoba mopusitsa igamulidwa mawa Bwalo lamilandu la majisitileti ku Ntchisi mawa likuyembekezeka kupereka chigamulo kwa mfumu ina Lachisanu idaepezeka yolakwa pamlandu wakuti inkabera anthu powanamiza. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Malinga ndi mneneri wapolisi ya Ntchisi Gladson Mbumpha, wogamula Young Ngoma adapeza nakwawa Nyalapu (dzina lenileni Fraser Vesiyano) yolakwa pamlandu woti idapusitsa anthu ozingwa a mmudzi mwa Chiwere kuti iwathandiza kugula feteleza ku Admarc ya mmudzi mwake. An artistic impression of a court room Ngoma adati mchitidwe wa nyakwawawo ngobwezeretsa chitukuko mmbuyo chifukwa nkuphwanya ufulu wa anthu ovutika. Chigamulo chiperekedwa Lolemba chifukwa samamva bwino mthupi, adatero Mbumpha Lachisanu. Malinga ndi Mbumpha, Nyalapu, yemwe ndi wa zaka 33, adapusitsa anthu ozingwa a mmudzi mwa Chiwere kuti awathandiza kugula feteleza ku Admarc ya mmudzi mwake. Iye adamata phula anthuwo kuti ali ndi njira zomwe angachite kuti athe kuwagulira fetelezayo koma pambuyo pake adayamba kuchita njomba. Anthuwo adali ndi makuponi koma zikuoneka kuti mmudzi mwawo, Admarc yomwe amadalira kudalibe feteleza ndiye mfumuyo itamva idaona ngati mwayi okhupukira nkuuza anthuwo kuti iwathandiza, adatero Mbumpha. Iye adati mfumuyi idauza anthuwo kuti asonkhanitse makuponi komanso asonkhe ndalama zomwe zidakwana K148 500 nkumupatsa ndipo adagwirizana kuti adzabwere tsiku lotsatilalo kudzatenga fetereza wawo. Njomba zidayamba kuwoneka anthuwo atabwera chifukwa mfumuyo idawawuza kuti abwerenso tsiku linzakero ndipo masiku amapita akuwuzidwa zomwezomwezo. Anthuwo atatopa adangoganiza zopita kwa mkulu wa pa Admarc yomwe imanenedwayo ndipo mkulu wa pamenepo Yasinta Jere adawauza kuti mfumuyo idagula feterezayo pa 11 January 2013, adatero Mbumpha.
7
Zionetsero zokhudza achialubino zilipo Anthu achialubino anenetsa kuti achitabe mbindikiro kunyumba ya boma ya Kamuzu Palace mwezi wa mawa pofuna kukakamiza boma kuti lichitepo kanthu pa za kuphedwa kwawo. Wapampando wa bungwe la Association for People with Albinism in Malawi (Apam) Overstone Kondowe wati mbindikirowo ulipo kuyambira pa 6 mpaka 8 March, ngakhale nduna ya zachitetezo Nicholas Dausi yapempha anthuwo kuti adekhe kaye chifukwa nkhaniyi siyinafike pochita zionetsero. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Flashback: Massa is seen with a placard during the search for Mark Masambuka who was later found murdered Malinga ndi Kondowe, anthu adzayenda kuchokera pabwalo la Community mtauni ya Lilongwe kudzera ku Nyumba ya Malamulo mpaka kunyumba ya boma ya Kamuzu Palace kukapereka kalata kwa mtsogoleri wa dziko lino Peter Mutharika. Kondowe adati, anthuwa akakhala konko kwa masiku atatu, ndipo masikuwa akakadutsa asadayankhidwe zakupsa akapempha mtsogoleriyu kulengeza kuti dziko lino lino lili pa chiopsezo moti iwo sangakhalemo. Tikatero tidzapempha mabungwe ndi maiko akunja kutenga anthu achialubino omwe akusowa chitetezo mdziko muno kupita mmaiko awo momwe muli chitetezo chokwanira, adalongosola motero. Iye adati anthu achialubinowa adzapempha kuchoka mdziko muno, pokhapokha mtsogoleri wa dziko lino akadzapanda kuwayankha madandaulo awo. Mtsogoleriyu akadzapanda kutiyankha, tikupempha aliyense yemwe ndi wa chialubino kudzasonkhana ku maofesi a akazembe oimira maiko akunja mdziko muno kuti apite ku maiko awo, adatero Kondowe. Malinga ndi Kondowe kalata yomwe akukapereka kwa Mutharika ili ndi madandulo akuluakulu asanu. Mwa madandaulowa ena akupempha boma kuti lipereke ndalama zokwana K3 biliyoni ku ndondomeko zomwe zidakhazikitsidwa chaka chatha momwe muli ntchito zothandizira anthuwa zomwe mwa zina zikukamba zowamangira nyumba zolimba zoti zigawenga zizikanika kuthyola, kuwapatsa chitetezo chokwanira. Iye adatinso anthuwa akufuna bwalo la milandu la paderadera loweruza milandu ya anthu okhudzidwa ndi kuphedwa kwa anthu achialubino. Tikufunanso kuti kukhazikitsidwe bungwe lapadera lofufuza komwe akuti kuli misikako chifukwa ife tikudabwa kuti anthu omwe akugwidwa ndi angonoangono awa, koma osati akuluakulu awo, eni ndalamawo, adatero Kondowe. Iye adati zafikapa boma komanso mtsogoleri wa dziko lino alephera kuwateteza. Malinga ndi Kondowe dziko lino liunikenso malamulo a ufiti komanso asinganga azikhala mkaundula ndi kumagwira ntchito yawo motsatira malamulo okhazikitsidwa. Koma Dausi adauza msonkhano wa atolankhani Lachiwiri ku Lilongwe kuti anthu a chialubino achepetse moto chifukwa zinthu sizidafike povuta penipeni. Zinthu sizidafike poti nkuabindikira ku nyumba ya chifumu kapena kuyamba kupempha kusamuka mdziko muno ndi kukakhala kumaiko a kunja, adatero Dausi. Izi zawonjezera mkwiyo wa anthuwa omwe pofika Lachitatu bungwelo lidalengeza kuti atuluka munthambi yomwe mtsogoleri wa dzino lino adakhazikitsa poyangana za ufulu wa anthuwa. Kondowe adati zomwe adanena Dausi zikusonyeza kuti boma lilibe chidwi pa chitetezo cha anthu a achi alubino. Kuchokera mchaka cha 2014, anthu okwana 25 ndiwo aphedwa mdziko muno pa zikhukhulupiliro zoti mafupa ndi zina mwa ziwalo zawo nzolemeretsa. Ndipo naye womenyera ufulu wa anthu Gift Trapence adati a mabungwe apitiriza kukakamiza boma kuti liteteze anthuwa popereka ndalama ku ndondomeko yomwe muli ntchito zowatetezera chifukwa pakadalipano palibe chomwe bomali likuchitapo. Iye adatinso ali ndi chisoni chachikulu chifukwa cha kulankhula kopasula kwa Dausi. A boma alephera, ndi chifukwa chake anthuwa akufuna kungosamuka mdziko muno. Ndife okhumudwa kwambiri, adatero Trapence. Koma pomwe Tamvani adalankhula ndi mmodzi mwa asinganga mdziko muno pofuna kumvetsetsa ngati ziwalo za anthu achialubino zingalemeretse anthu, singanga wina wa mboma l;a Salima Jamitole Kadango adati ndi bodza la mkunkhuniza kuti munthu angalemere ndi ziwalo za anthuwa. Zikuchitika kwathu kuno ndi chipongwe chabe, palibe angalemere chifukwa cha ziwalo za anthu achialubino. Anthuwa akuphedwa chabe. Ife ngati asinganga kwathu nkuchiza anthu basi, adatero Kadango. Pomwe mfumu Kameme ya mboma la Chitipa kumalire a dziko lino ndi la Tanzania komwe mchitidwewu udachokera idati zomwe zikuchitika mdziko muno ndizochititsa manyazi. Bwanji boma kufufuza za momwe anzathu a ku Tanzania adathana nalo vutoli? Apa tisalozanenso zala koma tifufuze kuchokera kwa anzathuwa za momwe adachitira, adatero Kameme.
15
Singanga Wanjatidwa Kamba Kogwirira Mwana Apolisi mboma la Chikwawa amanga singanga wina wa mankhwala azitsamba pomuganizira kuti wagwirira mwana wa zaka khumi ndi zitatu zakubadwa. Wachiwiri kwa mneneri wa apolisi mbomalo Sergeant Dickson Matemba watsimikiza zankhaniyi. Iye wati mkuluyu Goodson Bandecha wa zaka 44 zakubadwa, anachita izi pa 12 mwezi uno ponamiza msungwanayu kuti achira matenda a mmimba omwe amadwala akagona naye ndipo anamuwopseza kuti akakana kuchita naye izi msungwanayu achita misala. Atachita naye zadamazo msungwanayu anakaulura kwa makolo ake omwe anatengera nkhaniyi ku polisi omwe anamanga mkuluyo. Makolo a mtsikanayo anayitanitsa msingangayo kuti azawathandize kamba ka vuto la mmimba lomwe anali nalo ndipo apa ngangayo anapezerapo mwayi ndi kugwirira mwanayo, anatero a Matemba. Padakali pano apolisi mbomalo amanganso bambo wina yemwe anaba mwana ndi kumakakhala naye ngati banja kotero alangiza anthu mbomalo kuti asamalire ana awo komanso asamakhulupirire asinganga.
7
Tinkakalongosola za ntchito Okaona nyanja amakawonadi ndi mvuu zomwe. Mawuwa apherezedwa ndi ukwati wa Amos Mazinga wa ku Dowa mmudzi mwa Ngozi T/A Chiwere ndi Regina Mkonda wa ku Mulanje mmudzi mwa Reuben. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Awiriwa akuti adakumana kuofesi ya maphunziro ku Nathenje mu 2014 atamaliza maphunziro a zauphunzitsi komwe amakolongosola za komwe azikagwirira ntchito. Amos adati iye atangomuona Regina, mtima wake udadumpha kwambiri. Amos ndi Rehina kupsopsonana tsiku la ukwati wawo Ndine mmodzi mwa anthu omasuka ngakhale pagulu koma tsikulo ndidaona nyenyezi yothobwa mmaso, adatero Amos. Iye akuti panthawi yomwe iwo amayembekezera kuthandizidwa, mpamene adapeza mwayi wolankhulana ndi msungwanayo ndipo adacheza bwino mpaka kupatsana nambala za foni. Kusiyana kwa pamenepo kudali madzulo atalandira thandizo koma kudali kusiyana pamaso chabe chifukwa macheza awo adapitirira kudzera palamya. Tidakhala nthawi yaitali tikuchezerana palamya mpaka tsiku lina nditalimba mtima ndidayambitsa nkhani ya chikondi koma kunena zoona ndidalimbana naye mpaka adatheka, adatero Amos. Iye akuti chikondi chake pa Regina chidakula kwambiri kaamba ka khalidwe lake lokonda kupemphera, kuchita zinthu mwa nzeru ndi modzilemekeza komanso mwasangala. Regina adati iye poyamba adamutenga Amos ngati mchimwene koma pangonopangono chikondi chidayamba kumugwira moti samafunanso kuti Amos adzagwe mmanja mwa munthu wina koma iye. Iye adati ngakhale amakanakana poyamba, mtima wake udali utalola kale koma amafuna kuona ngati Amos adalidi munthu wachilungamo wosangofuna kumuseweretsa. Sindidafune munthu woti kugwa naye mchikondi panthawi yochepa kenako nkukhumudwitsidwa ndiye ndimayenera kuonetsetsa kuti ndikudzipereka mmanja oyeneradi, adatero Regina. Ukwati adamangitsa kumpingo wa CCAP.
2
Chimunthu Banda Walowa Tonse Alliance Speaker wakale wa nyumba ya malamulo Henry Chimunthu Banda walengeza kuti akhala pambuyo pa mgwirizano wa zipani za ndale wa Tonse, pa chisankho chatsopano cha president chomwe chikudzachi. Watuluka DPP-Banda Banda yemwe anali wa chipani cha Democratic Progressive (DPP), miyezi yapitayo anadabwitsa anthu atakana kukhala nduna ya boma pamene mtsogoleri wa dziko lino Peter Mutharika anamusankha. Chimunthu Banda yemwenso ndi phungu wa dera la kumpoto kwa boma la Nkhotakota wati iye pamodzi ndi anthu aku dera lake awona kuti nthawi yakwana tsopano yosintha zinthu mdziko muno posankha mtsogoleri yemwe angayendetse dziko lino mosakondera. Pakadali pano chomwe anthu ndingakuuzeni ndi chakuti chisankho chikudzachi ndi choti anthu akasankhe ngati akugwirizana ndi zomwe zikuchitika mdziko muno kapena ayi choncho anthu a kuno ambiri mwa iwo aganiza zosintha zinthu, anatero Banda. Poyankhulapo pa nkhaniyi mlembi wamkulu wachipani cha DPP a Grezelder Jeffrey (DPP) wati sakuopa ndipo sakudabwa kuti a Chimunthu alengeza izi ponena kuti iwo anatuluka mchipanichi kalekale.
11
Atentha nyumba kaamba ka K2 000 Mkulu wina ku Ntchisi waona mbwadza atagamulidwa kuti akaseweze zaka 8 kundende kaamba kobutsa nyumba ya mnzake chifukwa cha ngongole ya K2 000. Escom in free-for-all fuel scam Wait gets longer Secrecy over party funders Bwalo la milandu ku Ntchisi pa 27 November lidalamula Thokozani Paul, wa zaka 21, yemwe amachokera mmudzi mwa Mdaopamudzi mdera la T/A Nthondo mbomali kuti akagwire ntchito yakalavulagaga kaamba koyatsa nyumba ya nyumba ya Winston Njirisi, wa zaka 39. Woimira boma pamilandu, Sergeant Austin Daudi, adauza bwaloli kuti bamboyu, yemwe ali pabanja komanso ali ndi ana, adapalamula mlanduwu usiku wa pa 21 November pamudzi wa Chimbaka mdera la Nthondo lomwelo. Malingana ndi Daudi, Njirisi akuti adali ndi ngongole ya K2 000 ya womangidwayu yomwe ankafuna kugulira ndowa ya chimanga. Wodandaula adalephera kupereka ndowa ya chimanga kwa womangidwawa komanso kubweza K2 000, zomwe zidakwiyitsa omangidwawa. Patsikulo onse awiri adapita kukamwa mowa ndipo ali komweko mkangano udabuka kaamba ka ngongoleyo ndipo mkanganowo udakafika mpakana kunyumba ya wodandaulayu, adatero Daudi. Iye adati cha mma 7 koloko usiku Paul adanyamuka kunyumba ya Njirisi kupita kunyumba kwake ndipo patangodutsa mphindi makumi atatu, adabwerera ndi cholinga chokabutsa nyumba ya mnzakeyo ndipo panthawiyo nkuti Njirisi akugona mnyumbamo ndi banja lake pomwe nyumbayi imayaka. Adapulumuka kaamba ka kukuwa kwa anthu amene adaona nyumbayo ikuyaka ndipo adathawira panja atangopulumutsamo chitenje chimodzi ndi masikito. Atakaonekera kukhoti pa 27 November, Paul adapezeka wolakwa pamlandu wotentha nyumba motsutsana ndi gawo 337 la malamulo a dziko lino. Popereka chigamulo, majisitireti Dorothy Kalua adati mlanduwu ndi waukulu potengera kuti wodandaulayo adamusiya padzuwa popeza nyumba ndi katundu wambiri adapsera momwemo.
7
Zaka 30 zolimbana ndi umphawi zapita mmadzi Bungwe loona za maphunziro, sayansi ndi chikhalidwe mumgwirizano wa maiko a dziko lapansi la UNESCO lati dziko la Malawi lalephera kutukula miyoyo ya anthu ovutika mzaka 30 zomwe lakhala likuyesetsa kutero. Zotsatira za kafukufuku yemwe bungweli lidapanga pogwiritsa ntchito nthambi ya zakafukufuku ya Centre for Social Research, zaonetsa kuti mmalo mosintha miyoyo ya anthu, mfundo zomwe boma lakhala likutsatira mmagawo atatu zangowonjezera mavuto a Amalawi. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Ndondomeko zothetsera umphawi zalephera kukwaniritsa zolinga zake pamene Amalawi ambiri akusaukirasaukirabe Zotsatira za kafukufuku yemwe adachitika, zaonetsa kuti mavuto omwe amayi, achinyamata, ana angonoangono ndi olumala amakumana nawo adaonjezereka chifukwa cha mfundo zomwe zimayenera kuchepetsa mavutowo, lipoti la zotsatira za kafukufukuyo latero. Malingana ndi lipotili, ndondomekozi zidayamba mzaka za mma 1980 pomwe mabungwe a World Bank ndi International Monetary Fund (IMF) adayambitsa pologalamu yosintha zinthu ya Structural Adjustment Programme. Itatha pologalamuyi, mzaka za mma 1990, boma lidakhazikitsanso pologalamu yothetsa umphawi ya Poverty Alleviation Programme, kenaka Poverty Eradication Programme ndipo itatha iyi, kudabweranso pologalamu ya Malawi Growth and Development Strategy (MGDS). Lipoti la bungwe la UNESCO lati chodandaulitsa nchakuti mapologalamu onsewa adalephera kukwaniritsa zolinga zake koma mmalo mwake zidangoonjezera mavuto omwe zimafuna kuthetsawo. Potsirapo ndemanga pa zomwe bungweli lanena, nduna ya zachuma Goodall Gondwe wati kutsutsa zotsatira za kafukufukuyu nkulakwitsa koma chofunika ndi kuunika momwe muli zigweru zofunika kukonza kuti mavuto a umphawi ndi kusiyana pachuma pakati pa opeza ndi osauka kuchepe. Gondwe adati boma lipanga zotheka kuti mavutowa azitha pangonopangono mpaka idzafike nthawi yoti anthu onse ali pamtendere ndipo mavuto awo achepa. Katswiri pa zachuma Henry Kachaje wati nkhani yotukula chuma ndi kuchepetsa mavuto omwe anthu amakumana nawo njofunika kugwirana manja pakati pa boma, makampani omwe si aboma ndi mabungwe. Mkuluyu wati kuti chuma chikwere ndipo anthu apepukidwe, mpofunika kuyamba kutukula ntchito za malonda ndi kukonza kayendetsedwe ka chuma cha boma pokonza ndondomeko ya chuma yabwino ndi kuitsatira. Nkhani yothetsa mavuto si yapafupi koma njotheka bola patakhala ndondomeko yabwino ya chuma cha boma ndi njira zoyendetsera ndondomekoyo mwaluntha. China ndi kulimbikitsa mgwirizano pakati pa boma, makampani ndi mabungwe, adatero Kachaje. Aphungu a ku Nyumba ya Malamulo akuyembekezeka kuyamba mwei uno kuti akakambirane za ndondomeko ya chuma cha 2016/2017 ndipo Kachaje adati apa ndipo poyenera kuyambira popanga ndondomeko yoganizira za umphawi wa anthu. Malinga ndi zotsatira za kafukufuku yemwe adachitikayu, mavuto monga kusiyana kwakukulu pa chuma pakati pa magulu a anthu osiyanasiyana, nyumba za boma zomwe sizidamangidwe moganizira anthu olumala ndi kusiyana mphamvu pakati pa amayi ndi abambo ndi ena mwa mavuto akuluakulu. Lipoti la bungwe la Oxfam lomwe nyuzipepala ya The Nation ya pa 22 January, 2016, lidadzudzulanso mchitidwe wolowetsa ndale pa chuma cha dziko womwe lidati kukupangitsa kuti vuto la umphawi lizinkera mtsogolo. Lipotilo lidati atsogoleri a ndale ndi amabizinesi akuluakulu amadzikundikira chuma pomwe anthu osauka akungosaukirabe. Mkulu wa bungwe la Aid and Development Charity, John Makina, adati zomwe zili mulipotili zimaonekera poyera potengera nyumba ndi sitolo amakono zomwe zikumangidwa mmizinda ikuluikulu ya Lilongwe, Blantyre ndi Mzuzu. Iye adati pomwe mmizindayi mukutukuka chonchi, mmadera akumidzi akunka nalowa pansi kusonyeza kuti ndalama zili mmanja mwa anthu ochepa pomwe ambiri akuvutika. Mavuto ena ndi kuchepa kwa chisamaliro kwa anthu okalamba, ana amasiye ndi mabanja omwe amayanganiridwa ndi amayi kapena ana, zomwe zimapangitsa kuti anthu opempha azichuluka, makamaka mmisewu ndi mmizinda ya dziko lino. Manambala akusonyeza kuti magawo atatu a ndondomeko zomwe takhala tikutsatira sadaphule kanthu polimbana ndi kusiyana pakati pa anthu monga amuna, amayi, asungwana ndi ana achichepere, likutero lipotilo. Mkulu wa mgwirizano wa mabungwe a anthu olumala la Federation of Disability Organisations in Malawi (Fedoma), Amos Action, adati anthu olumala ndi amodzi mwa anthu omwe amakumana ndi mavuto aakulu monga kusalidwa. Iye adati mfundo zina zomwe zidakhazikitsidwa nzabwinobwino koma vuto limakhala potsatira mfundozo kuti zotsatira zofunikazo zikwaniritsidwe.
2
Tambulasi Walangiza Ophunzira Apewe Kulowelera Ndale Wolemba: Thokozani Chapola .mw/wp-content/uploads/2019/10/tambulasi.jpg" alt="" width="293" height="388" />Tambulasi: Apewe kutenga gawo mu zinthu zosemphana ndi sukulu Mkulu wa sukulu ya ukachenjede ya Chancellor Professor Richard Tambulasi wapempha ophunzira pa sukuluyi kuti apewe kuchita zionetsero pakakhala zovuta zina pa sukuluyi. Professor Tambulasi amalankhula izi pa mwambo wolumbiritsa President komanso komiti yatsopano ya ophunzira pa sukuluyi. Iwo ati ophunzirawa akuyenera kutsata njira yokambirana ndi kuthetsa mavuto amene ali pakati pawo. Professor Tambulasi alangizanso ophunzirawa kuti achenjere ndi a ndale ena omwe amadzera mwa atsogoleri a ophunzirawa kuti akwaniritse zofuna zawo pa ndale. Atsogoleri amayenera kukhala zitsanzo zabwino kwa ena ndipo amenyere ufulu wabwino kwa ophunzira anzawo. Apewe kutenga gawo mu zinthu zomwe ndi zosemphana ndi maphunziro, anatero Professor Tambulasi. Phunyanya: Chomwe tinabwelera kuno ndi sukulu Poyankhulapo President yemwe wasankhidwa kumene pa udindowu Godfrey Phunyanya wati ayesetsa kugwira ntchito mokomera ophunzira anzake. Chomwe tinabwelera pano ndi sukulu ndiye ine ndigwira ntchito kuti maphunziro a anzanga apite patsogolo, anatero Phunyanya. Ena mwa anthu omwenso asankhidwa mmaudindo osiyanasiyana ndi monga Annie Fundi yemwe amusankha kukhala wachiwiri kwa mtsogoleri pa sukulupo. Mpando wa speaker wapita kwa Blessings Mmamera ndipo wachiwiri wake ndi Atupele Nsonda.
11
GANIZO LOKWEZA FIZI LIBWERETSA NJIRIMBA Kudali matatalazi ku Nyumba ya Malamulo Lachinayi lapitali pamene aphungu adapindirana ndevu mkamwa pokambirana za ganizo la boma miyezi itatu yapitayo lokweza fizi msukulu zasekonadale ndi zaukachenjede mdziko muno ndipo sizikudziwika kuti aphule poto ndani pankhaniyi. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Nkhaniyi idatentha mNyumba ya Malamuloyi pomwe aphungu, maka otsutsa ndi oima paokha, adadzudzula boma kuti silidakhoze pokwenza fizi msukuluzi kaamba koti panthawi ino Amalawi ambiri ali pamavuto aakulu a zachuma malinga ndi njala yomwe yagwa mdziko muno. Ngakhale mbali ya boma mNyumbayi idayesetsa kuti nkhaniyi isakambidwe, aphunguwo sadagonje mpakana mapeto ake adagwirizana kuti nkhaniyi ndi yofunika kuunikidwa modekha. Adayambitsa nkhani: Jumbe Boma, kudzera muunduna wa zamaphunziro, lidakweza ndalama zolipirira maphunziro msukulu za boma zasekondale ndi zaukachenjede ati pofuna kuchepetsa chipsinjo chomwe boma lidali nacho poyendetsa sukuluzi. Panthawiyo, mneneri wa unduna wa zamaphunziro Manfred Ndovie adati kukwera kwa fiziku nkopindulira Amalawi chifukwa zithandiza kuti maphunziro apite patsogolo. Pali zambiri zomwe zikufunika kukonzedwa pankhani za maphunziro. Choyamba ndi malo ophunziriramo, zipangizo zophunzirira, malo ogona ndi chakudya. Kuti izi zisinthe mpofunika ndalama ndiye mukudziwa kale mmene boma lilili pankhani ya zachuma, adatero Ndovie. Koma phungu wa chigawo cha pakati mboma la Salima, Felix Jumbe, yemwe ndi wachipani cha MCP, adati kukweza kwa fizi kwafika panthawi yomwe Amalawi ambiri ali ndi vuto la njala komanso mavuto a zachuma. Iye adati zomwe boma lidaganizazi nkufuna kusautsa anthu osalakwa omwe ali kale paumphawi wadzawoneni. Aphungu ambiri adagwirizana ndi ganizo la Jumbe ndipo mmodzi mwa iwo ndi Esther Jolobala woima payekha, yemwe adati zomwe adanena Jumbe ndi ganizo lozama lofunika kuliona bwino. Ganizo lokweza sukulu fizi silidafike nthawi yabwino. Zimenezi zisokoneza makolo ambiri ndipo ine sindili muno kufuna kusangalatsa mbali ya boma kapena yotsutsa, koma anthu a kudera langa kummawa kwa boma la Machinga, adatero Jolobala. Nduna ya zachilungamo ndi malamulo Samuel Tembenu idayesetsa kuletsa zokambirana nkhaniyi ponena kuti nyumba ya malamulo ilibe mphamvu yosintha lamulo kudzera mnjira yomwe Jumbe adatsata. Naye phungu wa kummwera kwa boma la Mangochi, Lilian Patel, wa chipani UDF, adati nkhaniyo si yofunika kukambidwa kaamba kakuti sidali pamndandanda wa nkhani zofunika kukambidwa, koma sizidamveke ndipo zidatengera sikikala wa Nyumbayo Richard Msowoya kulamula kuti nkhaniyo ikambidwe ndi kuunikidwa ndi aphunguwo. Pambuyo pake aphungu adagwirizana kuti boma lisakweze fizi panopo mpaka mtsogolomu zinthu zikayambanso kuyenda bwino kumbali ya chuma. Potsirapo ndemanga, mkulu wa mgwirizano wa mabungwe oona kuti maphunziro akuyenda bwino la Civil Society Education Coalition (CSEC), Benedicto Kondowe, adati kukweza fizi nkofunika kuti maphunziro aziyenda bwino koma adati boma silidatsate ndondomeko yabwino. Iye adati ndi mmene zinthu zilili panopa, anthu amafunika nthawi yokwanira kukonzekera osangoti lero ndi lero chifukwa Amalawi ambiri alibe ndalama. Kunena chilungamo mMalawi muno muli mavuto. Omwe ali ndi ndalama ndi anthu ochepa kwambiri ndiye kukweza fizi panthawi yomwe anthu akukonzekera zaulimi si chanzeru. Akadayamba alengeza nkupereka nthawi yokonzekera, adatero Kondowe.
3
Awiri afa ndi bibida ku KK Abambo awiri amwalira ndi mowa wa kachaso mnjira zofanana koma malo osiyana mboma la Nkhotakota. Mneneri wa polisi mbomali, Williams Kaponda, wauza Msangulutso kuti Mphatso Chinguwo, wa zaka 30, adagwa nkumwalira pamalo ake ogwirira ntchito atalenguka ndi kachaso, pomwe Khiri Bwalo, wa zaka 29, adagwera mchitsime akuchokera komwa kachaso. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Kutcheza kachasu: Mowawu umalengula kupanda kuudyera Nkhani zonsezi zachitikadi koma malo ake ndi nthawi nzosiyana ngakhale kuti onse adamwalira chifukwa chomwa kwambiri kachaso osadyera ndipo Chinguwo adalenguka kwambiri kaamba koti amakakamira kugwira ntchito, adatero Kaponda. Iye adati Chinguwo amagwira ntchito yopopa mapaipi otsekeka ndi mnzake Alfred Green, wa zaka 32, mmudzi mwa Mngoma kwa T/A Mwadzama mbomali ndipo Lachinayi, ali mkati mogwira ntchitoyo iye adangogwa, osaphuphaso. Kaponda adati mnzakeyo ataona izi adagwidwa tsembwe ndipo adathamanga kukaitana anthu ndipo adakafika naye kuchipatala atamwalira kale koma monga mwa mwambo, apolisi adapempha achipatala kuti ayese mtembowo nkuwona chomwe chidamupha ndipo adapeza kuti kudali kulenguka ndi kachaso. Timakana kuti pazikhala maphokoso munthu ataikidwa kale poganizirana kuti mwina womwalirayo adachita kuphedwa koma zotsatira zidasonyeza kuti adamwa mowa wa kachaso wambiri osadyera kanthu ndiye adalenguka nawo, adatero Kaponda. Iye adatiso Bwalo, wa mmudzi mwa Tchale, T/A Mwansambo, adalawira bambo ake, Gibson Bwalo, a zaka 63, kuti akukamwa kachaso ndipo pobwererako usiku wa pa 27-28 March adagwera mchitsime. Pa 27 March adanyamuka mma 6 koloko madzulo wa kukachaso mmudzi mwawo momwemo ndipo adapezeka mchitsime mma 6 koloko mmawa wa pa 28 March. Uyuso atamuyesa, adapeza kuti adatsamwa ndi madzi mchitsime momwe adagweramo koma kadali kaamba koledzera ngati woyamba uja, adatero Kaponda.
6
Atsogoleri akwangula kampeni lero Migwirizano ya zipani pachisankho chikudzachi zikuomba mkota wa mfundo za kampeni lero ndipo atsogoleri a mmigwirizanoyo akhala ali mbweee! kutolera mavoti otsalira. Bungwe la chisankho la Malawi Electoral Commission (MEC) dzulo lidati misonkhano ya kampeni itsekedwa pokwana 6 koloko mawa mmawa. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Mutharika (Kumanzere) ndi Chakwera ndiwo atengetsana kwambiri Malingana ndi mkulu woyanganira za kampeni mchipani cha Malawi Congress Party (MCP) Moses Kunkuyu, mtsogoleri wa MCP Lazarus Chakwera akhala pabwalo la Masintha ku Lilongwe pomwe othandizana naye mu mgwirizano wa Tonse Saulos Chilima wa UTM akhala ku Blantyre. Tikufuna tikumbutse anthu mfundo zathu. Tidadutsamo kale koma tikawakumbutse ndi kuwatsimikizira kuti takonzeka kulowa mboma, adatero Kunkuyu. Koma Lachinayi, Mgeme Kalilani yemwe ndi mneneri wa mtsogoleri wa mgwirizano wa DPP ndi UDF Peter Mutharika adati pulogalamu ya momwe Mutharika akwangulire kampeni yake siyidatsimikizike. Mutharika akupangira limodzi kampeni ndi Atupele Muluzi wa UDF yemwe ndi wotsagana naye mumgwirizano wawo. Panyengoyi, migwirizano ya Tonse Alliance komanso DPP/UDF zalonjeza mfundo zosiyanasiyana zachitukuko komanso umoyo wabwino. Mwa zina, mgwirizano wa Tonse Alliance udatsindika zotsitsa mtengo wa feteleza kufika pa K4 500 thumba la makilogalamu 50, kulemba ntchito achinyamata omwe ali paulova ngakhale ali ndi zoyenereza, kuthetsa mchitidwe wa tsankho, kuyambitsa ndondomeko yoti anthu okalamba azilandira ndalama pamwezi ndi kutukula ntchito zamalimidwe, zaumoyo ndi kulemekeza malamulo. Mgwirizano wa DPP/UDF mfundo zake mudali nkhani yolimbikitsa kutukula achinyamata powaphunzitsa ntchito zamanja ndi kuwapatsa ngongole, kutukula amayi pantchito zosiyanasiyana, kulimbikitsa umodzi ndi chilungamo, kutukula ulimi popitiriza pulogalamu ya sabuside, kutukula ntchito za makina a kompyuta pogawa mayuniti a Intaneti aulere komanso kupitiriza pulogalamu yolemba achinyamata ntchito. Ngakhale kampeni yafika kumapeto chonchi, migwirizanoyi yayenda mowirira makamaka pa nkhani ya zipolowe ndi kuchitirana zamtopola zosiyanasiyana. Anthu ena kumbali zonse adamenyedwa, kuvulazidwa, kuphwanyiridwa ndi kuotcheredwa katundu chifukwa chopezeka mmadera omwe ena amaona kuti samayenera kupezekako. Mneneri wapolisi James Kadadzera adatsimikiza kuti apolisi adalandira malipoti oti anthu ena amachitira zamtopola anzawo pakampeni ndipo adalonjeza kuti akufufuza malipotiwo. Pa zokwangula kampeni lero, Kadadzera wati apolisi ayesetsa kupezeka paliponse makamaka komwe kuchitikire misonkhano kuti pasakhale za mtopola zilizonse. Ndi cholinga chathu kuti anthu amvetsetse mfundo zotsiriza. Ukapita mwayi uwu, anthu sadzapezanso mpata omva mfundo za atsogoleri awo pachisankhochi ndiye ndi ntchito yathu kukhazikitsa bata, adatero Kadadzera. Zipangizo zovotera pachisankhochi zafika dzulo mu mzinda wa Lilongwe ndipo bungwe la Malawi Electoral Commission (MEC) likhala likutumiza zipangizozo mmaboma.
11
Anthu Agwiritse Zokomera Mulungu-Papa Papa Francisko wati anthu akuyenera kugwiritsa zinthu zokhazo zokomera Mulungu. Papa Francisko walankhula izi lachinayi pa Misa yomwe anatsogolera ku likulu la Mpingo ku Vatican.Iye wati chifukwa cha zinthu zambiri zomwe zilipo komanso zomwe zikuchitika masiku ano akhristu akuyenera kusamalitsa kuti choncho asataye chikhulupiriro chao mwa Mulungu. Pamenepa iye wati ndi kofunika kuti akhristu azipempha chaulere cha Mulungu pamene azindikira kuti akusochera. Iye wati anthu ambiri amayamba bwino chikhristu chao koma mapeto ake monga Mfumu Solomon amataya Mulungu chifukwa cha zinthu zosiyanasiyana. Papa Francisko wati Mfumu Solomon anayamba bwino ngati Mfumu popempha luntha koma mapeto ake akazi ambirimbiri omwe adakwatira adamutayitsa Mulungu woona nkuyamba kupembedza Milungu ina. Iye wati Mfumu Solomon adayamba kutaya Mulungu pangonopangono. Papa Francisko wati masiku ano anthu akutaya Mulungu pangonopangono poika mtima kwambiri pa chuma komanso kunyada pongotchula zochepa chabe. Iye wati nkoyenera kuti akhristu azipempha chaulere cha Mulungu pamene azindikira kuti akusochera.
13
Ku Zomba abwekera feteleza wa mbeya Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Odwala kuchipatala cha Zomba Central Pa Bungwe la Millennium Villages Projects (MVP) lati nthawi yakwana pamene alimi akuyenera kukolola pogwiritsa ntchito feteleza watsopano wotchedwa Mbeya amene akumakonzedwa kuchokera ku zinthu zopezeka mmadera osiyanasiyana mdziko muno. Mkulu wa bungwe la MVP Dr Andrew Daudi adalankhula izi kuchionetsero cha zaulimi chimene chidachitikira pabwalo la mfumu John Masamba kwa T/A Mlumbe mboma la Zomba. Chionetsero cha ulimichi chidakonzedwa pofuna kupereka mwayi kwa alimi ndi mabungwe osiyanasiyana amene amakhudzidwa ndi nkhani za ulimi kuti akaphunzire kwa alimi ena zimene amachita kuminda ndi kumadimba osiyanasiya mmadera mwawo. Feteleza wa Mbeya akupangidwa posakaniza ndowa imodzi ya deya, ndowa imodzi ya zitosi za nkhuku kapena nkhumba ndi theka la ndowa la phulusa komanso makilogalamu 10 a feteleza wa msitolo. Akatha kusakaniza alimiwa akumazikulunga mthumba la pulasitiki ndi kuzisunga pozizira kwa masiku 21 ndipo tsiku la 21 likafika amazitulutsa ndi kuziyanika pamnthuzi kwa masiku awiri, akatero feteleza watheka. Ubwino wa fetelezayu ndi wakuti safuna ndalama zochuluka chifukwa amakonzedwa kuchokera kuzinthu zopezeka mosavuta monga deya, phulusa, madzi ndi manyowa. Mlimi angoyenera kugula makilogalamu 10 a feteleza wachitowe kapena wobereketsa. Feteleza wa Mbeya saononga nthaka mmene amachitira winayu kotero tikuwalimbikitsa alimi kuti agwiritsitse felereza ameneyu, adatero Daudi Phungu wa ku Nyumba ya Malamulo wa derali Grace Maseko, amene adali mlendo wolemekezeka pamwambowu, adayamikira bungwe la MVP pochita kafukufuku wakuya za mmene angatukulire ulimi pakati pa alimi a kumudzi ndi cholinga chakuti nkhani ya njala ikhale mbiri yakale mdziko muno. Phunguyu adatinso akamema anzake ku Nyumba ya Malamulo kuti alimbikitse boma ndi mabungwe osiyanasoiyana kuti limutenge feteleza wa Mbeyayu ngati chida chimodzi chothandizira kuthesa njala mdziko muno. Alimi ambiri amene agwiritsa ntchito fetelezayu kumadimba kwawo akusimba lokoma kuti akolola zinthu zochuluka chaka chino ndipo anena motsimikiza kuti nyengo yobzala mbewu ikubwerayi iwo agwiritsa ntchito feteleza wa Mbeyayu basi. Fetelezayu akutchedwa Mbeya chifukwa adachokera mumzinda wa Mbeya ku Tanzania kumene akatswiri a zasayansi kumeneko atachita kafukufuku adaona kuti akhoza kupindulira alimi ochuluka zedi.
4
Anthu 15 Anjatidwa Kamba Kotentha Zipangizo Zophera Nsomba Wolemba: Thokozani Chapola mw/wp-content/uploads/2019/05/handcuff-300x168.jpg" alt="" width="300" height="168" /> Apolisi mboma la Mangochi amanga anthu khumi ndi asanu (15) powaganizira kuti anatentha zipangizo zophera nsomba za ndalama zoposa 9 million kwacha za a Labani Mhone. Wofalitsa nkhani za apolisi mbomalo Roderick Maida watsimikiza za nkhaniyi. Iye wati apa 14 mwezi uno amunawa anachita izi kaamba ka mkwiyo poganizira kuti a Mhone ndi omwe anachititsa kuti msodzi wina amire mmadzi ngati zizimba zoti adzipha nsomba zambiri. Anthuwa ati amawaganizira a Mhone kuti ndi amene anachititsa kuti msodzi wina amire mmadzi ngati mwamatsenga kuti azipha nsomba zambiri. Ndipo apa ndi pomwe anakawotcha ma boti anayi, ukonde ophera nsomba uwiri, engine ya yamaha imodzi komanso mabwato anayi, anatero a Maida. Maida wati msodzi yemwe anamira mmadziyu akupitilirabe kusowa.
7
Kamatira: Nthenda yosautsa Thenda zina ukazimva mmakutu kuchita kuwawa chifukwa chakuwopsa kwake. Anthu ambiri amataya mtima ndi matenda aja a Edzi komatu kunjaku kulinso matenda ena omvetsa ululu wadzawoneni. Ena mwa matenda otere ndi aja ena amawatcha kamatira. STEVEN PEMBAMOYO adacheza ndi Socrates Mbewe zokhudza matendawa ndipo machezawo adali motere: Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu A Mbewe, tandifotokozerani kuti mumachokera kuti ndipo mumatani. Choyamba ine kwathu ndi ku Sawawa kwa mfumu yaikulu Chikowi ku Zomba. Pano ndili muno mu mzinda wa Lilongwe kuthandiza anthu makamaka pankhani ya mankhwala azitsamba. Mwachidule ndine singanga. Mbewe: Ndachiritsa ambiri odwala kamatira Ndimangomva za matenda a kamatira, kodi amenewa ndi matenda anji? Malume, amenewa ndi matenda osautsa kwabasi. Munthu amangomva mseru, kubaya ndi kupotokola mmimba koma kuti achite chimbudzi kapenanso kutaya madzi amalephera ndiye amakhala akumva ululu koopsa. Kwenikweni matenda amenewa amayamba bwanji? Pali njira zosiyanasiyana. Zina zachilengedwe zomwe angafotokoze bwino ndi achipatala komanso pali njira za mwa anthu zochita kuponyerana zomwe kuthana nazo kwake ndi kuchikuda basi. Kuwazindikira kwake akamayamba ungawazindikire bwanji? Ndilankhula kwambiri kumbali yachikudayi chifukwa ndiko ndimadziwa kwambiri monga ndanena kale. Matenda amenewa ali mitundu pawiri. Pali kamatira wamoto yemwe munthu amangomva kutentha mmimba ndi mchikhodzodzo koma kumalephera kudzithandiza ndipo ngati sadathandizidwe, masiku 7 ndi ambiri akhoza kupita. Mtundu wina ndi wa kamatira wozizira yemwe munthu amatha kukhala sabata zitatu akungomva ululu. Inuyo mudathandizako munthu wa vuto limeneli? Ambirimbiri ndipo amabweranso okha kudzandithokoza chifukwa cha chikumbumtima cha ululu chomwe amakhala nacho. Ndathandiza anthu ambiri mmadera osiyanasiyana osati kuno kokhanso, ayi. Mankhwala ake mumatani? Pali zizimba zake. Koma chachikulu nchakuti timasema mtengo wa mankhwalawo nkuusakaniza bwinobwino ndiye munthu uja amathira theka la supuni yaingono muphala nkumwa. Akatero amatsegula mmimba kwambiri ndipo zotulukazo zimakhala zakuda kwambiri ngati makala okanyakanya. Komano oponyerayo amachita bwanji? Pali njira zosiyanasiyana koma machitidwe ake ndi amodzi. Ena amatapa chimbudzi kapena mkodzo olo madindo amatako. Ena amagwiritsa ntchito nsima yotsala kwa munthu yemwe akufuna kulodzayo kapena nkhoko zampoto momwe mudaphikidwa nsimayo. Machitidwe ake, amatenga zomwe ndatchulazi nkusakaniza ndi mankhwala kenako nkuika muchithu chosachucha kapena kudontha. Ambiri amakonda bango ndipo mkatimo amasakanizamo singano kuwonjezera ululu uja. Ndiye kuchira kwake ndi kwa asinganga basi? palibenso njira ina ngati zili zoponyeredwa, apo bii ndiye kuti wolodzayo akhululuke nkumumasula mnzakeyo. Zikakhala zachilengedwe ndiye mapilitsi aliko kuchipatala, munthu amatha kumwa nkutsekula mmimba bwinobwino. Koma chachikulu choti mudziwe nchakuti si onse omwe amadziwa mankhwala ake, ena sadziwa koma amangokakamira chifukwa chofuna makobidi. Singanga weniweni akaunika, ngati zili zachilengedwe amamuuza chilungamo munthu. Koma muzonse zomwe mwakumana nazo inuyo mumapeza kuti chimachititsa anthu kuponyerana nthenda yoopsayi nchiyani? Nkani yaikulu imakhala dumbo. Ngati munthu wina amachita nawe nsanje ndiye akuganiza njira yokuzunzira kapena ngati anthu adayambana ndiye winayo akufuna kumvetsa mnzakeyo kuwawa mpamene izi zimachitika.
6
Ngozi Zapansewu Mboma la Ntcheu Zachepa ndi 53% Apolisi mboma la Ntcheu ati akwanitsa kuchepetsa ngozi zapansewu ndi 53.8% mmiyezi itatu yoyambirira ya chakachi kuyambira January kufika March poyerekeza ndi nthawi ngati yomweyi chaka chatha. Chigalu: Takwanitsa kuchepetsa ngozi zapansewu Malinga ndi mneneri wa apolisi mbomalo, Sub Inspector Hastings Chigalu, chaka chino mu nthawiyi kwachitika ngozi zokwana 23, ndipo pa ngozi-zi anthu 12 ndi omwe afa kusiyana ndi chaka chatha pomwe anthu 26 anafa pangozi 15 zomwe zinachitika mu nthawi ngati yomweyi. Iwo ati mu mwezi wa April chaka chino kunachitika ngozi zisanu ndi imodzi ndipo mwangozi-zi anthu asanu ndi omwe anataya miyoyo yawo pamene atatu anavulala. Ndizoona kuti ife apolisi tikayamba chaka chilichonse timachigawa mmagawo atatu omwe pa miyezi iliyonse timaona mmene tagwirira ntchito ndipo chaka chino takwanisa kuchepesa miyoyo yawanthu omwe afera panseu. Iwo adandaula ndi milandu yakupha yomwe ati mchakachi yakwera ndi 9 pamene chaka chatha inali iwiri ndipo apempha anthu kuti agwire ntchito limodzi pa ntchito yolimbana ndi mavuto osiyanasiyana mbomalo.
14
Chidwi pantchito ya uphunzitsi chizilala Bungwe la aphunzitsi mdziko muno la Teachers Union of Malawi (TUM) lati zomwe lachita boma pokhazikitsa mfundo yoti ofuna kuphunzira ntchito ya uphunzitsi mmakoleji a boma (Teachers Training CollegeTTC) ayambe kulipira zichititsa kuti ambiri asakhale ndi chidwi cholowa uphunzitsi. Woyendetsa ntchito za bungweli, Charles Kumchenga, adanena izi pothirirapo ndemanga pa ganizo la boma loti ophunzira ntchito ya uphunzitsi mmakoleji 8 a boma azilipira ndalama zokwana K105 000 pachaka kuonjezera pa ndalama zomwe boma limapereka. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Pakalipano ngakhale mwana wapulayimale kumufunsa ntchito yomwe amafuna kudzagwira, ambiri satchula ya uphunzitsi chifukwa amaona okha mmene aphunzitsi akuvutikira, ndiye pano akuti munthu uzilipiranso ndalama zambirimbiri kuti ukhale mphunzitsiambiri chidwi sakhalanso nacho, adatero Kumchenga pouza Tamvani. Kumchenga adati zinthu zambiri sizili bwino nkale mmakoleji a aphunzitsizi ndipo nthawi zonse boma limathamangira kuti ndalama ndizo zavuta likafunsidwa kukonza zina mwa zinthuzo. Ndi zoonadi boma lati aphunzitsi azilipira kuti aphunzire ntchito koma nkhawa yathu ili pakuti kodi izi zisintha zinthu msukulu zophunzitsiramo aphunzitsizi? Pali zambiri zofunika kukonza monga malo ogona, chakudya ngakhalenso malo ophunziriramo, adatero Kumchenga. Iye adati ndi zomvetsa chisoni kuti ntchito ya uphunzitsi imatengedwa ngati yotsalira kwambiri pomwe ndiyo gwero la ntchito ina iliyonse. Kumchenga adatchulapo kusowa kwa nyumba zokhalamo aphunzitsi, kuchedwa kukwezedwa pantchito, malipiro ochepa, kuchedwa kwa malipiro ndi ndalama yolimbikitsira aphunzitsi akumidzi ngati ena mwa mavuto omwe amalowetsa pansi ntchito za maphunziro. Koma poikira kumbuyo zomwe boma lachita, mlembi wamkulu muunduna wa zamaphunziro, Lonely Magreta, wati boma lidaganiza zoyambitsa kulipira mma TTC ndi msukulu zina pofuna kutukula ntchito za maphunziro. Iye adati kudalira boma lokha sikungapindule kanthu chifukwa lili ndi zambiri zofunika kuchita ndiye kugawana udindo kungathandize kuti zinthu zisinthe msanga. Cholinga chathu nchakuti ntchito za maphunziro zipite patsogolo. Mwa zina, tikufunitsitsa kuti zipangizo zophunzitsira ndi zophunzirira zizikhala zokwanira kuti wophunzira aliyense azikhala ndi buku lakelake panthawi yophunzira, adatero Magreta. Iye adati wophunzira aliyense ku TTC azipereka K105 000 pachaka yomwe ikuyimirira K20 pa K100 iliyonse yomwe imafunika kusula mphunzitsi mmodzi pachaka, kutanthauza kuti boma limafunika ndalama zokwana K525 000 pa mphunzitsi mmodzi. Kupatula kuyambitsa zolipira mma TTC, boma latinso aliyense wofuna kukachita maphunziro ku Domasi komwe aphunzitsi amakaonjezera maphunziro awo, azilipira yekha. Wadipuloma azilipira K180 000 ndipo wofuna digiri ndi K280 000 pachaka Kusinthaku kwakhudzanso sukulu za sekondale komwe fizi yakwera kufika pa K12 000 ku MCDE; K10 000 kusekondale yoyendera; msekondale zothandizidwa ndi boma K75 000. Kuyunivesite komwe akuti aliyense azilipira payekha, fizi ndi K275 000 pachaka, pomwe mmbuyomu osankhidwira kumakoleji a University of Malawi ankalipira K55 000 yokha pachaka, pamene ofuna kudzilipilira ankalipira K275 000. Kuphatikiza apa, boma lati lasiya kupereka alawansi yomwe ophunzira ankalandira kuti iziwathandiza pogulira zipangizo monga mabulu ndi zowathandiza pamaphunziro awo. Mkulu wa mgwirizano wa mabungwe oyanganira zamaphunziro mdziko muno la Civil Society Education Coalition (Csec), Benedicto Kondowe, waati ganizo la bomali lili bwino, koma labwera molakwika. Pocheza ndi Tamvani, Lachiwiri lapitali, Kondowe adati zomwe lachita boma polengeza kusinthaku modzidzimutsa zichititsa kuti anthu ambiri omwe adali ndi chilakolako cha sukulu alephere kuchita maphunziro awo chifukwa sadakonzekere mokwanira. Mwachitsanzo, mukatengera ndalama zomwe amalandira aphunzitsi, [wa PT4 wongoyamba kumene ntchito amalandira K54] ndi angati angakwanitse kusunga ndalama yokalipira ku Domasi kuti akaonjezere maphunziro? Izi zikutanthauza kuti aphunzitsi ambiri aimira pomwe alipo basi, ndiye maphunziro sangatukuke choncho,adatero Kondowe. Iye adati boma limafunikira kukonza ndondomekoyi ndi kulengeza panthawi yabwino kuti anthu akonzekere, osati kungowadzidzimutsa, ayi.
3
Amukwenya ponena olumala kuti agalu Banja lina lapempha mkulu woyanganira za maphunziro mmaboma a Phalombe, Mulanje ndi Thyolo (Divisional Education ManagerDEM) kuti athane ndi mphunzitsi wina amene akumuganizira kuti adanena ana olumala pasukulu ya sekondale ya Phalombepo kuti ndi agalu. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Kalata yomwe tapeza, yatumizidwanso kwa wachiwiri kwa mkulu woyendetsa maphunziro a ana olumala, mkulu wa sukulu ya Phalombe, mkulu wa bungwe la anthu amene ali ndi vuto la kumva la Malawi National Association for the Deaf (Manad), mkulu wa mgwirizano wa mabungwe a anthu olumala la Federation of Disability Organisations in Malawi (Fedoma) ndi ena. Malinga ndi kalatayi, mpunzitsiyo akuti adachita izi pa 2 February pamene banjalo lidapita kukaona mwana wawo. Kalatayo, yomwe walemba ndi mmodzi mwa a pabanjapo, Bettie Chumbu, yati patsikulo iwo atafika pasukulupo adakumana ndi wophun-zirayo ndipo adali ndi ophunzira anzake a mavuto osiyanasiyana achibadwidwe. Sukuluyi, malinga ndi mphunzitsi wamkulu, James Kamphonje, ili ndi ophunzira azilema zosiyanasiyana monga achialubino, osamva, osalankhula ndi ena. Onse pamodzi akuti alipo 15. Chumbu adati akucheza ndi ophunzirawo mpamene mphunzitsiyo adatulukira, botolo la mowa lili mmanja nkunena mawu amene adawakwiyitsawo. Adati, mukuchita chiyani ndi agaluwa?, adatero Chumbu. Akuti adamufunsa mphunzitsiyo zomwe ankatanthauza ponena mawu amenewo, koma iye akuti adabwereza mawuwo, amvekere: Yes these are dogs [Inde, awa ndi agalu]. Gwen Mwamondwe, yemwe ankayendetsa galimoto yomwe adakwera Chumbu popita kusukuluko ndi Hussein Chindamba, yemwe adatsagana ndi nawo paulendowo, adatsimikiza za nkhaniyi ponena kuti adayesetsa kuuza mphunzitsiyo kuti zomwe wayankhula zidali zopanda mutu ndipo ayenera kupepesa, koma akuti zidakanika mpaka ana asukulu ena ndiwo adalowererapo nkumududa pamalopo. Koma Lachiwiri Msangulutso utafuna kumva mbali ya mphunzitsiyo, adangoti: Tilankhulane cha mma 5 koloko kuti ndiyankhepo. Koma titamuimbira kangapo, iye sadayankhenso foni. Kumbali yake, Kamphonje adati nkhaniyi ili pakati pa banja lodandaula ndi mphunzitsiyo ndipo mbali ziwirizi zikukambirana. Chomwe ndikudziwa nchakuti banja lodandaulalo likukambirana ndi Malikebu, zomwe agwirizane timva kwa iwo, adatero mphunzitsi wamkuluyu amene adakana kulankhulapo zambiri. Titamufunsa Chumbu ngati akukambirana ndi mphunzitsiyo, iye adati: Nkhani tidaisiya mmanja mwa akuluakulu ndiye palibe chifukwa choti tiyambe kukambirana ndi mphunzitsiyu. Koma wakhala akundiimbira foni kuti tikambirane. Mafoni amene akuimba sindikuwayankha ndipo mmalo mwake adanditumizira uthenga wapafoni kuti ndikupepesa kuti mundikhululukire. Ndikukudikirirani kuti ndidzapepese pamaso. Chonde ndikhululukireni, sizidzachitikanso, Mulungu akudalitseni. Mkulu woyanganira maphunziro mmaboma a Thyolo, Mulanje ndi Phalombe, Christopher Nauje, adati akudikira lipoti kuchokera kwa banja lolakwiridwa. Ndidalankhuladi palamya ndi abanja lodandaula pankhaniyi ndipo ndidawauza kuti atumize dandaulo lawo kuofesi yathu polemba kalata. Panopa ndikudikirabe kalatayo ndiye sindingayankhepo kanthu, adatero Nauje. Mkulu woona za maphunziro a olumala muunduna wa zamaphunziro, David Njaidi, adatsimikiza kuti walandira dandaulo kuchokera kubanja lodandaula ndipo wati akhala pansi kuti aone chomwe angachite. Apa chatsala nchakuti tikambirane ndipo tipereke zomwe tapeza komanso zomwe tingachite ndi mphunzitsiyo, adatero Njaidi.
7
Pimani onyamula mafuta Kati deru kadaopsa mlenje. Anthu okhala kwa Sonda komwe kuli nkhokwe za mafuta mzinda wa Mzuzu sakumwa madzi ndi madalaivala amene amadzatula mafuta kuchokera mdziko la Tanzania. Pomwe tinkasindikiza nkhanyiyi nkuti mdziko la Tanzania anthu 285 akudwala matenda a Covid-19, 11 atachira ndipo 10 atamwalira ndi matendawa. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Izi zikupereka mantha kwa anthu a kwa Sonda kuti madalaivala omwe akubweretsa mafuta mderali atha kuwatengera imfa. Madalaivalawa akamalowa mdziko muno sakuwabindikiza monga zikuyenera kukhalira pamene ukutuluka kapena kulowa mdziko muno. Galimoto zonyamula mafuta kungofika kumene kuchokera ku Tanzania Koma mneneri wa unduna wa zaumoyo Joshua Malango adati anthu asachite mantha chifukwa boma liyamba kubindikiza madalaivalawo kwa sabata ziwiri pachipata cha dziko lino kuyambira sabata ino. Iye adati kusunga madalaivalawo kuthandiza kuthana ndi matendawo. Anthuwo sadziyezedwa ngati ali ndi Covid-19 kapena ayi mokakamizidwa, koma chizichitika nchakuti aliyense wolowa mdziko muno adzikhala kaye kwa sabata ziwiri pa malo olowerawa, kuti tione ngati akuonetsa zizindikiro za nthendayo ndipo aziyesedwa akaonetsa zizindikirozo, adatero Malango. Malinga ndi wapampando wa nthambi ya chitetezo mderalo, Isaac Soko, madalaivalawo akafika kumeneko amakonda kuyendayenda, zomwe zikupereka chiwopsezo kuti atha kubweretsa mliri wa Covid-19 kuderalo. Soko adati nthawi zina madalaivalawo amakhala oposa 40 koma satsatira ndondomeko zoyenera kuti asafalitse kapena kutenga matendawo. Tili pachiwopsezo chachikulu cha nthenda ya Covid-19 chifukwa anthuwa akuchokera mdziko la Tanzania komwe nthendayi yafala kwambiri, adatero Soko. Iye adati mantha awo akuchuluka chifukwa madalaivalawo akafika mdziko muno akumayendayenda ndi anthu a mderalo. Iye adati madalaivala ambiri ndi a chi Swahili ndiye akafika kuno Chichewa chimawavuto, zomwe zimawachititsa kuti atengane ndi Amalawi amene amalankhula Chichewa. Mfumu ya deralo, Belewa, yomwe idadandaula za vutolo pamaliro mkati mwa sabatayi, idapempha boma kuti lidzionetsetsa kuti madalaivalawo akuyezedwa asadalowe mdziko muno, komanso adzikhala ku mbindikiro wa sabata ziwiri. Malo oyezera nthendayo mchigawo cha kumpoto adatsekulidwa Loweruka pa April 11 ndipo pofika pomwe timalemba nkhaniyi anthu osapitilira khumi ndiwo adayezedwa. Pa anthuwo, palibe adapezeka ndi nthendayo mchigawocho. Mneneri wa bungwe la National Oil Company of Malawi (Nocma), lomwe limabweretsa mafutawo, Telephorous Chigwenembe, adakana kulankhulapo pa zomwe akuchita madalaivalawo akafika mdziko muno. Dziko la Malawi nalo lili pa nkhondo yolimbana ndi matendawo. Pofika dzulo, anthu 33 ndi omwe adatsimikizika kuti akudwala matendawo, atatu adamwalira ndipo atatu ena adachira, kutanthauza kuti 27 ndi omwe akudwala matendawa. Maiko a Uganda ndi Kenya ndi ena mwa maiko omwe akudadandaula ndi madalaivala a galimoto zonyamula katundu. Mwachitsanzo, mdziko la Uganda, madalaivala awiri ochokera ku Tanzania apezeka ndi nthendayo Lachitatu msabatayi.
7
Luanar ikhazikitsa magulu a alimi akafukufuku Nthambi ya zaulangizi pasukulu yaukachenjede ya Lilongwe University of Agriculture and Natural Resources (Luanar) sabata zapitazo idakhazikitsa magulu a alimi a kafukufuku. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Magulu a alimiwa akhazikitsidwa ndi cholinga chopereka mwayi kwa alimi kuti atengepo mbali pa kafukufuku kuti apeze mayankho a mavuto omwe akukumana nawo paulimi. Kwa nthawi yaitali, alimi akhala akungolandira zotsatira za kafukufuku kuchokera kwa akatswiri a kafukufuku ndi alangizi. Izi zapangitsa kuti alimi azingolandira chilichonse kaya ndi chogwirizana ndi kudera kwawo kapena ayi kotero kukhazikitsidwa kwa maguluwa kuthandiza alimiwo kupeza mayankho a mavuto a ulimi mmadera awo. Ntchitoyi ndi ya zaka zinayi ndipo ikuchitika kudzera mupulojeketi ya Best Bets III ndi chithandizo chochokera ku McKnight Foundation. Magulu a alimi akafukufukuwa akhazikitsidwa mmadera a zaulimi a Zombwe mboma la Mzimba, Mkanakhoti ku Kasungu ndi Kandeu ku Ntcheu. Ena mwa alimi otenga nawo gawo pa chilinganizochi Malingana ndi yemwe akutsogolera ntchtitoyi, Daimon Kambewa, kwa nthawi yaitali alimi akhala akutengedwa ngati osadziwa chilichinse kotero akatswri akhala akupanga kafukufuku paokha ndi kumawauza alimi kuti atsatire zomwe apeza. Izi zachititsa alimi kumangotsatira zilizonse ndipo njira zina sizinathandize kutukula ulimi. Kutengapo mbali pa kafukufuku kuthandiza alimi kukhala ndi luntha ndi chidwi choganiza ndi kupeza njira zomwe zingawathandize kuthetsa mavuto awo paulimi mogwirizana ndi madera awo. Kwanthawi yaitali akatswiri a zaulimi akhala akupanga kafukufuku wawo paokha ndi kumawauza alimi zoti achite ndipo izi zapangitsa alimi kumangodikira alangizi kuti abweretse njira zatsopano za ulimi. Ntchito yopanga kafukufuku limodzi ndi alimi ithandiza kulimbikitsa kudzidalira komanso kukhala ndi luntha, luso ndi chidwi chithetsa mavuto a ulimi paokha, adatero Kambewa. Gulu lililonse lili ndi anthu 22 ndipo anthuwo asankhidwa ndi anthu a mmadera awo potengera chidwi chawo poyesera luso lamakono paulimi. Membala aliyense wa gulu akhala ndi munda wa chionetsero koma azikumana ndi kumakambirana nagawana nzeru. Alimiwa aziyenderana mminda ya wina ndi mnzake kuti aziphunzitsana ndi kumalimbikitsana. Ntchitoyi ikuyembekezeka kuthandiza alimi kukhala anthu oganiza mozama pofuna kuthetsa mavuto omwe akukumana nawo paulimi ndipo zichepetsa mchitidwe wodalira kapena kudikira alangizi kuti awauze njira zothetsera mavuto awo popeza alangizi alipo ochepa kuyerekeza ndi alimi.
4
AFORD Idzudzula Mlangizi wa President Chipani cha Alliance for Democracy AFORD chati ndi chokhumudwa ndi zomwe adayankhula mlangizi wa president pa nkhani za ndale a Francis Mphepo zoti adawudza mtsogoleri wa dziko lino Professor Arthur Peter Mutharika kuti asiye kuchita zitukuko chigawo chaku mpoto. Anthu sanamvetse bwino-Mphepo Muchikalata chomwe chipani cha AFORD chatulutsa ndipo chasayinidwa ndi Wofalitsa nkhani mu chipanichi a Khumbo Mwaungulu chati chipani chawo ndichokhumudwa ndi zomwe mkulu-yi analankhula Francis Mphepo. Tikudzudzula zomwe analankhula a Mphepo ponena kuti anthu a kumpoto ndi osayamika ndipo boma lisiya kutukula kumpoto. Mawu amenewa ndi opasula komanso obweretsa tsankho. Tikufuna apepese apo ayi tichitapo kanthu, anatero Mwaungulu. Koma mlangizi wa president pa nkhani za ndale a Francis Mphepo atsutsa idzi ndipo ati iwo sadayankhule zomwe akunena achipani cha AFORD. Anthu sanamvetse bwino zomwe ndinanena komanso ena azitanthauzira molakwika chifukwa President wathu ndi okonda mtendere komanso amakonda mzika iliyonse ya dziko lino ndiye ine sindingakambe zimene zili zosemphana ndi iyeyo, anatero a Mphepo.
11
Kudziwa za mthupi; kukonza tsogolo Sabata yatha inapatulidwa ndi boma pankhani yoyezetsa magazi kuti anthu adziwe ngati ali ndi kachirombo koyambitsa Edzi ka HIV. Mutu wa ntchitoyi chaka chino unali Yezetsani Magazi kuti Mukonze Tsogolo ndipo boma linalinga kuti lifikire anthu 250 000. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Pachithunzipa mukuona Mofolo Masulani wa zaka 32 yemwe amagwira ntchito yokonza panja ku Mandala mu mzinda wa Blantyre. Iye anatulukuka mkachipinda koyezetsera magazi kumsika wa Blantyre ali mweee kusekerera. Ndadziwa mmene ndiliri ndipo tsopano ndikwanitsadi kukonza tsogolo langa, iye anabwekera. Mkuluyu anati ali pabanja komanso ali ndi ana atatu ndipo aka kanali koyamba kuyezetsa magazi. Masulani amachokera ku Matindi mdera la Lunzu, makamaka mmudzi mwa Jamusoni kwa T/A Kapeni ku Blantyre. Wogwrizira udindo woyendetsa ntchito zolimbana ndi HIV Edzi mbomali, Rosemary Ngaiyaye, anati ntchitoyi inayenda bwino ngakhale zipangizo zina zinafika mochedwerapo kapena mochepera pa loto la ofesi yake.
6
Anthu a Mboma la Likoma Akufuna Bwanamkubwa Wawo Achoke Anthu ena omwe akuti ndi okhudzidwa mboma la Likoma alembera kalata boma kuti lichotse bwanamkubwa wa bomalo komanso mkulu owona za umoyo mbomalo. Anthuwa achita ziwonetsero ati posakondwa ndi momwe awiriwa akugwilira ntchito zawo mbomalo. Anthu okhudzidwa aku Likoma kuwerenga kalata ya madandaulo awo Mmodzi mwa anthu okudzidwawa a Mathews Manyuka awuza Radio Maria Malawi kuti bwanamkubwayu sakufotokoza bwino momwe agwiritsira ntchito ndalama zokwana 30 million-kwacha zomwe zimayenera kuthandiza polimbana ndi mliri wa Covid-19 komanso kuphatikizapo ndalama zina zochuluka zomwe zimayenera kugwira ntchito ya chitukuko mbomalo. Ziwonetserozi zikuchitika pa zifukwa ziwiri chomwe china ndi kusowa kwa bwana DHO mu ofesi yawo kuchokera pamene anatumizidwa kuti azizagwira ntchito mboma lino, komanso bwana DC alephera kutipasa malipoti ochulukwa okhuza chitukuko ndipo ngati mboma lino muli chitukuko ndi chomangidwa ndi a mission basi, anatero a Manyuka. Iwo ati akufuna anthuwa achotsedwe ntchito ndipo apatsidwe DC komanso DHO watsopano. Koma atafunsidwa, bwanamkubwa wa bomalo Eric Nema wakana kuyankhapo kanthu pa nkhaniyi ponena kuti anthu odandaulawa alembera kalatayi mabwana ake osati iyeyo monga bwanamkubwa wa bomalo.
11
Amangidwa popha anamapopa Ndende ya Nsanje ikusunga anthu awiri omwe akuyenera kuyankha mlandu wopha Landani Chipira wa zaka 48 atamuganizira kuti ndi namapopa mmudzi mwa Gulupu Mchacha James kwa T/A Mlolo mbomalo. Malingana ndi mneneri wapolisi ya Nsanje Agnes Zalakoma, anthuwa, omwe sadawatchule maina poopa kusokoneza kafukufuku wawo, adaonekera mukhoti Lachiwiri ndipo mlandu udzapitirira pa 20 October 2017. Koma kafukufuku wa Tamvani wapeza kuti awiriwo ndi gulupu ndi mfumu ina kumeneko. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka An artists impression of the arrest Zalakoma adati anthu a mmudziwo adakwiya ndi machitidwe a Chipira, yemwe anali mfumu Chizinga, ngati namapopa ndipo adamugenda mpaka kupha. Masana apa 28 September, anthu olusa adathyola nyumba ya mkuluyo ndi kumugenda. Kufika lero, tamanga anthu awiri powaganizira kuti akukhudzidwa ndi imfayo. Sitiwatchula maina awo kuopa okhudzidwa ena angathawe, iye adatero. Pa nkhani yomweyi, mneneriyu adati apolisi amanganso amayi awiri a mmudziwo, Chrissy Goba ndi Nota Tomas powaganizira kuti adafalitsa mauthenga abodza odzetsa mantha mwa anthu zomwe ndi zosemphana ndi gawo 60 la malamulo a zilango mdziko muno. Mbusa Danger Giant, wa mpingo wa Open Door mdera La Gulupu Mchacha James, adati chibwana chalanda ndipo anthu akudandaula chifukwa chotaya moyo wa mfumu pa mpheketsera chabe. Munthu wina mmudzi mwa malemuwa adati wapopedwa magazi ndiye ambiri adangoti mfumu ikudziwapo kanthu ndi kukayigenda. Chibwana ndi kuchita zinthu mchigulu zadzetsa chisoni mmudzimo, adatero Giant. Kumangidwa kwa awiriwo kudadza pomwe mtsogoleri wa dziko lino Peter Mutharika adadzudzula mchitidwe wopha anthu oganiziridwa kukhala a namapopa. Pamsonkhano wandale, Mutharika adakonza zokayendera maboma amene mchitidwewu wakula mchigawo chakummwera monga Mulanje, Phalombe, Thyolo ndi Nsanje. Mutharika adati: Ndakhudzidwa ndi zopopana magazi. Amalawi mitima ikhale pansi. Tiyenera kupewa kufalitsa nkhanizi chifukwa zilibe umboni ndipo nzopweteketsa anthu osalakwa. Anthu 7 aphedwa kale poganiziridwa kuti ndi anapopa zimene zachititsa dziko la United States of America komanso bungwe la United Nations kuchotsa ogwira ntchito ake mmadera okhudzidwa.
7
Papa Walimbikitsa Umodzi Pakati pa Zipembedzo Mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse Papa Francisco wati umodzi ndi ofunika pakati pa anthu a zipembedzo zosiyana-siyana. Malinga ndi malipoti a wayilesi ya Vatican Papa Francisco walankhula izi lachinayi, tsiku lomwe anthu a zipembedzo zosiyana-siyana anali ndi mapemphero opempha chithandizo cha Mulungu kuti mliri wa Coronavirus uthe. Lachinayi pa 14 May anthu a zipembedzo zosiyanasiyana pa dziko lonse la pansi anachita mapemphero opempha chithandizo cha Mulungu pa mliri wa Coronavirus. Mmawu ake pa tsikuli Papa Francisco watsindika za kufunika kwa umodzi pakati pa anthu onse angakhale asiyane zipembedzo ponena kuti anthu onse ndi ana a banja limodzi. Iye wati anthu akuyenera kupitiriza kupemphera kuti Mulungu amve kulira kwa anthu ake ndikuthetsa mliri wa Coronavirus ndipo wapitiriza kunena kuti aliyense ali ndi udindo poyetsetsa kuchitapo kanthu kuti mliriwu uthe. Papa Francisco wachenjeza kuti anthu omwe sadagwidwe ndi nthenda ya Covid 19 asanyadire kuti iwo ali pa bwino kapena kuti apulumuke koma akuyenera kuzindikira mavuto ena omwe mliriwu wabweretsa mwa chitsanzo pa nkhani ya maphunziro komanso chuma. Iye wati pambali pa mliri wa Coronavirus pali njala komanso nkhondo. Iye wati mavuto amenewa akusowa mapemphero a mphamvu kuti Mulungu achitire chisoni anthu ake. LaMulungu pa 3 May Papa Francisco adalengeza za mapemphero a zipembedzo zosiyana-siyana omwe achitika tsiku lachinayiwa pa 14 May potsatira ganizo la komiti yaikulu ya anthu ochokera ku zipembedzo zosiyana-siyana (Higher Committee of Human Fraternity) lomwe iye adavomereza loti pakhale mapemphero opempha chithandizo cha Mulungu kuti mliri wa Coronavirus womwe wakhudza dziko lonse la pansi uthe.
14
Aika mwala wa maziko kawiri pachipatala Kachikena: Banda kuyalanso mwala Lolemba msabatayi mtsogoleri wa dziko lino Joyce Banda adatsogolera anthu a mboma la Ntcheu pomwe amayala mwala wa maziko pa chipatala cha amayi apakati. Kuyala kwa mwalaku kumadza mkazi wa mtsogoleri wakale wa dziko lino Callista Mutharika atayalanso mwala wamaziko pamalopo mmbuyomu. Mutharika adalonjeza ndalama pafupifupi K18 miliyoni zomwe amati zimangire chipatalacho pomwe Banda adalandira K35 miliyoni kuchokera kukampani ya magetsi ya Escom yomwe imangire chipatalacho. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Malinga ndi mfumu ina ku Ntcheuko yomwe siidafune kutchulidwa dzina, Mutharika atayala mwalawo ntchito yomanga chipatalacho idayambika. Mwala wa maziko udadzayalidwa kale, tangodabwa winanso wamaziko ukubwera, timaganizatu kubwera chipatala osati mwala. Ntchito yomanga chipatalacho idayambika kale moti apapa komwe kunamangidwako kwagumulidwa kuti ntchitoyo iyambirenso, idatero mfumuyo. Koma mkulu wa bungwe loona zaumoyo la Malawi Health Equity Network (MHEN) Martha Kwataine wati payenera kukhala kafukufuku kuti ndalama zomwe adalonjeza Mutharika adalonjeza zidalowera kuti ntchitoyo iyime. Ntchitoyi ndi ya Amalawi eni osati munthu, apapa timvetse komwe kudapita ndalamazo nanga zagwira ntchito yanji. Ngati ntchitoyo idayambidwa zakhala bwanji kuti boma ligumule kudayambidwako mmalo moti angopitiriza? Izi zifufuzidwe, adatero Kwataine. Patsikulo phungu wa kumadzulo mboma la Ntcheu Chikumbutso Hiwa komanso Nduna ya za Umoyo Catherine Gotani Hara pamodzi ndi Banda adatengetsa Mutharika polephera kumalizitsa chipatalacho. Sindikufuna ndiyambe kutsatira chomwe chidachitika kuti chipatalachi chisamalizidwe koma kuonetsetsa kuti zomwe anthu amayembekezera zakwaniritsidwa, adatero Banda. Koma Kwataine adati si bwino ntchito zomwe zipindulire anthu kumazilowetsa ndale ponena kuti zotere sizingapititse Malawi patsogolo.
6
Ma CBO Mboma la Zomba Adandaula ndi Kutsekedwa Kwa Sukulu Mgwirizano wa mabungwe angono angono Community Based Organizations Network mdera la mfumu yaikulu Mwambo mboma la Zomba wati kuyimitsidwa kwa sukulu chifukwa cha mliri wa Coronavirus mdziko kwachititsa kuti maphunziro asokonekere. Mlembi wa Mwambo CBO Network mboma la Zomba a Josamu Stephano ndi omwe ayankhula izi pa mkumano wa mabungwewa komwe amakambirana zolimbikitsa ntchito yoteteza ana a mdelaro. A Stephano ati chifukwa cha kubwera kwa Coronavirus, ana ambiri atayilira kaamba koti akuganiza kuti sadzabweleranso ku sukulu ndipo ati padakalipano ana ambiri atenga mimba komanso ena akwatiwa kale. Maphunziro ku dela lathu kuno asokonekera kamba koti ana ambiri tili nawo mmakomo ndiponso ana ambiri atayilira, anatero a Stephano. Iwo adandaula kuti sukulu zikazatsegulidwa ana ambiri sazabwerera kamba koti ena akwatiwa ndipo ena mwaiwo atenga mimba. Poyankhulapo mmodzi mwa membala wa Mwambo Community Based Organization Network mayi Ethel Banda ati maphunziro ana ambiri a mderalo ayamba kupezeka ku malo omwera mowa komwe akuchita uhule. Dziko la Malawi lakhuzidwa kamba koti ana ambiri maphunziro abwerera mmbuyo ndipo atenga mimba pomwe sukulu imatilerera ana, anatero mayi Banda.
3
Akana kulemba UTM Akatswiri pa nkhani za ndale ati mlembi wa zipani sadalakwitse pokana kulemba UTM ngati chipani mdziko muno. Wachiwiri kwa mlembi wa zipani Chikumbutso Namelo adakana kulowetsa mkaundula wa zipani gulu la United Transformation Movement(UTM) lomwe likutsogoleredwa ndi wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino Saulos Chilima. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Mtsogoleri wa UTM: Chilima Mchikalata chopita ku UTM kuchokera ku ofesi ya mlembiyi, Namelo adakana kutero chifukwa gululo lidapempha kugwiritsa ntchito dzina la UTM mmalo mwa dzina lonse la United Transformation Movement. Mkalatayo Namelo adati kugwiritsa ntchito dzina la UTM nkungofuna kubalalitsa ofesi ya mlembiyi chifukwa palinso kale chipani china chotchedwa United Transformation Party (UTP). Ndipo posakhutira ndi chiganizochi gulu la UTM latengera nkhaniyi ku bwalo la milandu kuti awunike bwino malinga ndi mneneri wa chipanich Joseph Chidanti Malunga. Koma poperekapo maganizo ake, katswiri pa nkhani za ndale wochokera pasukulu ya ukachenjede ya University of Livingstonia (Unilia) George Phiri adagwirizana kwatunthu ndi ofesi ya mlembi wa zipani kuti kulowetsa mkaundula wa zipani dzina la UTM kukadabweretsa chipwirikiti. Phiri adati vuto lagona poti nthawi zambiri mkaundula mumafunika kulowa dzina lonse osati lachidule ayi popangira zokudza pa mawa monga kumangidwa kapena kumanga ena. Nchifukwa chokwanira kusawalowetsa mkaundula chifukwa kwa mlembi wa zipani kukhonza kukhala UTM, iwo kunjako nkumagwiritsa ntchito United Transformation Movement zomwe zikhonza kubweretsa chisokonezo, adalongosola motero Phiri. Iye adati koma vutoli ndi lalingono ndipo likhonza kukonzedwa mosavuta posagwiritsanso ntchito mabwalo a milandu. Ngakhale sindine loya, ndikhonzabe kunena kuti amangoyenera kukhala pansi ndi kuunikanso dzinalo ndi kukonza pali vutopo ndikukaperekanso zikalata zina chifukwa kubwalo la milandu kukhonza kungochedwetsa zinthu, adatero Phiri. Pogwirizana ndi Phiri naye Chimwemwe Tsitsi yemwe ndi mphunzitsi kusukulu yaukachenjede ya Polytechnic adati zifukwa zomwe adapereka mlembi wa zipani zidali zomveka bwino potengera malamulo a dziko lino ndi zovuta kulembetsa chipani chomwe chili ndi dzina lofananilako ndi chomwe chidalembetsedwa kale. Sitikudziwa kuti a UTM adaganizapo bwanji chifukwa pachiyambi adauza Amalawi kuti aphatikizana ndi chipani cha UTP chomwe mtsogoleri wake ndi Newton Kambala ndipo angochotsa P ndikuikapo M. Koma pano tikuona akukalembetsa ngati UTM, adadabwa Tsitsi. Iye adati gulu la UTM likuyenera kukhala pansi nkuunikapo bwino komanso kupeza upangiri kwa akatswiri amalamulo pa nkhani ya dzinali. Akuyenera kupanga izi mwamsanga chifukwa nthawi yawathera kale, adalongosola Tsitsi. Ngakhale adaonjezera kuti gulu la UTM likhonza kuona kuvuta kusintha dzina chifukwa cha katundu monga galimoto ndi zovala zomwe zalembedwa mdzinali ndipo kusinthaku kungakhale kodula.
11
Mapemphero a mvula aliko lero Pamene ngamba yadzetsa chikaiko choti Amalawi akhoza kukolola zochepa chaka chino, mtsogoleri wa dziko lino Peter Mutharika lero akhala nawo pa mapemphero a mvula amene achitike mumzinda wa Lilongwe. Malinga ndi mlangizi wa Mutharika pa za chipembedzo Timothy Khoviwa, mapempherowo akhalanso othokoza Mulungu pa zochitika za chaka chatha. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Mutharika led Malawians in prayer Mapempherowo akachitikira ku Bingu International Conference Centre (BICC) pansi pa mfundo yaikulu yakuti Kudzipereka kwa Mulungu posinkhasinkha mtendere ndi chitukuko cha dziko. Tikakhalanso tikupempha Mulungu kuti atipatse zokolola zokwanira mu 2016. Kuli atsogoleri a mipingo yosiyanasiyana. Iyinso ndi nthawi yakuti a zipembedzo zosiyanasiyana akhalire pamodzi, adatero Khoviwa. Mapempherowa akudza pomwe nthambi yoona za nyengo idati kudula kwa mvula kwa sabata ziwiri kwadzetsa chikaiko pakati pa alimi ndi Amalawi ena onse. Mneneri wa nthambiyo Ellina Kululanga adati kudulaku kwadza chifukwa cha nyengo ya El Nino imene ikuchititsa kuti madera a mchigawo cha kumwera mugwe ngamba pomwe kumpoto ndi pakati chiyembekezo chilipo kuti mvulayi igwa bwino. Malinga ndi kafukufuku wa nyuzipepala ya The Nation, madera ambiri mvula siyikugwa bwino zimene zingachititse kuti zokolola zichepe. Izi zikudza pomwe mchaka cha 2015 zokolola zidatsika ndi makilogalamu 30 pa makilogalamu 100 alionse chifukwa cha vuto la madzi osefukira amene adakokolola mbewu zambiri.
13
Amati aukitsa wakufa koma athera mzingwe Mudali fumbi mmudzi mwa Mpheziwa kwa T/A Kasumbu mboma la Dedza posachedwapa pamene khwimbi la anthu lidakhamukira mmudzimo kukaonerera ntchito ya asinganga atatu omwe amati atha kuukitsa wina kwa akufa. Mapeto ake awiri mwa atatuwa adathera mmanja mwa apolisi ndipo pano akuyankha mlandu wopanga upo wofuna kuchita chinyengo pamene wachitatuyo adati phazi thandize ndipo mpaka pano apolisi akumusakasakabe. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Gulupu Chinyamula, mkazi wa malemuyo ndi mneneri wa polisi ya Dedza, Edward Kabango, atsimikiza za nkhaniyi. Malinga ndi Kabango, oganiziridwawo ndi Gift Phiri, Jemitala Alfred, komanso wina amene akungodziwika ndi dzina loti Masambaasiyana. Atatuwa akuti amadzithemba kuti ali nayo mphamvu youkitsa munthu kwa akufa ndipo adati ngati anthu ali ndi chikaiko aonera pa Evance Bunya, yemwe adamwalira pa 15 May chaka chino atadwala mutu kwa sabata imodzi. Mkazi wa malemuyo, Rose Bunya, adauza Msangulutso Lachinayi lapitali kuti asingangawo adabwera ndi mnzake wa mayiyu yemwe amati amathandiza kuukitsa munthu kwa akufa. Gunya adati, Iwo atabwera adandiuza kuti malemu amunanga adachita kusowetsedwa mmatsenga kotero ngati ndingafune atha kupanga mankhwala ndipo angathe kubwera nkukhalanso moyo. Koma ngakhale asingangawa amati malemuyo adachita kusowetsedwa mmatsenga, Gunya adati mwambo wonse wa maliro udayenda bwinobwino ndipo mwamuna wake adakaikidwa kumanda monga achitira ndi maliro onse. Gulupu Chinyamula, yemwe amayanganiranso mudzi wa Mpheziwa, adati asingangawo adatchaja ndalama pafupifupi K400 000 ngati akufuna kuti malemuyo abwere komwe amati adamupititsako mmatsenga. Mmudzimo anthu adali kalikiriki kusonkherana, apa nkuti ine kulibe, ndipo adapeza ndalama zoposera K200 000 zomwe akuti adachita kukongola kwa anthu pamene zina zidaperekedwa ndi achibale a malemuwo, adatero Gulupu Chinyamula. Akuti asingangawo adakana kulandira ndalamayo ponena kuti yachepa ndipo mayi Bunya adaperekanso wailesi. Apa mpomwe akuti asingangawo adawatsimikizira kuti malemuyo atulukira. Malinga ndi Kabango, pa 31 July wapitayu ndilo tsiku lomwe oganiziridwawa amati achite matsengawo kuti wakufayo atulukire pamaso pa abale ake dzuwa likuswa mtengo. Anthu adasonkhana ndipo kudali zoimba, komanso kudakonzedwa zakudya kuti anthu adye uku akudikira kuti malemuyo atulukire. Mosakhalitsa, kudatulukira asinganga awiri ndipo adafunditsa nsalu munthu mmodzi amene amati ndi wouka kwa akufayo. Adamulowetsa mnyumba ya malemuyo ndipo adati ngati munthu akufuna kukamuona bamboyo alipire K1 000, adatero Kabango. Koma mwambowu akuti udasokonekera pamene Gulupu Chinyamula adamva za nkhaniyi. Ngakhale amanamiza anthu kuti angathe kuukitsa munthu kwa akufa, ine sindidakhulupirire ndiponso amalephera kufotokoza bwino kuti anthu akhulupirire. Ndiye ndidangowathira zingwe ndi kuitana apolisi kuti adzawatenge, adatero Chinyamula. Kabango watsimikizira zakunjatidwa kwa Phiri ndi Alfred ndipo wati apolisi akusakasakabe Masambaasiyana yemwe akumuganizira kuti ndiye amatsogolera zochitikazo. Masambaasiyana akuganiziridwanso kuti ndiye adalandira ndalamazo, ndiye kafukufuku ali mkati, adatero Kabango. Kabango adati omangidwawa atsekuliridwa mlandu wopanga upo wofuna kuchita chinyengo. Iwo akuti adaonekera kubwalo la milandu Lachitatu pa 12 August koma akhoti awapatsa belo.
19
Atenge basi ndani? Matimu a Nyasa Big Bullets ndi Mighty Be Forward Wanderers Lolemba akhala akukumana pampikisano wa Basi Ipite Soccer Fiesta wolimbirana minibasi ya K25 miliyoni pa Kamuzu Stadium mumzinda wa Blantyre. Mkulu wa Luso TV Dick Juma Lachinayi adati basiyo, imene idafika mdziko muno Lachinayi, ipitirira kusungidwa ndi bungwe la Football Association of Malawi (FAM) mpaka wopambana apezeke. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Ilowera kwa ndani?: Wachiwiri kwa wapampando wa Bullets (kumanzere) Austo Kasito ndi Christo Kananji wachiwiri kwa mlembi wa Manoma Basi ndi imeneyi yafika lero ndipo mawa (Lachisanu) ikaperekedwa mmanja mwa FAM kuti ayisunge, adatero Juma. Iye adati adasankha matimuwa kaamba ka mavuto a mayendedwe omwe ali nawo ndipo akufuna kupereka mwayi woti opambana adziombole kumavutowa.
16
Alimi otsogola amasamalira nthaka Chuma chili mu nthaka, komatu sichipezeka mu nthaka yosakazidwa. Kusasamala za chilengedwe monga mitengo kukupangitsa kuti nthaka iziguga. Izitu zikusautsa alimi chaka chilichonse potaya nthawi ndi ndalama zawo mminda yokanika kupereka zipatso zoyenera. Ngakhale zili chonchi, alimi ena akusimba lokoma chifukwa minda yawo ili ndi mphamvu zogonera. Mmodzi mwa alimiwa ndi Joseph Khoswe wa mmudzi mwa Matipa mu Chingale EPA mboma la Zomba yemwe akubwekera dongosolo losamala nthaka ndi akalozera. TEMWA MHONE adacheza ndi Khoswe motere: Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Alimi ena mu Chingale EPA ku Zomba kuunga mlambala pansi pa chingwe cha kalozera Panopa tiziti kwacha moti alimi azipita ku munda? Eya. Ulimitu ulibe tchuthi. Kudacha kalekale titakolola mu April. August ndi mwezi wogalauza apo ndi apo. Lingaliro lokonza minda mvula ikayamba kapena masabata awiri isadagwe likuchititsa ulimi mdziko muno kukhala wovuta. Chizolowezichi chimayipitsa mbiri ya ulimi pomaganiza kuti ulimi ndi magobo chifukwa timachita zinthu zambiri mu nthawi yochepa pothamangitsana ndi mvula. Mukuukokomezatu ulimi mpaka levulo ku munda? (Akuseka) Pomwe pali chuma palibe kusewera. Ulimi ndi bizinezi yodalira nthaka yomwe timayenera kuyisamala chaka chonse. Pambali pa mavuto odza ndi kusintha kwa nyengo, mugwirizana nane kuti ambiri ulimi ukuwakanika chifukwa minda idaguga ndipo mbewu sizikubereka moyenera. Levuloyi (yogwiritsa ntchito amisili omanga nyumba poyala njerwa) ndi chimodzi mwa zida zokonzera akalozera oteteza nthaka. Zina ndi zikhomo, chikwanje, chingwe cha mamita 5, mitengo (ndodo) iwiri yotalika mamita 1.6 mpaka 2.0 ndi hamala. Akalozera ndi chani? Ndi dongosolo lopezera kayendedwe ka madzi mmunda ndi cholinga chokonza mizere yoteteza nthaka. Mwachitidwa akalozera timaungamo milambala yomwe imateteza nthaka pochepetsa kuthamanga kwa madzi mmunda. Mizere yonse yotsatira imalunjika mlambalawo. Potengera kutsika kwa malo, akalozera kapena milambala imene imatalikana 5 kapena 10 mitazi mmunda. Mumakonza motani akalozera? Timafunika anthu atatu. Awiri aima ndi ndodo zomangidwa chigwe chija ndipo ine ndikhala pakati ndi levuloyi kuyeza. Malo omwe timadzi mu levulo tabwera pakatikati wa kumapeto amaika chikhomo ndi kusunthira komwe kuli ndime. Timatero mpaka munda wonse uthe. Dongosololi ndi lofunika bwanji mmunda? Kuteteza nthakako ndiye kuti chonde sichikokoloka, komanso amathandiza chinyezi kukhalitsa mmunda polowetsa madzi okololedwawo pansi. Ndi yankho ku vuto la ngamba ndi kuguga kwa nthaka monga madongosolo ena ophimbira, ngonyeka (box ridges), ulimi wa mmaenje ndi maswale. Mwapindula motani ndi akalozera? Chajira kaya muti chonde mmunda mwanga ndi chogonera. Kukagwa ngamba, ndi maonera kufoota kwa mbewu za alimi ochita chisawawa poti mwanga chinyezi chimakhalitsanso. Zokolola ndi kholophethe mpaka ndidasankhidwa kukhala mlimi wachitsanzo kumbali ya akalozerayi.
4
Amabungwe akukonzanso zogwirira ntchito limodzi Pozindikira kuti mutu umodzi susenza denga, mabungwe omwe si aboma omwe akugwira ntchito zosiyanasiyana mdziko muno, kuphatikizapo za maufulu a anthu komanso kayendetsedwe ka boma, ati ali ndi cholinga chokhazikitsa ndi kulimbikitsa mgwirizano pakati pawo kuti azitha kugwira ntchito limodzi pofuna kutumikira mtundu wa Amalawi pa zofuna zawo. Mmodzi mwa akuluakulu a mabungwe omenyera ufulu wa anthu ndi kudzudzula zolakwika pakayendetsedwe ka zinthu, McDonald Sembereka, adatsimikizira Tamvani kuti mabungwe angapo avomera kale kulowa nawo mumgwirizanowu ndipo posachedwapa uyamba kugwira ntchito yake. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Cholinga chathu nchimodzi basi monga oyimirira Amalawi kuonetsetsa kuti zinthu zikuyenda bwino ndipo Amalawi sakuvutika kapena kuphwanyiridwa maufulu awo osiyanasiyana. Taganiza izi poona momwe zinthu zayamba kuyendera mdziko muno, adatero Sembereka. Koma katswiri wa zamalamulo ndi ndale Blessings Chinsinga wati zomwe akulingalira mabungwewa zingatheke pokhapo atasintha khalidwe ndi magwiridwe a ntchito zawo kuti athe kuongolera ndi kudzudzula kayendetsedwe ka zinthu mdziko muno. Tamvani itamufunsa maganizo ake pa lingaliro la mabungwewa, Chinsinga adati ngakhale ganizoli ndi labwino pachitukuko ndi tsogolo la dziko lino, mabungwewa ali ndi ntchito yaikulu yomema Amalawi kuti awakhulupirirenso potengera momwe zinthu zakhala zikuyendera mmbuyomu. Ndi ganizo labwino koma lovuta kukwaniritsa chifukwa kuyamba nkuyamba, pali kusagwirizana pakati pa mabungwe eni ake. Izi mukhoza kutsimikiza potengera momwe ntchito za mabungwewa zakhala zikuyendera, makamaka pokonza zionetsero, adatero Chinsinga. Iye adati Amalawi ambiri adataya chikhulupiriro kuchokera mchaka cha 2011 pomwe atsogoleri a mabungwe adamema zionetsero za dziko lonse koma mapeto ake anthu ena adaphedwapo ndipo patangopita nthawi pangono mabungwewa adakhala chete. Zionetsero za 2011 ndizo zidali nsanamira yaikulu ya mabungwe yosonyeza mphamvu, kugwirizana ndi mtima wofunadi kuthandiza, koma zomwe zidachitika zija zidagwetsa anthu ulesi waukulu moti pano ambiri alibenso nazo chidwi [zochita za amabungwewa], adatero Chinsinga. Iye adati chofunika apa nkuyamba apanga mfundo imodzi yomwe ingaonetse kuti cholinga chawodi nchimodzi, apo ayi, palibe chomwe angapindulepo. Koma Sembereka wanenetsa kuti mgwirizano wa ulendo uno ukhala wosiyana ndi migwirizano ina yonse mmbuyomu kaamba koti mfundo zake zikhala zakupsa ndi zomanga komanso zotengera maganizo a anthu ndi kudalira zokambirana mmalo mongolozana zala. Amalawi ena omwe alankhula ndi Tamvani ati chimawagwetsa ulesi kwambiri nchakuti atsogoleri a mabungwewa sachedwa kutembenuka akalonjezedwa kapena kupatsidwa maudindo mboma lolamula. Lameck Silungwe wa ku Chitipa adati nzokhumudwitsa kuti amabungwe amakokomeza kuti iwo ndi omenyera ufulu anthu ndi kudzudzula pomwe boma likulakwitsa koma mapeto ake amaoneka ngati iyi ndi njira yopemphera maudindo mboma. Ndi atsogoleri angati a mabungwe omwe adapereka chiyembekezo mwa Amalawi kenako nkutseka pakamwa Amalawiwo akuwafuna kwambiri? Ndi ochuluka oti mwina enafe sitingathe kuwalakatula onse. Zimenezi ndizo zimagwetsa ulesi, adatero Silungwe. Masozi Banda wa mboma la Nkhata Bay naye adati adali ndi chiyembekezo chachikulu kuchokera kwa amabungwe pa zomwe adachita mchaka cha 2011, koma kenako adaona ngati wagwiritsidwa ntchito nkutayidwa ngati wopanda phindu. Anthu ambiri tidalolera kupita kukapanga zionetsero mmizinda chifukwa cha chikhulupiriro koma patangotha miyezi yochepa chabe, atsogoleri ambiri adayamba kulowera kosiyanasiyana kutisiya manja ali mkhosi, adatero Banda. Naye Manuel Sajiwa wa mboma la Lilongwe adati akhoza kutsatira mabungwewa pokhapokha ataonadi kuti pali cholinga chenicheni osati kufuna kupanga phokoso longolambulirapo njira yopezera maudindo. Zimayamba chonchi, amabwera pangonopangono nkumatitsimikizira kuti akudzatitsogolera kuti timenye nkhondo ya ufulu wathu koma posakhalitsa umangomva kuti anthu ochepa, makamaka iwowo, ali mmaudindo kenako zii, adatero Sajiwa. Zitachitika zionetsero za 2011 zomwe adatsogolera akuluakulu a mabungwe oima paokhawa, anthu ambiri adaphedwa pazipolowe zomwe zidabuka pakati pa apolisi ndi anthu pomwe apolisi adaletsa anthu kuononga katundu wa eni. Patangotha miyezi yochepa chichitikireni izi, atsogoleri ena a mabungwe adapatsidwa maudindo mboma latsopano la PP ndipo izi zidakhalangati zasokoneza mgwirizano wa mabungwewa omwe adayamba kugwira ntchito paokhapaokha. Ena mwa akuluakulu a mabungwe omwe adalandira maudindo kuchoka mchaka cha 2011 ndi Sembereka, yemwe adapatsidwa udindo wa mlangizi wa pulezidenti pankhani za mabungwe mboma la Joyce Banda wa chipani PP; Dorothy Ngoma, womenyera ufulu yemwe adapatsidwa udindo woyanganira za uchembere wabwino mboma lomwelo la PP; ndipo mboma latsopano la DPP, mmodzi mwa amabungwe omwe adakhala chete atapatsidwa udindo ndi Mabvuto Bamusi, yemwe ndi mlangizi wa Pulezidenti pa zamabungwe omwe si aboma.
11
UDF yalonjeza za chiyambi chatsopano Chipani cha United Democratic Front (UDF) chanenetsa kuti chidzapitiriza kutukula ntchito za ulimi, maphunziro komanso umoyo wa anthu mdziko muno chikalowa mboma pa 21 May. Izi zanenedwa Lamulungu pamene Atupele Muluzi amakhazikitsa manifesito ya UDF yomwe mutu wake ndi Chiyambi Chatsopano. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Mkamanga: Sakufotokoza bwino mwinano Kumbali ya ulimi, manifesitoyo ikuti UDF idzamanga nkhokwe za mmadera zomwe zizidzasamalidwa ndi anthu amene akukhala kuderalo. Koma katswiri pa ndale mdziko muno, Emily Mkamanga watsutsa zakuthekera kwa mfundoyo ndipo wati chipanicho sichidafotokoze bwino mmene nkhokwezo zidzamangidwire. Sakufotokoza bwino madera amene adzapindule komanso mbewu zomwe chipanicho chikufuna kuti Amalawi azidzasunga mnkhokwezo. Tonse tikudziwa kuti mbewu zambiri zimaonongeka kale mnkhokwe, kodi zomwe anthu adzasungezi zidzasamalidwa bwanji? adatero. UDF yati idzasintha mbewu zina zomwe alimi amadalira pa chuma ndi chakudya monga fodya ndi chimanga kupita ku mbewu zina koma sichidafotokoze bwino za misika ya mbewuyo. Chipanicho chati Amalawi adzapitiriza kugula zipangizo zotsika mtengo ngati angachisankhe kuti chilowe mboma. UDF yatinso idzaonetsetsa kuti pulogalamu ya zipangizo zotsika mtengozo ikupindulira anthu akumudzi komanso osaukitsitsa ngati njira imodzi yothana ndi njala. Pa mfundo iyi Mkamanga adati ndondomekoyo sionetsa phindu lenileni kwa alimi chifukwa chinyengo chidalowererapo. Iye adati ndi bwino kuti ndondomekoyo ithetsedwe kuti pangokhala mtengo umodzi wa zipangizo za ulimi kuti aliyense azipindula. Pa nkhani ya maphunziro, chipanicho chati chidzaonetsetsa kuti aphunzitsi alipo ochuluka makamaka msukulu zomwe zili mmadera a kumidzi komanso kuti atsikana azikhala pa sukulu mpaka atakwana zaka 15 ndi cholinga chothana ndi maukwati a ana. UDF yati idzapanga ubale ndi mabungwe osiyanasiyana kuti athandizepo pa maphunziro awo. Kumbali ya umoyo, chipanicho chati chidzamanga zipatala mmizinda ya Blantyre, Lilongwe ndi Mzuzu poonjezera pa zipatala zazikulu zomwe zilipo kale. Ngati zipani zina, UDF yalonjezanso kudzapeza njira zina za mayendedwe zomwe zidzalumikize dziko lino ndi maiko ena mu Africa.
11
anatchezera Akundidabwitsa Anatchereza, Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Ndili pa chibwenzi ndi mwamuna wina. Chomwe chimandidabwitsa nchoti nthawi zonse ndikamuimbira foni usiku samayankha. Ndikamufunsa amati idali kotchajitsa. Gogo ndikuona ngati mwamunayu akundiyenda njomba ali ndi mkazi wina ndipo akuopa kuti akayankha amudziwa kuti ali ndi chibwenzi. Ndithandizeni, PK, Ndirande, Blantyre. PK, Ndikadakuthandizani mokwanira ndikadziwa kuti chibwenzi chanu chidayamba bwanji. Nanga mwakhala zaka zinga muli pa chibwenzi? Nanga mwamunayo ali ndi wa zaka zingati? Amakhala kuti? Ndindani? Nanga amachita chiyani? Ndalankhula izi kaamba koti ndikuona ngati simukumudziwa bwino. Nthawi zambiri atsikana ambiri safufuza mokwanira asanamulole mwamuna makamaka munthuyo akakhala wachikulire. Zotsatira zake amakagwa mchikondi ndi mwamuna wa mwini wake zomwe zimaika pachiopsezo miyoyo ndi tsogolo lawo. Ndikupempheni kuti mumufufuze bwino mwamunayu ndi kupeza zoona zake musadachite chilichonse. Chitani izi mwachangu kuopa kudzanongoneza bondo mtsogolo. Natchereza Ndithandizeni Gogo Natchereza Ndidakumana ndi mtsikana wina yemwe nditamuona mtima wanga udakhutira kuti ndi mkazi amene ndimafuna atakhala mayi wa ana anga. Takhala tikuimbirana foni, komanso kuyenderana kwa zaka ziwiri. Koma chodabwitsa nchoti ndikamufunsira amakana. Ndikamufunsa chifukwa chomwe wakanira safotokoza. Gogo, ndithandizeni. Mtsikanayu ndimamukonda, ndiwokongola, waulemu, wochezeka, komanso wodzilemekeza. JKJ Mchinji JKJ Chikondi chimapilira, chimaleza, komanso sichipsa mtima. Mpatseni nthawi mtsikanayu mwina mtsogolo muno zidzayenda. Ndikadakonda mudafufuza mbiri yake. Atsikana ena amaopa kukwatiwa kapena kukhala pa chibwenzi chifukwa cha zomwe adakumana nazo kapena anzawo ndi abale awo adakumana nazo. Kambiranani mwina atha kumatsuka nkukuuzani chomwe chimamuchititsa. Natchereza Ofuna banja Ndikufuna mkazi womanga naye banja. Akhale wa zaka za pakati pa 30 ndi 39, wopemphera, koma yemwe adapezeka ndi kachilombo ka HIV. 0883164130/ 0995268735 PPX Ndikufuna mkazi Ndithandizeni ndikufuna mkazi. Ndine mnyamata wa zaka 34 ndipo ndimachita bizinesi. Mkaziyo ayimbe foni iyi 0991 711 433.
12
Chisankho Chayambika Mdziko La Mozambique Wolemba: Thokozani Chapola s/2019/10/nyusii.jpg 303w" sizes="(max-width: 605px) 100vw, 605px" />President Nyusi kuponya voti yake Anthu a mdziko la Mozambique lero ayamba kuponya voti pofuna kusankha mtsogoleri wa dzikolo komanso aphungu a kunyumba ya malamulo. Malipoti a wailesi ya bbc ati anthu oposa 13 million ndi omwe ali ovomerezeka kuponya nawo votiyi. Mtsogoleri wa dzikolo Fillipe Nyusi yemwe akuyimira chipani cha FRELIMO chomwe chakhala chikulamulira dzikolo chitengereni ufulu wodzilamulira kuchoka ku dziko la Portugal mchaka cha 1975, akupikisana nawonso pa chisankhochi pomwe akufuna kuti asankhidwe kulowa teremu yake ya chiwiri pa udindowu. Malipoti ati gulu lomwe linali la nkhondo ndipo padakalipano linasanduka chipani chotsutsa cha RENAMO chadzudzula kale chipani cha FRELIMO kuti chikufuna kubera mavoti pa chisankhochi. Padakali pano president Nyusi wapempha anthu kuti apewe ziwawa pa chisankhochi.
11
Kuphunzira chingerezi tsono chiziyambira mSitandade 1 Kanyumba: Nduna ya maphunziro Angapo mwa makolo mdziko muno ati ndi okondwa ndi ndondomeko yatsopano yomwe unduna wa maphunziro mdziko muno wakhazikitsa kuti ana msukulu za boma ayamba kuphunzira mChingerezi kuyambira Sitandade 1 pamaphunziro onse kupatula Chichewa. Pocheza ndi Tamvani, makolo angapo mmadera osiyanasiyana ati ana asukulu akhala akulephera kuyankhula Chingerezi chothyakuka kaamba koti sasulidwa mokwanira kusukulu. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Chingerezi ndi chiyankhulo chofunikira kwambiri kupatula Chichewa, Chitumbuka ndi ziyankhulo zina mdziko muno. Rodrick Savamkunkhu wa ku Chinsapo ku Lilongwe, yemwe ali ndi ana onse awiri kupulayimale ndipo winayo ndi wa Sitandade 1 pa Chinsapo wati: Ili ndi ganizo labwino kwambiri chifukwa anawa akhala akuphunzira kuyankhula chiyankhulochi akadali achichepere pamaphunziro. Savamkunkhu wati ophunzira okhawo omwe amaphunzira sukulu zapamwamba zomwe si zaboma ndiwo amakhala ndi mwayi wophunzira Chingerezi mozama poti amayambira kalasi yoyamba kuphunzira maphunziro onse mChingerezi kupatula Chichewa. Nayo Ellen Mwafulirwa wa ku Dwangwa mboma la Nkhotakota alandira nkhaniyi ndi manja awiri ponena kuti ichotsa kunyazitsa komwe ophunzira amasiku ano amabweretsa akamayankhula Chingerezi chothyokathyoka. Izi zili bwino, mwina nkuchepetsako Chingerezi chomvetsa chisoni chomwe ana athu amayankhula, watero Mwafulirwa. Koma Charity Kandikole, wochokera ku Balaka, wati ngakhale ndondomekoyi ili bwino makolo agwirane manja ndi boma poonetsetsa kuti aphunzitsi akutsatadi ndondomeko imeneyi. Nduna ya zamaphunziro Lucius Kanyumba yati ndondomekoyi iyamba kutsatiridwa mchigawo cha maphunziro chomwe chikubwerachi. Ndi khumbo la boma kuona ophunzira akuyankhula ndi kulemba Chingerezi chabwino, watero Kanyumba.
3
MCP Yalimbikitsa Mgwirizano Pakati Pa Achinyamata Ndi Mavenda Ku Zomba Mkulu wa achinyamata mchipani cha Malawi Congress (MCP) mchigawo chaku mmawa, Ramsey Khan walimbikitsa mgwirizano pakati pa achinyamata otsatira mgwirizano wa Tonse ndi mavendor a mu mzinda wa Zomba. Khani wayankhula izi lachitatu ku Domino Lodge mu mzinda wa Zomba pomwe anakonza phwando posangalala kuti mgwirizano wa Tonse wapambana pa chisankho. Iye wati achinyamata ayembekezere kuti miyoyo yawo isintha popeza kuti adzichita ma business osiyanasiyana kaamba koti iwonso ndi omwe anathandizira kuti Tonse Alliance ipambane. Mavenda amenewa amu Zomba ndi amene anagwira ntchito yotamandika kuti chipani chathu chipambane. Anthu amenewa ndi amene apangitsa kuti zinthu zisinthe ndipo zasinthadi. Fetereza wa 4 sauzande wabwera, ngongole zija zafikanso chifukwa cha anthu amenewa, anatero Khani. Poyankhulanso mmodzi mwa anthu ochita business mboma la Zomba yemwenso ndi wapampando wa chipani cha Peoples (PP) mu msikawo, a Ayatu Chidothe anati ma Vendor amu mzindawu chomwe akufuna ndi chitukuko popeza kuti nthawi ya misonkhano yokopa anthu inatha. Amati MCP singalamulire dziko lino koma anayiwala kuti Mulungu ndi amene amayika munthu pa mpando kapena kumuchotsapo ndipo zatheka, anatero a Chidothe.
11
Zimbalangondo zikhapa achitetezo Gondwa: Tifufuze kaye Anthu akugona khutu lili kunja, tulo tayamba kusowa, chitetezo chatekeseka ku Soche mumzinda wa Blantyre komwe zimbalangondo zatikita achitetezo a mderalo la neighborhood watch ndi kuvulaza mmodzi modetsa nkhawa. Izi zachitika usiku wa sabata yathayi Lachiwiri nthawi ili 2 koloko anthu akupha tulo. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Zidalipo zisanu ndi mmodzi (6) ndipo chimodzi chidali ndi mfuti. Zimbalangondozi zidabwera pagalimoto, adatero mkulu wina mderalo, yemwe adakana kutchulidwa dzina poopa kuti zimbalangondozo zingakamufinye kunyumba kwake. Zitangotsika mgalimotomo zidayamba kulimbana ndi achitetezo athu omwe adalipo anayi. Mkuluyu adati achitetezowo adali ndi zikwanje ngati zida zachitetezo, koma sizidanunkhe kanthu moti zimbalangodozo zidalanda zidazo nkukhapa nazo eniakewo. Anyamata athu achitetezo adathawira mchimanga koma mmodzi adakhapidwa modetsa nkhawa, adavulazidwa kwambiri moti pano akuyendera kuchipatala ku Queens, adatero mkuluyu Lachitatu lapitali. Cholinga cha zimbalangondozo sichikudziwika chifukwa zitavulaza achitetezowo, zidakwera galimoto nkumapita. Iye adati chichitikireni cha izi, anthu akuchita mantha chifukwa zamvekanso kuti zigawengazi zapha mlonda wina ku Socheko. Pakalipano anthu mderalo agwiriza zoti azilondera okha makomo awo ndipo sakugona tulo. Nkhaniyi akuti yafika kupolisi ya Soche ndipo apolisi ena ayamba kale kuyendayenda komwe kudaponda zigawengazi ndipo agwirapo kale ena amene akuwaganizira kuti akusowetsa mtendere ku Socheko. Mneneri wa polisi kuchigawo chakummwera Nicholas Gondwa wati ayambe wafufuza za nkhaniyi ndipo atiuza bwino zotsatira zake.
7
Pafunika K450 miliyoni ya makhansala Pafupifupi K450 miliyoni zikufunika kuti boma likwanitse lonjezo lake lopezera makhansala njira ya mayendedwe akamayendetsa ntchito za chitukuko mmadera awo, Tamvani wapeza. Pulezidenti wa makhansala mdziko muno Samson Chaziya adatsimikiza kuti boma lidavomereza kuti lipereka K1 miliyoni kwa khansala aliyense kuti adzipezere mayendedwe. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Tidali ndi mkhumano ndi nduna ya maboma angonoangono ndi komiti ya ku undunawu pa 13 February 2015 pomwe timakambirana nkhaniyi ndipo adalonjeza kuti khansala aliyense alandira K1 miliyoni yoti aonere mayendedwe, adatero Chaziya. Iye adati pakadalipano makhansala alipo okwana 450. Nkhani ya mayendedwe a makhansala idavuta pomwe boma limafuna kupereka njinga za moto za ngongole kwa makhansalawo koma ndondomekoyi siyidakomere makhansala. Woyendetsa ntchito za maboma angonoangono ku undunawu Kiswell Dakamau adatsimikiza za mkhumanowo koma adakana kuwulula zomwe zidakambidwa. Mneneri wa unduna wa maboma angonoangono ndi chitukuko cha mmidzi Muhlabase Mughogho adati pamsonkhanowo padatuluka nkhani ziwiri zikuluzikulu zomwe magulu awiriwo adakambirana. Iye adati nkhani yoyamba idali ya ngongole za mayendedwe ndipo adatsimikiza kuti unduna udavomereza zopereka ma K1 miliyoni kwa makhansala osati njinga monga momwe chikonzero chidalili poyamba. Ndalamazo sizichokera kuunduna koma unduna ukambirana ndi mabanki kuti apereke ngongole kwa makhansalawo ndipo za mmene ndalamazo zidzabwezedwere tidzachita kukambirana, adatero Mughogho.
2
YCW Maula Dinale Yasankha Atsogoleri Atsopano Bungwe la Young Christian Workers (YCW) ku Maula Dinale mu ya Lilongwe lapempha makolo kuti alimbikitse ana awo kusonkhana ndi anzawo mmabungwe omwe ali mu mpingo wakatolika mdziko muno. Wapampando wopuma wa bungwe-li Paul Chibwana wanena izi polankhula ndi Radio Maria Malawi pambuyo pa msonkhano wawo waukulu omwe unachitikira ku St. Patricks Parish ku Area 18 mu mzinda wa Lilongwe. Malinga ndi a Chibwana kusonkhana kwa achinyamatawa kumathandiza kwambiri pakuzamitsa moyo wauzimu ndi wathupinso kaamba kaziphunzitso zosiyanasiyana zomwe zimakhala ku mabungwe-wa. Pa msonkhanowu panachitikanso zisankho zosankha komiti yatsopano yoyendetsa ntchito za bungweli komwe asankha William Chirwa, wa ku St. Francis Parish, kukhala wapampando wa bungwelo ndipo Wachiwiri wake ndi Chifundo Nsewu, wochokeranso ku St. Francis Parish komweko.
13
Sabata zingapo zapitazi, takhala tikulengeza kuti patsamba lino tizikupatsirani Anatchereza ndi malangizo pamavuto amene mumakumana nawo. Mavutowa akhoza kukhala a mbanja, maphunziro, chipembedzo komanso momwe mumakhalira ndi ena. Anzanu ayamba kale kutitumizira madandaulo awo ndi awa ali mmunsimu. Chisale watuluka nkumangidwanso Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Ndili ndi zaka 20 ndipo amuna anga sagona mnumba ndiye chonde, ndithandizeni. Akuti ndikawauza ankhonswe banja langa litha. Ukwati tapanga August wapiyu. Ndine A Zikomo A, Mwamuna wakoyo ngwachibwana cha mchombolende! Mwangokwatirana kumene ndipo ukuti sagona mnyumba, ndiye amakagona kuti? Ukapanda kusamala naye ameneyo akubweretsera mmavuto aakulundikunenatu matenda oopsa, kuphatikizapo HIV/Edzi. Ngati wayamba kale kunena kuti ukakanena kwa ankhoswe banja lithapo ndiye kuti iye za banja alibe nazi ntchito koma kusangalatsa chilakolako cha thupi lake basi. Ndiye usazengerezepo apa, pita kaitule nkhaniyi kwa ankhoswe. Ngati akufuna kuti banjali lithe, lithe basi. Mwamuna wachimasomaso ndi woopsa kwambiri ndipo safunika kumusekerera. Anatchereza, Mwamuna wanga anandisiya ndili ndi mimba palendi. Ndikaimba foni amayankha ndi mkazi amene akufuna kukwatirana naye. Ndipange bwanji pamenepa? Choyamba, kuti mwamunayo azichoka pakhomo nkukusiyani palendi, chidachitika nchiyani? Eetu, amati umanena chatsitsa dzaye kuti njovu ithyoke mnyanga! Mukamafuna kuti tikuthandizeni, nkhani yanu muziiyala bwinobwino kuti tidziwe gwero la mavuto anu. Koma kungokalakala pamwamba, munena kuti agogo sanandithandize. Poti ine ndikusowa poyambira kuti ndikuthandizeni, ndingonena kuti pitani kwa ankhoswe anu mukawafotokozere zomwe amuna anu achita, mwina atha kukuthandizani. Komanso njira ina ndi yopita kukadandaula kubwalo la milandu kuti mwamuna wanu ngati akufuna kukwatira mkazi wina akusudzuleni mwadongosolo, nanga ukwati umatha choncho? Akapezeka kuti mwamunayo ngolakwa, akhoti amatha kumulamula kuti mwana akadzabadwa azidzamupatsa chithandizo chakutichakuti kufikira atakula. Tayesani njira ziwirizi, mwina mutha kuthandizika pa vuto lanu. Anatchereza, Zikomo ngati muli bwino. Ine dzina langa ndine Anthony P Nyirongo, ndavutika transport ndiye ndinasiya foni pababa shopu kuonjezera moto ndiye ndinawerenga nyuzi ya pa 27 September ndiye ndinawerenga pena pake kuti amene ali ndi vuto angathe kulemba text pa nambala yanu. Thanks.
12
Mgwirizano ungathetse zipolowe Mgwirizano pakati pa atsogoleri, ngakhale asemphane maganizo pa ndale ndiko kungathetse zipolowe ndi mikangano ya ndale, atero akadaulo. Iwo adanena izi potsatira chiwembu chofuna kuotcha maofesi a bungwe loona z ku Lilongwe sabata yatha, kuotchedwa kwa galimoto ziwiri za otsatira gulu la United Transformation Movement (UTM) masiku apitawo komanso kuopsezedwa kwa otsatira UTM ku Nyumba ya Malamulo. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Throsell: Zokhumudwitsa Kadaulo wa zandale ku Chancellor College Mustafa Hussein adatamanda mtsogoleri wa chipani chachikulu cha MCP Lazarus Chakwera komanso mtsogoleri wa UTM Saulos Chilima pogwirana chanza ndi kusekererana ku mwambo wa Angoni Maseko wa Umhlangano. Iye adati izi zimathandiza kuti otsatira zipani zawo aziyanjana, osakhala ndi maganizo a chiwembu kwa amene akutsutsana nawo maganizo. Izi nzofunika chifukwa ngati atsogoleri akusonyeza chikondi ndi chimvano chotere, mpovuta kuti anthu otsatira zipani zawo azipanga ziwawa chifukwa aziopa kukhumudwitsa atsogoleriwo, adatero Hussein. Kadaulo wina George Phiri wa ku University of Livingstonia (Unilia) adati atsogoleri awiriwa ngofunika kuwayamikira chifukwa chopachika kusiyana kwawo pandale nkudzichepetsa pamaso pa anthu owatsatira. Nzachidziwikire kuti kumwambo umenewo kudali otsatira zipani zonse ndipo adaona zomwe atsogoleri awo adachita. Kotero, anthuwo ngakhale atakhala ndi cholinga cha zipolowe akhonza kusintha maganizo, adatero Phiri. Iye adati nthawi idakwana yoti Amalawi azindikire tanthauzo lenileni la ndale za demokalase kuti ndi mpikisano koma ofuna kutukula dziko osati kunyozana kapena kuchitana ziwembi. Ndale za demokalase zimafunika kuti zipani zizipikisana pamfundo za chitukuko ndi utsogoleri koma nthawi zambiri timaona otsatira zipani akulimbana ngati kuti simtundu umodzi, adatero Phiri. Bungwe la mgwirizano wa maiko la United Nations (UN) lidadzudzula mchitidwe wa zipolowe umene ukupita patsogolo pomwe tikulowera ku chisankho cha pa 21 May 2019. Mneneri wa UN pa nkhani za ufulu wa anthu Liz Throssell adati zipolowe zimene zakhala zikumvekazi nzosakoneza. Galimoto ya phungu wina Agness Nyalonje idaotchedwa ku Mangochi mmwezi wa August, phungu winaso Patricia Kaliati adakumana ndi mazangazime akufuna kulowa mNyumba ya Malamulo mmwezi wa April ndipo atsogoleri amabungwe osiyanasiyana akhala akuwopsezedwa. Izi zikupereka chiopsezo pa demokalase, adatero Throssell.
11
Parish ya Ntaja Yalonjeza Kupitiriza Kuthandiza Radio Maria Parish ya St. Marys Ntaja mu dayosizi ya Mangochi yati ipitiriza kudzipereka pothandiza Radio Maria Malawi. Bambo mfumu a parishiyi, bambo Beato Mathyola anena izi pakutha pa mwambo wa misa ya Thandizani Radio Maria yomwe yachitika lero ku parishiyi. Bambo Mathyola kuchita mwambo wa perekani-perekani Iwo ati Radio Maria Malawi ikusowa zambiri, kotero anthu okonda wailesiyi akuyenera kupitiriza kuyithandiza, kuti ntchito zake zofalitsa nthenga wabwino, zipitilire kuyenda bwino. Akhristu ali ndi udindo kuthandiza Radio Maria kuti ipite patsogolo. Mikwingwirima yomwe tikukumana nayo isatilepheretse kuthandiza wailesiyi yomwe ikugwira ntchito zotamandika kwambiri pogawa mawu a Mulungu, anatero bambo Mathyola. Polankhulapo mkulu woyendetsa ntchito za Radio Maria Malawi a Louis Phiri ayamikira akhristu a parishiyi kaamba ka chidwi chomwe ali nacho pothandiza wailesiyi. Tikudziwa kuti matenda a COVID-19 abweretsa mavuto ambiri pa chuma koma iwo alimba mtima kuthandiza wailesiyi ndipo limeneli likhale phunziro kwa maparishi ena kuti asawilingule pothandiza wailesiyi, anatero a Phiri. Pamwambowu akhristu a ku St. Marys Parish, ku Ntaja athandiza wailesiyi ndi ndalama zoposera 3 hundred and 6 thousand kwacha.
13
World Vision Donates Buckets to Mangochi Police Mangochi Police Station has reason to smile after receiving 35 buckets from World Vision International (Mangochi Branch) to help in the fight against the coronavirus pandemic. The donation was received at Station premises on March 25, 2020. Daudi: They will also be distributed to our branches Speaking during the handover ceremony, World Vision Project Officer Miss Ireen Majankono said the organization thought it wise to assist in order to protect the officers and clients from the deadly Covid-19. Prevention is better than cure and we dont want to experience what other nations are facing due to the spread of the deadly virus, said Majankono. In his remarks the Station Community Policing Coordinator Assistant Superintendent Clement Madeira, who represented the Officer ln-charge, applauded World Vision for the nice gesture. Madeira said the donation has come at a right time when the whole world has been hit hard with coronavirus. He encouraged other stakeholders to borrow a leaf from World Vision International stressing that police officers also need to be safe at all times. World Vision lnternational has been working together with the Police especially in gender-based violence interventions and child marriages. According to Mangochi police deputy publicist Amina Daudi, the 35 buckets will be distributed at the parent station and its three posts and 21 police units.
14
Mudali mu basi ya National Shamuda Drake ndi mtolankhani wa wailesi ya Galaxy yemwe tsopano ali pabanja ndi mkazi wake Madalitso Moyo. Momwe Drake amayamba ulendo wake wochokera ku Lilongwe komwe amakaona mchimwene wake kupolisi ya Kawale, sadadziwe kuti nkupeza nthiti yakeyo. Naye Madalitso, pamene amachoka ku Dwangwa komwe amagwira ntchito kukampani yopanga shuga ya Illovo ulendo wa ku Mzuzu kukaona abale patsiku lokumbukira anthu amene adafera ufulu wa dziko lino pa 3 March, samadziwa kuti nkupeza wachikondi. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Drake ndi Mada adamangitsa ukwati ku Mzuzu Awiriwa adakhala mpando woyandikana mubasi ya National Bus Company koma sanayankhulitsane, kufikira pamene adafika pamalo ochita chipikisheni apolisi a Matete. Apa mpamene tidayamba kulankhulana ndipo adandifotokozera komwe amalowera. Macheza adapitirira ndipo titafika pa Bandawe, ndidamufunsa ngati angandipatse nambala yake ya foni yomwe adandipatsa ndikutsika basi pasiteji ya kwathu ku Malaza ku Chintheche, adafotokoza Drake. Drake adamuimbira foni usiku omwewo kuti amve wayenda bwanji koma sadakambe zambiri. Drake adati patadutsa masiku angapo, adamuyimbiranso kumpatsa moni, apa adali njoleyo idali itabwerera ku Dwangwa ndipo adayankhulitsana ngati ongodziwana chabe. Koma nditakhala masiku angapo, mtima wanga udayamba kukankha mwazi ndipo ndidamuyimbira kuti ndikadakonda titakumana bwino ndi kukambirana nkhani ina. Iye adati adalibe mpata chifukwa ntchito yawo amagwira sabata yonse, koma nditalimbikira adangoti ndidzapite nthawi ya nkhomaliro ndipo tidzakambirana kwa mphindi 30 zokha,adatero Drake. Ndipo tsikuli litakwana Drake adakampezadi Mada akadali kuntchito ndipo atakumana adamtengera kunyumba kwake komwe kudalinso anzake ena awiri. Apa adamkonzera chakudya ndipo adakambirana uku akudya. Adandifunsira banja, ndipo ndidamuuza kuti ndikaganize kaye, adatero Mada. Patatha masiku atatu, Drake adakokanso chingwe ndipo cimwemwe chidadzala tsaya Mada atanena kuti walola. Abusa mayi Agness Nyirenda ndiwo adamangitsa ukwati ku Zolozolo CCAP mumzinda wa Mzuzu ndipo madyerero adali kusukulu ya sekondale ya Katoto.
15
Dekhani pa zogawa dzikoAkadaulo Odziwa zandale ndi malamulo ati maganizo ogawa dziko lino kuti chigawo cha kumpoto kukhale dziko loima palokha akufunika kudekha ndi kulingalira mozama. Akuluakuluwo adatambasula izi Tamvani utafuna kumva maganizo awo pa zomwe adanena gavanala wa chipani cha Peoples Party mchigawo cha kumpoto, Christopher Mzomera Ngwira yemwe mmbuyomu adanena kuti chigawo cha kumpoto chikhale dziko loima palokha. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Roadblock ya Jenda: Malire a zigawo zina ndi kumpoto Koma atafunsidwa mosiyana, katswiri wa zamalamulo Edge Kanyonyongolo, mkulu wa bungwe lolimbikitsa kukambirana pa za mfundo zoyendetsera dziko lino la Institute for Policy Interaction (IPI) Rafiq Hajat, komanso otambasula za ndale Boniface Dulani ndi Blessings Chinsinga adagwirizana pamodzi: nkhaniyi siyikufunika phuma. Malinga ndi Kanyongolo, dera kapena gawo likathothoka kudziko nkukhala palokha limakumana ndi mavuto kuti maiko ena alivomereze kuti ndi dziko. Vuto ndi lakuti maiko ena amachiona chovuta kuvomereza dziko latsopanolo mmalo mwake silikhala ndi mpata wotenga nawo mbali pa zinthu zomwe maiko amachitira limodzi, adatero Kanyongolo. Dulani adati kulimbikitsa zogawa dziko kuli ngati kuukira zomwe siziloledwa mmalamulo a dziko lino. Iye adati ngati mbali kapena gawo lina likuona zovuta ndi mmene boma likuyendera, njira yabwino nkupempha kuti apatsidwe mphamvu zomayendetsera gawo lawo osati kukhala paokha. Mfundo imeneyi, kapena kuti federation mChingerezi ikulimbikitsidwa ndi chipani cha Malawi Congress Party. Maiko a South Africa, Nigeria, United States of America amatsata njirayi. Njira yopempha mphamvuyi imakhala bwino maiko omwe ndi akuluakulu powerengera kuti madera ena amakhala kutali kwambiri ndi likulu ndiye mpovutadi kulandira thandizo moyenera, adatero iye. Hajat adati nkhaniyi ndiyosafunika phuma koma kuunika bwinobwino. Anthu omwe akulimbikira izi akhoza kukhala ndi mfundo zokonza kusamvana komwe ndi gwero la nkhaniyi. Nthawi zina ndi bwino anthu oterewa kuwapatsa mpata oti ayese zomwe akutanthauzazo, adatero Hajat. Ndipo Chinsinga adati kugawa dziko si za masewera chifukwa chitukuko chikhoza kusokonekera. Iye adati pali mtunda waukulu kuti dziko lagawidwe chifukwa akuluakulu ndi anthu okhudzidwa amayenera kukhalirana pansi ndi kugwirizana mmene kagawidweko kayendere. Nkhani yoyamba ndi kukonza chisankho cha liferendamu chomwe sichinthu cha pafupi chifukwa akuluakuluwo amayenera kugwirizana bwinobwino mmene zinthu zikhalire dzikolo likagawidwa, adatero Chinsinga. Iye adati zikakhala chonchi, munthu aliyense amakhala ndi mpata wosankha mbali yomwe akufuna kuti akhale posatengera komwe amachokera. Katswiriyu adati ntchitoyi ikhoza kuvuta chifukwa cha nkhani ya maukwati ndi ntchito komanso zitukuko zomwe anthu ochokera mchigawo china adakhazikitsa mchigawo chomwe si chakwawo. Iye adagwirizana ndi Dulani kuti maiko ambiri omwe mumakhala mpungwepungwe ngati uwu amagwirizana kuti chigawo chomwe sichikukhutitsidwa ndikayendetsedwe kazinthucho chikhale ndi mphamvu zoyendetsera chigawocho koma chilli pansi paulamuliro wa dziko lomwelo. Mafumu ena a mchigawo cha kumpotochi atsutsana ndi maganizo a Ngwira ponena kuti zomwe akunenazo si maganizo a anthu a kumpoto. Mmodzi mwa mafumuwa, Kyungu yak u Karonga adati anthu omwe akulimbikitsa zokhazikitsa chigawochi ngati dziko pa lokha sadafunse anthu kuti apereke maganizo awo. Sadafunse munthu aliyense pankhaniyi ndiye akhala bwanji maganizo a anthu a kumpoto? Ife zimenezo sitikuzidziwa ayi, adatero Kyungu. Mfumun yaikulu Chikulamayembe ya ku Rumphi nayo idakana kutenga nawo mbali pa maganizo opanga chigawochi kukhala dziko pa lokha ndipo nayo idati mpofunika anthu atafunsidwa kaye nkumva maganizo awo. Mmodzi mwa akuluakulu a mabungwe omwe si aboma pankhani ya maphunziro Benedicto Kondowe adati nzomvetsa chisoni kuti Amalawi safuna kuphunzirira pa zinthu zomwe zidachitikapo kale nkulephereka kugwira ntchito. Kondowe yemwe ndi mkulu wa bungwe loyendetsa mgwirizano wa mabungwe omwe amakhudzidwa ndi nkhani za chitukuko cha maphunziro la Civil Society Coalition for Education Quality adati nkhani yolowetsa mitundu pandale idabwezeretsako chitukuko cha maphunziro mmbuyo ndipo kubwereza zoterezi kungakhale ndi zotsatira zowawa kwambiri. Nkhani yolowetsa mitundu pa ndale idavuta mzaka za mma 1988/89 pomwe boma la Malawi Congress Party lidalamula kuti aphunzitsi onse a kumpoto abwerere kwawo. Chifukwa cha ichi kudapezeka kuti sukulu zina zidagwa mmavuto a aphunzitsi, adatero Kondowe. Iye adati chofunika nkuunika chomwe chayambitsa nkhani yogawanayi nkukonza mowonongeka monse kuti dziko lipitirire kuyenda bwino. Malinga ndi Mzomera Ngwira yemwe akuti chigawo cha kumpoto chimasalidwa mzinthu zambiri monga ntchito za chitukuko. Koma malinga ndi malipoti, mtsogoleri wakale wadziko lino Joyce Banda adati izo nzosatheka ndipo zipani zina zotsutsa monga cha UDF sidatinso ganizoli silingathandize. Ngwira adati ali ndi chikhulupiriro kuti anthu a kumpoto atapatsidwa mwayi woponya chisankho cha liferendamu akhoza kusankha kuti chigawochi chichoke mmanja mwa dziko la Malawi ndi kukhala dziko lina palokha. Ndikudziwa zomwe ndikunena ndipo si kuti ndikulankhula zopanda pake ayi. Mwina pa anthu 100 aliwonse awiri kapena atatu okha ndiwo sangagwirizane ndi maganizo osandutsa mpoto kukhala dziko palokha, adatero iye.
11
Sinodi ya Nkhoma ikudana ndi zochotsa mimba Asadzasainire: Banda Sinodi ya Nkhoma ya mpingo wa CCAP yati kuloleza kuti amayi azichotsa mimba ndi kolakwika, nkhanza, uchimo komanso usatana pamaso pa Mulungu chifukwa ndi kuchotsa moyo wa munthu. Zonena za mpingowu zadza pamene mtsutso ukukula kuti malamulo a dziko lino asinthidwe kuti amayi azichotsa mimba ngati angafune. Padakali pano, malamulo a dziko lino amaletseratu kuchotsa mimba kupatula pomwe madotolo atanena kuti kusunga mimbayo kuika moyo wa mayi kapena mwana yemwe akuyembekezera uli pachiopsezo. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Chikalata cha mpingowo chimene adachisayina mbusa Vasco Kachipapa komanso mbusa Brian Kamwendo chidati moyo umayambika pamene mphamvu ya bambo ndi ya mayi zikumana nkupanga mwana ndipo imapitirira nthawi yonse imene mayi ali ndi mimba mpaka mwana kubadwa, kukula mpaka kufa kapena kumwalira. Choncho kuchotsa pathupi nkulakwira malembo oyera, chikalatacho chidatero. Padakali pano, bungwe lounikira malamulo la Malawi Law Commission likukonza bilo yokhudza zochotsa mimba, ndipo ngati biloyo aphungu a ku Nyumba ya Malamulo atakaivomereza, idzakhala lamulo lololeza kuchotsa mimba. Koma chikalatacho chidati aphungu asakalole izi chifukwa adasankhidwa kuti ateteze miyoyo ya anthu. Tikupemphanso mtsogoleri wa dziko lino Joyce Banda, yemwe ndi mzimayi kuti ngati aphungu angaloleze lamulolo, iye adzakane kusainira kuti zitero, chidatero chikalatacho. Unduna wa zaumoyo wati kuchotsa mimba kumadzetsa mavuto ena ndipo boma limaononga K300 miliyoni chaka chilichonse pothandiza amayi amene adakachotsa mimba mobisa pogwiritsa ntchito njira zodziwa okha.
13
Tea Akugulitsidwa Motchipa Kwambiri-Unduna Wolemba: Sylvester Kasitomu ntent/uploads/2019/09/nankhumwa.jpg" alt="" width="388" height="344" />Unduna wake ulowelerapo-Nankhumwa Unduna wa za malimidwe, ulimi wa mthilira ndi chitukuko cha madzi, walonjeza kuti ulowererapo pa mavuto omwe alimi angonoangono akukumana nawo mdziko muno. Nduna mu unduna-wu a Kondwani Nankhumwa anena izi lachitatu pomwe anayendera alimi a Tea ndi Nthochi a mmaboma a Thyolo ndi Mulanje. Paulendowu zadziwika kuti alimi angono angono a TEA akumagulitsa mbeu yawo pa mtengo otsikitsitsa poyerekeza ndi zomwe amalowetsa pochita mu ulimi-wu. Polankhulapo pambuyo pa ulendowu a Nankhumwa anati anakonza ulendowu ndi cholinga choti ayendere alimi anthochi omwe akhala akuvutika ndi matenda achisaka komanso tea. Timazayendera alimi anthochi komanso tea kuti tizamve tokha mavuto omwe anthuwa akukuamana nawo mderali potengera kuti izi ndi mbewu zomwe anthu mbomali amadalira, anatero a Nankhumwa. Mwazina anankhumwa alonjeza kuti akamba ndi anthu omwe amagula tea mmabomawa kuti akweze mitengo yogulira komanso kubweretsa mbewu nthochi za tsopano kuti anthu kuti abzale mmaderawa. Mtsogoleri wa alimi a tea mu dera la Maonga Smallholders Association a Wilfred Kasitomu anati alimi angonoangono a tea mbomali akukumana ndi mavuto ochuluka kaamba koti misika sikuyenda bwino potengera ndi zomwe iwo akulowetsa pochita ulimiwu. Ifeyo ku Thyolo kuno tilibe mbewu ina yoti tingadalire ndi tea yekha kaamba koti nthaka yathu inasuluka koma sitipindula kaamba ka misika yomwe imatigula masamba athu mwachitsanzo timagulitsa tea pa mtengo wa K121. 30t yomwe ndi yochepa kwambiri potengera ndi zomwe timalowetsa mmunda, anatero a Kasitomu.
4
Tame Mwawa: Phwete ndiye kudya kwake Sewero la Tikuferanji ndi limodzi mwa masewero omwe amapereka phunziro kwa anthu pazochitika mmoyo wa tsiku ndi tsiku komanso ndi msangulutso kwa anthu ambiri. Seweroli limaonetsedwa pakanema komanso kumveka pawailesi ya MBC. STEVEN PEMBAMOYO adachita chidwi ndi mmodzi mwa omwe amachita nawo seweroli, Tame Mwawa, yemwe ambiri amamudziwa kuti Chiphwanya museweromo ndipo adacheza naye motere: Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Mwawa: Ndidabadwa wazisudzo Ndikudziwe mnzanga. Ndine Tame Mwawa ndimakhala ku Machinjiri ku Blantyre koma kwathu nku Chiradzulu mmudzi mwa Kambalame, T/A Mpama. Udabadwa mchaka chanji? Ndidabadwa pa 26 October, 1977 ndipo ndine woyamba mbanja la ana 7, amuna 5 ndi asungwana awiri. Mbiri yako pazisudzo ndi yotani? Ndikhoza kunena kuti ndidabadwa wazisudzo kale. Abale anga amandiuza kuti ndili wamngono ndikadziongola kapena ndikamalira anthu amandiunjirira nkumaseka ndipo makolo anga adadziwiratu kuti ndidzakhala msangalatsi. Kusukulu anzanga ngakhalenso aphunzitsi ankachita kudziwa kuti Tame wabwera zilango ndiye zidali zosatha. Nthawi zina ndinkalembedwa pa anthu olongolola koma pomwe sindidapite kusukulu nkomwe. Pachikondwerero chokumbukira ufulu wa dziko ndinkapanga nawo zisudzo ndipo malipiro ake adali Fanta ndi mpunga wa nyama. Ndinkapanganso sewero la Ambuye Yesu. Udapezeka bwanji musewero la Tikuferanji? Nthawi ina yake ankakajambula seweroli pafupi ndi kwathu ndiye penapake pamafunika singanga koma munthu amasowa tsono ine ndidadzipereka kuti ndiyesere nkuchita bwino basi kulowa mseweroli kudali kumeneko. Panthawi imeneyo ndidadziwana ndi akuluakulu ena azisudzo monga Frank Yalu (Nginde) yemwe adanditenga kukalowa gulu lake la zisudzo lotchedwa Kasupe Arts Theatre. Pano ndidadziwika kwambiri moti ndimapezeka mmagulu azisudzo osiyanasiyana monga Kwathu komanso mumafilimi osiyanasiyana. Imodzi mwa mafilimu omwe ndilimo ndi ya Chinganingani yomwe ikuoneka pakanema ya Malawi komanso ndidayambitsa nawo pologalamu ya Phwete pa kanema yomweyi. Pawayilesi ndimapanga nawo Sewero la Sabata Ino. Dzina la Chiphwanya lidayamba bwanji? Kumudzi kwathu ku Chiradzulu kuli mkulu wina dzina lake Chiphwanya yemwe ndi wolongolola komanso wosachedwa kupsa mtima ndiye nditaona malo omwe ndimapatsidwa mmasewero ambiri ndidaona kuti dzinali ndi londiyenera. Nzoona kuti pakhomo pako udadzala zikho zambiri? Eya, ndimadziwiratu mbali zomwe anzanga amakonda kundipatsa pazisudzo motero ndidadzala zikho zambiri komanso mikanda pakhomo panga ili mbweee! Moti anthu ena amaona ngati ndimapangadi zausinganga.
15
Papa Ndiwokhudzidwa ndi Ngozi Yomwe Yachitika Mdziko la India Wolemba: Glory Kondowe Mtsogoleri wa mpingo wakatolika pa dziko lonse Papa Francisco wati ndi wokhudzidwa ndi ngozi ya kusefukira kwa madzi imene yakhudzz madera ena mdziko la India. Wapereka uthenga wa chipepeso Papa Papa Francisco walankhula izi potsatira malipoti akuti anthu oposera 180 omwe afa pa ngozi-yo yomwe yadza kamba ka mvula ya mphamvu yomwe yakhala ikugwa mdzikomo. Malingana ndi malipoti Papa Frascico wati ndi wokhudzidwa ndi ngoziyi ndipo wati ayikiza komanso kukumbukira mapemphero anthu omwe ataya miyoyo yawo pangoziyi. Madera ena omwe akhudzidwa ndi monga ndi Clarah Kelatakah, Muharashitra ndi ena ambiri ndipo ati madera ena omwe akhudzidwa kwambiri ndi madera monga Lucky Lala komwe kwafa anthu oposera 60 ndipo anthu omwe akhudzidwa chiwerengero chawo chaposa 288 thousand ndipo anthu ena oposera 582 thousand ndiomwe apulumutsidwa pangoziyi ndipo ati zomwe zachitikazi zokhudza kwambiri mu dziko la India.
14
PAC Yadandaula Ndi Kuchuluka Kwa Chiwerengero Cha Nduna Bungwe la mipingo ndi zipembedzo mdziko muno la Public Affairs Committe (PAC) ladandaula ndi kuchuluka kwa chiwerengero cha nduna zomwe mtsogoleri wa dziko lino wasankha. Matonga: Zikhudza chuma cha dziko Mlembi wamkulu wa bungwe la PAC, mbusa Gilford Matonga wati mtsogoleri wa dziko lino wasankha chiwerengero chochuluka cha nduna zake zomwe akuti zitha kuwonongetsa chuma cha dziko lino. Kukhuzidwa kwathu pa cabinet yomwe atulusa a president sikusatha kapena kutha ntchito koma ndi mmene cabinet-yo ilili kupezeka kwa banja mu cabinet-mu komanso kukula kwa cabinet-yi zomwe zitakhuze chuma cha dziko lino, anatero Matonga. Padakalipano nalo bungwe la Centre for Democracy Economic and Development Initiative (CDEDI) lati zomwe wachita mtsogoleri wa dziko linoyu zikusiyana kwambiri ndi zomwe amalonjeza pa misonkhano yokopa anthu. Mkulu wa bungweli a Sylvester Namiwa ati mwazina kusankha ma udindo komwe a Chakwera achita, zawonetsa kuti cholinga chawo ndi kufuna kuthokoza anthuwa osati kuwasankha anthuwa kuti atumikire a Malawi. Iwo atinso ndi okhumudwa ndi kusankhidwa kwa amayi ambiri omwe ayikidwa ngati achiwiri kwa nduna osati nduna zenizeni.
11
Palibe mlendo ku MCPMunthali Pomwe chipani cha Malawi Congress Party (MCP) chidachititsa msonkhano wake waukulu kumathero a sabata yapitayi mwa mpanimpani pothawa ziletso ku mabwalo a milandu, zidadziwika kuti chipanichi chasintha kayendetsedwe pochoka pokhazikika mchigawo chapakati nkusefukira mzigawo zonse za dziko lino. Pamsonkhanowo amnkhala kale mchipanichi omwe amachokera mchigawo chapakati monga Juliana Lunguzi, Max Thyolera, Lewis Chakwantha, Kusamba Dzonzi, Daniel Mlomo, Lyton Dzombe, Jean Sendeza, Rhino Chiphiko ndi ena sadapateko mpando olo umodzi. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Atsogoleri a MCP: Mkandawire, Mia ndi Chakwera Koma yambiri mwa mipandoyi idapita kwa alendo ochokera ku chipani cha Peoples Party(PP) Sidik Mia, Harry Mkandawire, Cornelius Mwalwanda, Salim Bagus, Ken Zikhale Ngoma ndi Catherine Gotani mwa ena. Izi zikuonetsa kuti maudindo achoka kuchipinda cha MCP komwe nkuchigawo chapakati ndipo afalikira mzigawo za kummwera ndi kumpoto. Koma tikayangana mmbuyo pa msonkhano omwe chipanichi chidapangitsa mchaka cha 2013, Lazarus Chakwera yemwe adali mlendo koma wochokera kuchigawo chapakati, adasankhidwa kukhala mtsogoleri pomwe wachiwiri wake adali Richard Msowoya wochokera ku chigawo cha kumpoto ndipo mlembi wamkulu adali Gustave Kaliwo wa kummwera. Ndipo pamasankho omwe adalipo sabata yathayi, Chakwera adasankhidwa kukhala mtsogoleri wopanda wopikisana naye, pomwe naye Sidik Mia wochokera ku mmwera adalowa ngati wachiwiri kwa mtsogoleri ndipo Eisenhower Mkaka yemwenso amachokera ku Lilongwe adalowa ngati mlembi wamkulu wachipanicho. Pomwe mpando wa mneneri udapita kwa mlendo winanso Maurice Munthali yemwe amachokera ku chigawo cha ku mpoto. Mpandowutu udali wa Mkaka, msonkhanowu usadachitike. Komatu anthu ena izi sizidawakomere ndipo anenetsa kuti chipanichi chidaperekedwa kwa alendo okhaokha maka ochokera ku PP oposa theka kukhala mmipando ikuluikulu nkusiya amnkhala kalewa pofuna kuwasangalatsa. Koma polankhulapo mneneri wa chipanicho Munthali adati palibe mlendo mchipani cha MCP chifukwa aliyense adali wa chipanichi ulamuliro wa zipani zambiri usadabwere. Malinga ndi Munthali, anthuwa angobwerera kuchipani chawo chakale. Iye adati a mnkhalakalewa akungoyenera kudziwa kuti kayendetsedwe ka ndale kamasintha malinga ndi momwe nyengo ilili. Komanso tisaiwale kuti paja mtsogoleri wathu Chakwera, adatsegula khomo kuti aliyense alowe ndipo palibe zoti uyu adali wa PP, kapena Aford kaya DPP ayi,adalongosola Munthali. Iye adaonjeranso kuti nchifukwa cha kutsekulidwa kwa khomoko anthu ambiri akubwera ndipo ngati chipani akufuna anthu ambiri. Amnkhalakalewa asadandaule kapena kuchoka mchipani chifukwa kubwera kwa anthuku kukungosonyeza kuti chipanichi chili ndi fungo labwino lomwe likuitana anthu, iye adatero. Mmodzi mwa akadaulo pa ndale Mustafa Hussein adavomerezana ndi Munthali kuti aliyense adali wa MCP ndipo anthuwa angobwerera ku chipani chawo chakale. Hussein adati posankha anthu ochokera mzigawo zosiyanasiyana chipanichi chatenga njira yabwino yoonetsa kuti ndi cha fuko la Malawi osati cha chigawo chapakati chokha. Aliyense ali ndi mizu ya MCP chifukwa nchipani cha kale. Apapa chipani cha MCP chapeza njira yabwino chifukwa ena amati ncha chigawo chapakati pomwe ena ankati ncha Achewa. Uku kudali kulakwitsa chifukwa chipanichi sadayambitse ndi Achewa ayi koma achina Orton Chirwa, yemwe adali wa ku Nkhata Bay, adatero Hussein. Iye adaonjeranso kuti chipani chiyende bwino ntchito imakhala pomanga maziko osati pa maudindo a kumtundaku.
11
Apha Mdzukulu Wake Kaamba Ka Njinga Wolemba: Glory Kondowe arrest.jpg 302w" sizes="(max-width: 473px) 100vw, 473px" /> Apolisi mboma la Dedza akusunga mchitokosi a Goodwin Golden a zaka 20 zakubadwa popha mdzukulu wawo wa zaka 8 chifukwa cha njinga yakapalasa. Wachiwiri kwa wofalitsa nkhani mbomalo Cassim Manda wati loweruka pa 14 mwezi uno malemu-yu Yoswa Olivani anatenga njingayo kwa makolo ake mkumayendetsa ndipo ali mkati moyendetsa anakomana ndi woganizilidwayu yemwe ndi amalume ake omwe anamulanda njingayo ndipo anamumanga pakhosi ndi chingwe mpaka kufa. Wofalitsa nkhani za apolisiyu wati woganizilidwayu anakataya thupi la malemuyo muchimbudzi. Atawona kusowa kwa mwanayu makolo anayamba kumusakasaka koma sanapezeke ndipo usiku anthu anakumana pabwalo panyumba yamalemuwo kukambilana zochita ndipo woganizilidwayu anali pomwepo koma ati anachoka pa malopo modabwitsa kulowera ku chimbudzi zomwe zinapangitsa anthu kuyamba kuganiza ndipo mpaka anamulondola kuchimbudziko ndipo anapeza thupi lamalemuwo lili tchimbudzicho, anatero Manda. A Goodwin ati anayetsetsa kuthawa koma anagwidwa ndi anthu amudzimo. Malinga ndi zotsatora za ku chipatala malemuyo wafa kamba kobanika ndipo anapezekanso ndi chigwe mkhosi pa nthawiyo. Woganilizidwayo komanso malemuwo onse amachokera mudzi mwa Kanyimbi mfumu yayikulu Kachere mboma la Dedza.
14
Chikalata cha Sinodi chili ndi mfundo Boma lisanyozere zounikira za chikalata cha Sinodi ya Nkhoma mu Mpingo wa CCAP younikira mavuto omwe ayanga pakati pa anthu mdziko muno, atero wachiwiri wakale wa mtsogoleri wa dziko lino, mlembi wamkulu wa Sinodi ya Livingstonia mu mpingo wa CCAP, Levi Nyondo, mkulu wa bungwe la zachilungamo, mfumu ina kudzanso anthu ena angapo msabatayi. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Kalatayi, yomwe idati boma la Bingu wa Mutharika silikulabada zofuna za anthu omwe adalisankha, idawerengedwa mmatchalitchi a Sinodiyi Lamulungu. Mutu wa kalatayi, yomwe uthenga wake udachokera pa Mateyu 5: 13-16, udali Kukwaniritsa chikhulupiriro chathu kudzera mmapemphero, nthawi yathu ndi mdziko mwathu. Koma mneneri wa boma, Patricia Kaliati, wati nkutheka uwu ndi mtopola chabe chifukwa cha kusakwaniritsa kuwapatsa K10 miliyoni yomwe Mutharika adalonjeza ku Sinodiyo. Kumvetsa malemba Iye wati anthu a Mulunguwa akuyenera kuchita zomwe Yesu amachita komanso kumamvetsa malemba. Mwa zina, kalatayi idati kusowa kwa mafuta agalimoto komanso ndalama zakunja kwavulaza anthu akumudzi malinga ndi kukwera kwa mitengo ya katundu ndi zina zofunika pa umoyo wa anthu. Uthenga wa kalatayi udapitiriranso kukumbutsa Mutharika za K10 miliyoni ya mamangidwe yomwe mtsogoleriyo adalonjeza mpingowu mu Juni chaka chatha. Wachiwiri wakale wa mtsogoleri wa dziko lino, Cassim Chilumpha, wati boma la DPP lilibe chidwi pamadandaulo a anthu chifukwa limatenga aliyense wopereka maganizo ake ngati wofuna kuononga. Iye wati likadakhala boma lofuna kuthandiza anthu ake likadayankha zingapo zokhudza Amalawi mosayangana zifukwa za ndale. Chilumpha wati akukaika kuti bomali lingayankhepo chifukwa aka sikoyamba kuti kutuluke chikalata chonga ichi ndipo nthawi zonse boma limangoyankha molalata. Pamene patuluka mafunso pamayenera patuluke mayankho, adatero Chilumpha. Anthu akuvutika Mfumu ina mboma la Mwanza yati Sinodiyo sidalakwitse polemba chibaluwacho chifukwa anthu kumudzi akuvutika kwambiri. Iyo yati ikadakonda boma litakonza zomwe amabungwe ndi amipingo akhala akunena kuti zikudandaulitsa anthu. Kuno ku Mwanza patha sabata ziwiri kulibe mafuta [agalimoto]. Tikufuna timve yankho la boma, ikutero mfumuyi. Nyondo wati ngati mpingo ukugwirizana kwathunthu ndi chikalata chomwe a Nkhoma alemba kotero boma likuyenera kukonza mberewere zake. Iye wati mpingo wawo ulibe maganizo otulutsa chikalata china koma uyesetsa kuthandizira chikalata chomwe anzawo alemba. Tikakamizabe kuti [boma] likonze zimenezi. Ngati zikanike kuti [boma] silikuchita kanthu ndiye tiona chomwe tingachite koma sitinganeneretu za chomwe tichite. Kaya ndikukakamiza kuti mtsogoleri wa dziko lino atule pansi udindo kaya ayi koma tichita kanthu zikakanika, adatero Nyondo. Konzani molakwika Tiyanjane Kadzah yemwe ndi mulimi wa mmudzi mwa Nakhalu kwa T/A Kayembe mboma la Dowa wati boma likonze molakwika chifukwa awa ndi anthu a Mulungu omwe akudziwa chomwe chikuchitika. Anthu a Mulungu sumalimbana nawo, umangokonza chomwe anena. Kunena zoona zinthu sizili bwino ndipo sizikuyenda. Sikumudzi kokha kuno komwe mavutowa azinga, adatero Kadzah. Cathy Lambulira wa mmudzi mwa Chindiwo kwa T/A Mlumbe mboma la Zomba ndipo akuchita maphunziro a ukachenjede mumzinda wa Blantyre wati boma likuyenera kuonetsa chidwi pazomwe chibaluwachi chikunena chifukwa zomwe zikunenedwa ndizo zikukhudza Amalawi kumudzi. Kumudzi kuno tikukhala pachiopsezo kaamba ka kukwera mtengo kwazinthu. Tingakhale bwanji pomwe chilichonse chikungokwera mtengo? Uku ndikupha kumene koma [boma] silikudziwa. Atakonza zimenezi chifukwa pachilichose tikuvutika ndi ife, wapempha Lambulira. Zinthu sizili bwino Mkulu wa bungwe loona zachilungamo la Justice Link, Justine Dzonzi, wati chikalatachi chikutsimikiza kuti zinthu sizili bwino. Dzonzi wati alibe chikhulupiriro kuti boma lingathe kusintha zinthu pakali pano. Koma T/A Mwakaboko ya mboma la Karonga yati sikumvetsa mmene zinthu zilili mdziko muno kotero anthu angodikirira 2014. Iye adakana kuyankhapo pankhaniyi ponena kuti anthu angodikira 2014 pomwe adzaponye masankho osankha yemwe akumufuna. Sikuti mavutowa ali mdziko mwathu muno mokha; maiko anzathu akuvutikanso. Sitingati ulamuliro oipa ndiwo wabweretsa mavutowa. Tidikire 2014 kuti tidzaone ngati zili bwino kapena ayi, adatero Mwakaboko. Mlembi wa mkulu wa Sinodi ya Blantyre mu mpingo wa CCAP, Alex Maulana wati iye sadalandire chikalata chomwe a Nkhoma atulutsa kotero sangaike mlomo ngati akugwirizana nacho kapena ayi. Iye adapempha kuti Tamvani imupatse nthawi kuti awerenge bwino chikalatacho. Mchaka cha 2010 Sinodiyi idatulutsanso chikalata chodzudzula Mutharika ndi boma lake la DPP. Mu Okotobala chaka chatha, Mpingo wa Katolika udatulutsa chikalata chodzudzula boma la Mutharika pandale, chuma ndi maufulu a anthu. Bishop Joseph Mukasa Zuza wa mpingo wa Katolika adati sangaikepo mlomo chifukwa sadaone kalatayo. T/A Mlumbe ya mboma la Zomba adati nkhaniyo yamukulira kotero sangayankhire.
13
Zotsatira za Mayeso a Standard 8 Zatuluka Wolemba: Thokozani Chapola Uduna wa za maphunziro, sayansi ndi luso la makono watulutsa zotsatira za mayeso a ophunzira a Standard 8 a chaka chino. Malingana ndi chikalata cha zotsatilachi, ophunzirawa akhonza ndi 77.46% zomwe zikutanthauza kuti mwa ophunzira 282, 428 omwe analemba mayesowa ophunzira 218, 756 ndi omwe apambana kuyimira. Mwa ophunzira opambana-wa 82, 072 ndi omwe awasankhira msukulu zosiyanasiyana za sekondale za boma zomwe zikuyimira 37. 5 %. Ophunzira omwe asankhidwawa undunawu wati akukayenera kukaonekera msukulu zomwe awasankhira pa 16 September 2019.
3
Apolisi ku Lingadzi Ati Agwira Ntchito Limodzi Ndi Achitetezo Chakumadera mu Nthawi ya Lockdown Apolisi ku Lingadzi mu mzinda wa Lilongwe lachitatu atsimikizira akuluakulu owona za chitetezo chakumadera (Community Policing) mmadera A Area 10 ndi Area 12 mu mzindawo kuti apereka chitetezo chokwanira pa nthawi yomwe mtsogoleri wa dziko lino walamula kuti anthu asayendeyende kwa masiku 21. Zgambo: Chitetezo chikhalapo chokwanira Wofalitsa nkhani za apolisi ku Lingadzi Sergeant Salome Zgambo watisimikizira zankhaniyi. Iye wati cholinga cha apolisi poyendera apolisi akumidziwo, chinali chofuna kukawalimbikitsa ndi kukawatsimikizira za chitetezo ku maderawo. Lero ife a Lingadzi Police tinayendera makomiti aku Area 10 komaso Area 12 kuwalimbikisa kuti chitetezo chikhalapo chokwanira ndipo tigwira ntchito usana ndi usiku, anatero a Zgambo. Iwo atsimikiziranso anthu mmaderawo kuti asakhale ndi mantha chifukwa cha kutulutsidwa kwa akaidi ku ndende pofuna kuti akayidiwa asamakhale mothinana pofuna kupewa mliri wa nthenda ya Coronavirus ponena kuti iwo akhalabe akuyanganira bwino deralo.
14
Bishop Stima Apempha Akhristu Akondwere Pasaka Mosamala Episkopi wa dayosizi ya Mangochi, ambuye Montfort Stima wapempha akhristu mu dayosizi-yi kuti pamene akukondwerera chaka cha Pasaka asayiwale kutsatira njira zomwe unduna wa zaumoyo wapereka zopewera kachilombo ka Coronavirus mdziko muno. Wapereka mafuno abwino kwa akhristu ake-Bishop Stima Ambuye Stima alankhula izi mu uthenga wawo wapadera wa chaka cha Pasaka, kwa akhristu awo. Iwo ati ngakhale Mulungu Woyera wa chaka chino siwunayende monga mwa zaka zonse, akhristuwa asaleke kupitiriza kupemphera komanso kulimbikitsa njira zopewera kachilombo ka Coronavirus. Ngakhale Mulungu Woyera wa chaka chino siwunayende monga mwa zaka zonse, tisaleke kupitiriza kupemphera komanso kulimbikitsa njira zopewera kachilombo ka coronavirus, anatero Ambuye Stima. Iwo ati kachilombo ka Coronavirus komwe kadza pakati pa anthu pa dziko lonse kadzetsa mavuto aakulu koma kuwuka kwa Ambuye Yesu kuthandize kudzetsa kuwala pochotsa mantha komanso chikayiko mmitima mwa akhristu.
13
Olembetsa akuchepa Boma la Nsanje likupitilirabe kutsogola pa maboma omwe nantindi wa anthu alembetsa pa ntchito ya kalembera wa mkaundula wachisankho cha chaka cha mawa. Ndipo poyerekeza ndi chisankho cha 2014, maboma onse, kupatula a Nsanje, Chikwawa ndi Nkhotakota, anthu alembetsa ochepa kwambiri chaka chino. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Ntchito ya kalembera tsopano yalowera kumpoto Malinga ndi kalata yomwe lidatulutsa bungwe loyendetsa zisankho mdziko muno la Malawi Electoral Commission(MEC) lachinayi, lidati pakutha pa gawo 7, anthu omwe alembetsa ndi 6.26 milliyoni. Chiwerengerochi ndi chotsika ndi 81peresenti poyerekeza ndi anthu 7.74 miliyoni omwe bungwe la MEC limayembekezera kuti alembetsa pakutha pa gawo 7, yatero kalatayo yomwe idasainidwa ndi komishona wa MEC Jean Mathanga. Chiwerengerochinso ndi chotsika ndi 91 peresenti poyerekeza ndi anthu omwe adalembetsa panthawi yomweyi mchaka cha 2014. Pa nthawiyi, anthu 6.85 miliyoni ndiwo adalembetsa. Komatu ngakhale ntchitoyu ili kumapeto pomwe gawo lomaliza layamba lero mmaboma a Mzimba, Likoma, Nkhata Bay ndi mzinda wa Mzuzu, zikuoneka kuti Amalawi ambiri sakutenga nawo gawo mkalemberayu poyerekeza ndi zisankho za mchaka cha 2014 ndi 2009. Izitu zikuonetseratu kuti chiwerengerochi chikhonza kudzatsikanso pa nthawi yamavoti tikaunika mbiri ya kavotedwe mdziko muno. Malinga ndi mneneri wa bungwe la Malawi Electoral Support Network (Mesn) Michael Kachaso, vuto lalikulu lagona poti mabungwe ambiri sadatenge nawo gawo pokaphunzitsa anthu zakufunika kwa kulembetsa. Iye adati ngakhale bungwe la MEC lidavomereza mabungwe ambiri kukaphunzitsa anthu zokalembetsa, ambiri mwa mabungwewa sadagwire ntchitoyi chifukwa chosowa ndalama. Kachaso adaonjezeranso kuti Amalawi ambiri sadalembetsenso chifukwa adanyanyala. Anthu olembetsa ndiochepa pa zifukwa zambiri monga kunyanyala chifukwa atsogoleri awo sadakwaniritse zomwe adalonjeza, adalongosola Kachaso. Iye adaonjezeranso kuti ena sakuona phindu lolembetsa chifukwa ali kale ndi chiphaso cha u nzika. Apa adati mmbuyomu ena amalembetsa kuti apeze ziphatsozi ndipo pano sakuonanso phindu la kalemberayu. Kachaso adatinso ngati bungwe la MEC lingaganize zobwerezanso kalemberayu, a mabungwe adzatengepo gawo lalikulu pophunzitsa anthu makamaka omwe alembetsawo kuti adzavote. Polankhulapo, mkulu wa bungwe la National Initiative for Civic Education (Nice) Ollen Mwalubunju adati bungwe lake layesetsa kumemeza anthu kuti akalembetse mkaundulayu. Mwalubunju adati vuto lagona poti anthu ambiri adanyanyala chifukwa atsogoleri omwe adasankha mmbuyomu sadakwaniritse zomwe adalonjeza. Ife tikuyesetsa kumbali yathu kuwamema anthu kuti akalembetse ngati akufuna kusintha zinthu chifukwa akangokhumudwa nkukhazikika, ndi njira imodzi yoti anthu omwe sakuwafuna akhalebe mmipando, adalongosola Mwalubunju. Iye adaonjezeranso kuti malinga ndi malipoti omwe bungwe lake likulandira kuchokera kwa anthu omwe akugwira nawo ntchito mmidzi, Amalawi ambiri akhumudwanso kaamba ka kukula kwa katangale mbali zonse za dziko lino. Talephera kuika ndondomeko zotsimikizika zothana ndi vutoli. Anthu ndi okhumudwa kwambiri ndi izi mwa zina, pachifukwa ichi adindo ndi atsogoleri a zipani aunikenso bwino malonjezano awo, Mwalubunju adatero. Iye adatinso bungwe la MEC lipange kafukufuku wofufuza zomwe zachititsa kuti anthu ambiri asatuluke. Mchaka cha 2014 anthu 7.5 miliyoni adalembetsa mkaundula ngakhale okavota adali 5.2 miliyoni. Izi zikutanthauza kuti pafupifupi 30 peresenti ya anthu olembetsa sidakavote nawo. Ndipo pamasankho a 2009, anthu pafupifupi 5.8 miliyoni ndiwo adalembetsa pomwe 4.6 miliyoni ndi amene adavota. Apa anthu pafupifupi 22 peresenti sadakavote nawo pamasankhowa. Kalemberayu adayamba mwezi wa June ndipo akuyembekezereka kutha pa November 9 mmaboma a Mzimba, Nkhata Bay, Likoma ndi mzinda wa Mzuzu. Ntchitoyi yayamba lero.
11
Tidali maneba ku Gulliver Mawu akuti mbuzi imadya pomwe aimangilira amamveka achabe koma nthawi zina mawuomwewa amakhala ndi tanthauzo lopambana, maka potengera zipatso zomwe abala panthawiyo. Pachiyambi, Kingsley Blessings Chowawa ndi Loness Gwazanga adali maneba chabe, koma pano chinebacho chawachitira ubwino chifukwa chifukwa chabala chipatso chokoma chomwe awiriwa adzakhale akuchibwekera. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Kunyadirana maneba: Ukwati wa Loness ndi Kingsley udzakhalako pa 3 October chaka chino Awiriwa akuti kukumana kwawo ku Gulliver ku Area 49 nku Lilongwe kudali ngati kwa masewera poti zimaoneka ngati kuyandikana ndiko kumawakokera kufupi ndipo zimaonekanso ngati masewera chabe. Ineyo ndinkakana chifukwa ndinkati munthu wamkhonde zoona? Mwina angochitira kuti poti ndayandikira mpakana zaka zisanu akundivutitsa kufikira mchaka cha 2011 pomwe ndidamuvomera, adatero Loness, yemwe pano ndi mtolankhani wa Malawi News Agency. Iye adati atakumana koyamba mchaka cha 2006 sizimamukhudza mumtima ndipo adalibe naye chidwi, koma chifukwa chake mpaka lero sachidziwa. Iye adaonjeza kuti mokakamiza adayamba kucheza ndipo Kinsley adamufunsira koma iye adakana ndipo akuti mnyamatayu sadagonje ndipo mmalo mwake machezawo adawathamangitsira ku chinzake kuti mwina azichitirana manyazi koma mnyamata sadaimve. Zitatheka mchaka cha 2011 awiriwa sadafune za bobobo, koma kukaonekera kwa makolo mpaka chinkhoswe chidachitika pa 4 April chaka chino kuholo ya patchalitchi cha Kagwa Woyera ku Area 49 ndipo akuti ukwati woyera udzakhalako pa 3 October ku Chikuti CCAP ku Area 49 komweko ndipo madyerero adzakhala ku Cherub Private School ku Area 47. Kingsley akuonetsa kuti za msungwanayu adafa mutu koopsa chifukwa adachita kunenetsa kuti azimugwiritsa ngati tambula yagalasi kuopa kuswa. Chomwe wavutikira chimafunika kusamala kwambiri chifukwa chikatayika ululu wake umakhala waukulu zedi kusiyana ndi chomwe changobwera chokha. Uyu ndiye ndidasankha padziko lonse, adatero Kingsley. Awiriwa akuti ngakhale kuti banja si msewu wamaluwamaluwa, iwowa adzayesetsa kuti banja lawo lokha lidzakhale loyenda mkuwala ndi lochititsa kaso pamaso pa mulungu ndi anthu. Kingsley amachokera mmudzi mwa Malembo kwa T/A Khongoni ku Lilongwe ndipo akugwira ntchito kubanki yobwereketsa ndalama ya Select Financial Services, pomwe Loness amachokera mmudzi mwa Kamonga, T/A Kaphuka ku Dedza.
15
Ulalo adali venda wa masiketi Makolo polangiza amati ukadekha, umawona maso a nkhono ndipo mwambi womwewu ansembe amati ukafuna kuvala kolona, ukuyenera kusunga khosi. Miyambiyi siyapafupi kwa anthu ambiri kuyitsata koma umboni wake ulipo wa nkhaninkhani pakuti kwa iwo omwe adadekha nkusunga makosi, pano Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu amadziwa momwe maso a nkhono alili ndipo kolona ali mkhosi. Edward ndi Maggie tsiku la ukwati wawo Apa pali umboni wa Edward Bannet Gangile wa kwa T/A Chiwere ku Dowa ndi Maggie Failo wa kwa T/A Malengachanzi ku Nkhotakota omwe ngakhale adakondana atangoonana koyamba, iwo adadekherana asadapalane ubwenzi. Nthawiyo, mchaka cha 2013, Gangile adali wowerengera za chuma ku chipatala cha mishoni cha Nkhoma ndipo akuti chipatalachi chimakonda kugula katundu monga mapepala ndi zolembera kushopu ya Maggie yomwe idali ku Area 3 mumzinda wa Lilongwe. Nthawiyo ndimayesetsa kumuthandiza mwachangu ndi mwansangala. Timapatsana moni ndi kucheza nkhani zingapo koma ndimalephera kumuuza za kukhosi. Adandisangalatsa kwambiri ndi nsangala zomwe amandirandira nazo, adatero Gangile. Iye adati mpata udapezeka tsiku ali mushopumo ndipo mudabwera venda ogulitsa masiketi omwe adasangalatsa Maggie ndipo mwa izi, namwaliyo adamufunsa ngati angamugulireko mkazi wake. Ndimathokoza Mulungu kuti ndidaganiza msanga chifukwa ndidangoyankha kuti ndidzamugulira ndikadzamupeza ndipo yankholi lidamupangitsa kundifunsa mafunso ambiri pa zamoyo wanga kuphatikizapo kukayika kuti mwina ndimamunamiza, adatero Gangile. Iye adati ichi chidali chiyambi cha awiriwa kufufuzana ndikudziwana bwinobwino mpaka adavomerezana kuti onse amadikirana kutanthauza kuti aliyense mwa iwo adadekha kapena kusunga khosi. Iye adati awiriwa adakhala miyezi ubwenzi usadayambe kwenikweni kuchoka panthawiyo ndipo zonse zitalongosoka, adapanga chinkhoswe pa 15 April, 2015 ku Area 47 kwa azakhali a Maggie ndipo ukwati udachitikira ku Lilongwe Golf Club pa 12 July, 2015.
15
Anthu Okhuzidwa Apempha Kuti Chisankho cha Aphungu Chichitikenso Gulu la anthu okhudzidwa la Concerned Citizens lati likufuna kuti bwalo la za malamulo lomwe linagamula kuti chisankho cha president chichitikenso mdziko muno, ligamulenso kuti chisankho cha aphungu akunyumba ya malamulo chichitikenso pamodzi ndi chisankhochi. Gululi lomwe lili ndi anthu oposa 180, lalembera kalata bwalo la High Court ku Lilongwe, kupempha kuti chisankho cha president chatsopano chichitike limodzi ndi cha aphungu akunyumba ya malamulo kamba koti bungwe la MEC lomwe bwalo la zamalamulo linati linalakwitsa pa kayendetsedwe ka chisankho cha president mmwezi wa May chaka chatha, ndi lomwenso linayendetsa chisankho cha aphungu a kunyumba ya malamulo. Gululi lati ndi kutheka kuti bungweli lidalakwitsa zonse pa chisankhochi ndipo latinso malamulo a dziko lino, amati chisankho cha president komanso aphungu a kunyumba ya malamulo chidzichitika limodzi ndipo osankhidwa adzikhala pa udindo kwa zaka zisanu. Ine monga mzika ya Malawi tikufuna kuti chisankho cha president chichitike limodzi ndi cha aphungu chifukwa aphunguwa akuyenera kugwira ntchito zaka zisanu zomwe zikusonyeza kuti aphunguwa akapitiriza agwira ntchito zaka zisanu ndi chimozi komwe kuli kuphwanya malamulo a dziko lino, anatero mmodzi mwa anthuwo. Pogwirizana ndi gululi pa zomwe lachita pokamangamala ku bwalo la milandu, anthu ena ku Zomba ati pa malamulo, aphunguwa amayenera kukhala zaka zisanu akugwira ntchito, choncho chikachitika chisankho cha president chokha, ndiye kuti aphungu anasankhidwa chaka chatha-wa, agwira zaka zisanu ndi chimodzi (6) zomwe ndi kuphwanya malamulo a dziko lino.
11
Flames ikaluza, Tom abwerera? Kuli nkhondo ku Calabar lero. Flames ikhala ikuphana ndi Nigeria masewero amenenso aunikire ntchito ya mphunzitsi wa Flames Tom Saintfiet. Kupambana kwa lero kuthandiza Uncle Tom kuti mwina apate ntchito yophunzitsa Flames. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Aganyu lero tili pambuyo pa Flames monga tichitira ngakhale kupambana kwalero kufunika Mulungu akhale mbali yathu. Pemphero lathu tigwirana manja ndi mneneri wa ku Chirimba mumzinda wa Blantyre yemwe wabwera poyera kuti waona Flames ikupita pagolo la Nigeria kawiri. Ulosiwu mwina ukutanthauza kuwina chifukwa mawu a mtumikiyu akuti kupita pagolo, ndiye sitikudziwa ngati kupita pagolo kuli kuchinya kapena kungopitapo. Tafuna timvetsetsane apa chifukwa mneneri winanso ku Zomba adalosera kuti akuona Amalawi titanyamula mbendera yathu uko tikusangalala. Iye amalankhula pamene Flames imakumana ndi Namibia. Pamapeto pake tidalepherana mphamvu. Ndiye pena tikuyenera kumvetsa zomwe oloserawa akunena. Koma nkhani ilipo ndi ya Uncle Tom. Kodi tikagonja lero abwereranso kumudzi kuno? Kudzatani? Tikufunsa choncho chifukwa iwo adati loto lawo ndi kugwetsa Nigeria basi, ngati Nigeria siigwa ndiye abweranso? Kapena atengeratu katundu wawo? Ife ndi okonzeka kukhala ndi Uncle Tom bola zomwe anabwerera zitheke. Tonse tili pambuyo pa Flames kuti iwine lero. Pamene maso akhale ku Calabar, aganyu tikhale tili ku Mzuzu kumene Moyale ikhale ikuphana ndi Red Lions mu mchikho cha Carlsberg komanso mawa tikumana pa Kamuzu pamene jombo ya Kamuzu Barracks ipondane ndi mphembedzu za Blantyre United.
16
Kusintha Kwa Nyengo Kukuphwanya Maufulu a Anthu-CADECOM Bungwe la zachitukuko mu mpingo wakatolika la CADECOM lati liwonetsetsa kuti litengepo gawo pa maufulu omwe anthu akuphwanyiridwa kaamba ka kusintha kwa nyengo. Mmodzi mwa akuluakulu ku bungweli a Aaron Kandiwo Mtaya ndi omwe alankhula izi pambuyo pa ulendo wa masiku atatu oyendera madera a Group Village Chaweza, Magoli komanso Kathebwe kwa mfumu yaikulu Mwambo mboma la Zomba. Iwo anati mavuto omwe anthu akukumana nawo kaamba ka kusintha kwa nyengo akubwezeretsa chitukuko mmbuyo, choncho ndi kofunika kuti mabungwe akhale patsogolo kuthandiza anthu omwe akhudzidwa ndi vutoli. Iwo anati ndi udindo wa boma komanso mabungwe kuti awonetsetse kuti ma ufulu a wanthu asawonongeke. Iwo anati pakufunikanso kukhazikitsa malo othawirako okhazikika pamene Anthu akhudzidwa ndi kusefukira kwa madzi osati azithawira msukulu kaamba koti zimenezi zikumasokoneza maphunziro mdziko muno.
18
Agumula chiliza nkutengamo alubino Adaikidwa mmanda pa 27 May mchaka cha 2000. Koma zodabwitsa zachitika pa 17 October 2015 pamene anthu olusa agumula chiliza ndi kuthawa ndi mafupa. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Izi ndizo zachitika mmanda ena kwa Mkanda, T/A Kalolo mboma la Lilongwe komwe anthu ena afukula maliro a alubino amene adaikidwa mmanda zaka 15 zapitazo. Malinga ndi T/A Kalolo, mandawo adagonekapo John Mphoka yemwe adabadwa mu 1952 ndipo adamwalira pa 25 May 2000 ndi kuikidwa pa 27. Malinga ndi Kalolo, malemuwo adali amtundu wa chi alubino, zomwe zikupereka maganizo kwa mfumuyi kuti alipo mdera lawo amene akukhudzidwa ndi nkhaniyi. Nanga inu munthu tidamuika zaka 15 zapitazo, ndiye ngati ndi alendo iwowo adziwa bwanji kuti pamenepa tidakwirirapo munthu wa chi alubino? Alipo konkuno amene akukhudzidwa ndi izi komabe tikufufuza, Kalolo adatero Lachitatu. Kalolo adati adazindikira kuti malemuwo abedwa Lolemba pamene mmudzimo mudagwa thambo lakuda. Iye adati pamene adzukulu amati akakumbe nyumba yoti malemuwo akagone, ndi pamene adaona malodzawo. Pamene timafuna kukumbapo padayandikana ndi pomwe tidagoneka malemuwo. Ndiye mwambo wokumba udasokonekera kaye pamene tidathamangira kukadziwitsa apolisi, adatero. Pamalopo akuti padangotsala bulangete lokha koma bokosi lidali litawola kale. Apolisi atadzafukula akuti adapeza mafupa 22 angonoangono koma mafupa ena onse adatengedwa ndi achiwembuwo. Mneneri wapolisi mumzinda wa Lilongwe Kingsley Dandaula adati nkhaniyo ndi yoona koma akuyenera alandire lipoti kuchokera kwa apolisi awo kuderalo. Tamvadi za nkhaniyi koma tikudikirabe apolisi kuderalo kuti atipatse zomwe apeza komanso kuti tidziwe momwe nkhaniyi ikuyendera, adatero Dandaula. Tili pa nkhani yonga iyi, chisoni chidagwira anthu ammudzi mwa Nyundo kwa T/A Mwansambo mboma la Nkhotakota pamene anthu ena adafukula mafupa pamene amalima mmunda. Malinga ndi mneneri wapolisi ya Nkhotakota, Williams Kaponda, izi zidachitika mu esiteti ya Basal pamene anthu amalima mmundamo pa 18 October. Anthuwo adali akugwira ntchito yolima mmundamo, koma adadzidzimuka pamene adatema fupa. Podabwa, iwo adakauza bwana wawo amene adadzatidziwitsa, adatero Kaponda. Kaponda adati pamodzi ndi achipatala, adathamangira kumundako komwe adakapeza mafupawo ndipo zidatsimikizika kuti adali amunthu amene akumuganizira kuti adamwalira mchaka cha pakati pa 2013 ndi 2014. Koma mayi wina komweko akuti wazindikira zovala za malemuwo kuti adali amuna ake amene adasowa.
7
Papa Wapemphelera Atsogoleri a Maiko Mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse Papa Francisko lero wapemphelera atsogoleri a maiko. Papa Francisko Papa wachita izi lachinayi pa nsembe ya misa yomwe anatsogolera ku likulu la mpingo wa katolika ku Vatican. Iye wati wachita izi powona udindo omwe atsogoleriwa ali nawo oyanganira anthu awo komanso chifukwa cha ziganizo zomwe iwo amachita pafupipafupi zomwe zimakhala zokondweretsa anthu komanso zina zosakondweretsa anthuwo. Ndipo iye wati pa chifukwa chimenechi ndi kofunika kumawapemphelera atsogoleri.
14
Asemphana maganizo Pa ulimi wa chamba Alimi ambiri mdziko muno ati ndi okonzeka kuyamba kulima chamba chosazunguza ubongo mmalo mwa fodya bola boma liwaunikire zomwe ayenera kuchita, koma ena akukaikirabe ngati ulimiwu ungawatulutse muchithaphwi cha umphawi momwe akusambira. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Izi zikudza pamene Nyumba ya Malamulo yavomereza bilu yopereka mphamvu kuboma kuti livomereze ulimi wa chamba chachilendochi monga njira imodzi yopititsira patsogolo chuma cha dziko lino kulowa mmalo mwa fodya. Phungu woima payekha wa dera la kumpoto mboma la Ntchisi, Boniface Kadzamira, masiku apitawo adapempha Nyumba ya Malamulo kuti ipereke mphamvu kuboma kuti livomereze ulimi komanso kugwiritsa ntchito mtundu wina wa chamba wotchedwa industrial hemp. Kadzamira adatsindika kuti mtundu wa chamba chomwe iye akufuna Amalawi azilima ndi ndi wosiyana kwambiri ndi mtundu wina wa chamba chozunguza ubongo chomwenso ena amapenga nacho akachisuta. Chamba akunenacho si ngati ichi chomwe chimazunguza ubongo! Iye adati chamba chomwe akunena chakhala chikulimidwa ndi kugwiritsidwa mmaiko ambirimbiri kuyambira chaka cha 1770, ndipo maiko omwe akulima mbewuyi adatukuka kwambiri kudzera mphindu lomwe amapeza kuchokera ku malonda a mbewuyi. Ine ndine munthu wosangalala komanso wokhutira kwambiri ndi momwe aphungu a ku Nyumba ya Malamulo adaikambirana nkhaniyi. Chamba chili ndi phindu lalikulu kwabasi. Dziko la Malawi nalonso liyenera kuyamba kulima ndi kugwiritsa ntchito mbewuyi kuti tiyambe kupeza nawo phindu lomwe anzathu akupeza maiko enawo, adatero Kadzamira. Ndipo pocheza ndi Msangulutso Lachiwiri, Gunde Njobvu wa mmudzi mwa Moloka mdera la mfumu Kayembe ku Dowa, adati iye ndi wokonzeka kukhala mmodzi mwa alimi oyambirira kulima mbewuyi. Njobvu adati wakhala akulima fodya wa bale zaka zambiri, koma palibe chomwe wapindula. Choncho, sindikuona vuto kuyesako ulimi wa chamba. Mwinanso chamba nkukhala mdalitso wanga ndipo sindikudziwa kuti ndingachite bwanji kuti ndikhale nawo mgulu la alimi oyambirira, adatero mkuluyu. Kambiza Mwale, mlimi wa zaka 60 wochokera mdera la mfumu Kasalika mboma lomweli, adati nkhaniyi adailandira, koma ali ndi mantha kaamba koti omwe akukolezera ulimiwu nkhaniyi sadatulukire nayo poyera kuuza alimi za kusiyana kwa mbewuyi ndi chamba chosuta. Iye adati ali ndi nkhawa poopa kudzagwa nazo mmavuto kaamba kosatsatira malamulo. Mwale adati iye satengapo kaye gawo paulimi umenewu kufikira boma litawaunikira bwino kusiyana kwake kwa mbewu ya chamba choletsedwa ndi mbewu ya chamba chomwe chimagwiritsidwa ntchito popanga zinthu. Towera Jere, wa mmudzi wa Mzukuzuku Jere mboma la Mzimba, naye adati sadapangebe chiganizo ngati nkofunika kuti iye atengepo gawo pa ulimi wa chamba. Jere adati mantha ake ali poti zikamayamba, boma ndi mabungwe amagwiritsa njira ndi mawu onyengelera pofuna kukopa anthu pamene pansi pa mtima akufuna kuwagwiritsa ntchito anthu osauka podzilemeretsa. Alimi mdziko muno agwiritsidwa ntchito ngati makasu a anamadya bwino kwa nthawi yaitali kwabasi. Pomwe ulimi wa fodya unkayamba, anthu timauzidwa kuti masomphenya athu akwaniritsidwa tikalimbikira kulima, koma ndi angati omwe akusimba lokoma lero kaamba ka phindu lochokera muulimi wa fodya? adafunsa mayiyu. Mmodzi mwa achinyamata omwe amakhala pa Luchenza mboma la Mulanje, Violet Banda, adati iye sakuona choletsa kulima chamba chosazunguza ubongo. K oma iye adapempha boma kuti liunikire Amalawi ngati kagulitsidwe ka mbewuyi kadzasiyane ndi momwe zilili ndi fodya wa bale ndi mitundu ina. Ndikunena ichi kaamba koti ndikutha kuona alimi atapatsidwanso chiyembekezo chabodza kuti miyoyo yawo idzasintha kudzera muulimi wa chamba. Ayenera kutiuza kuti kodi adzagule chamba ndani, ndipo akusiyana bwanji ndi omwe akugula bale kuokushoni lero? adatero mtsikanayu. Mkulu wa bungwe la Community Initiative for People Empowerment (Cipe) Trintas Manda adati alibe chiyembekezo kuti dziko la Malawi lidzatukuka kaamba kolima chamba. Manda, yemwe bungwe lake limagwira ntchito zake ku Mzimba ndi Kasungu, adatsindika kuti pokhapokha boma la Malawi litathetsa chiyengo chomwe chikuchitika pamsika wa fodya, dziko lino lidzapitirirabe kulirira kuutsi zokolola zili zake. Woyendetsa ntchito za bungwe la National Initiative for Civic Education (Nice) mboma la Nsanje Kondwani Malunga adati iye akugwirizana ndi zoti pakhale ndondomeko yapadera yodziwitsira anthu za kusiyana kwa chamba choletsedwa ndi chomwe dziko lino likufuna lichivomereze. Anthu ayenera kuphunzitsidwa mokwanira kuti azitha kusiyanitsa pakati pa chamba choletsedwa ndi chomwe boma likufuna kuchivomereza. Apo ayi, tidzaona mavuto ambiri kuposa phindu lomwe dziko lino likuyembekezera kupeza kudzera muulimi umenewu, adatero Malunga. Aphungu angapo ati akugwirizana ndi ganizo loyambitsa ulimi wa chamba mdziko muno. Koma ena, monga Lucius Banda, yemwe ndi phungu wa dera la kumpoto mboma la Balaka, wati monga munthu sangasiyanitse mowa wamasese ndi thobwa, padzakhala povuta kuti anthu asiyanitse mtundu wa chamba chosuta ndi chogwiritsa ntchito kupanga zinthu. Choncho, pamene tivomereza biluyi, nkofunikira kuti tiikenso ndondomeko zapadera zomwe zingatsogolere mabwalo a milandu pozenga mlandu omwe angafune kupezerapo mwayi lamuloli, adatero Banda. Ndipo mkulu wa bungwe la Drug Fight Malawi (DFM) Nelson Baziwelo Zakeyo wati sakugwirizana ndi zomwe achita aphungu a Nyumba ya Malamulo povomereza biluyi, ponena kuti izi zidzabweretsa chisokonezo mdziko muno.
2
Anatchezera Sakufuna kukaonekera Gogo Natchereza, Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Mnyamata wina adandifunsira chibwenzi ndi cholinga choti tidzakwatirane. Padakali pano padutsa zaka zinayi tili paubwenzi, koma palibe chomwe amandiuza chokhudza ukwati. Mnzangayu amangofuna tizigonana basi. Gogo ndithandizeni. Kodi ndimutaye mnyamatayu? TTK TTK, Mutaye! Mnyamatayu zomwe akufuna nzongogonana basi osati za banja. Anyamata ambiri amabwatika atsikana powauza kuti adzawakwatira koma akudziwa kuti zaukwati ali nazo kutali. Chakumtima kwawo chikaphwa, atsikana aja samawawerengeranso. Nawo atsikana vuto lawo lalikulu nkutengeka poganiza kuti akakana kugona nawo awasiya nkukapeza ena. Apatu ine ndikuona kuti mnyamatayu ndi kamberembere. Mutaye asakutaitse nthawi yako pachabe. Gogo Natchereza Bwenzi langa chimasomaso Gogo Natchereza, Ndidakumana ndi mtsikana wina mu mzinda wa Mzuzu zaka zitatu zapitazo, tidapatsana nambala za foni ndipo takhala tikuimbirana mpaka ubwenzi udayamba. Mtsikanayu amagwira ntchito pa ku banki ina mu mzindawo moti ali ndi mnyumba yakeyake yomwe amakhala. Gogo, mnzangayu ndamupezapo katatu konse ali pa chikondi ndi amuna osiyanasiyana, koma wakhala akundipempha kuti ndimukhululukire ndipo ine ndimakhululukadi. Gogo, mtima wanga ndiwosweka chifukwa mnzangayu ndimamukonda kwambiri moti maganizo, moyo ndi mphamvu zanga zonse zidali pa iye. Nditani, gogo? Chonde ndithandizeni! HKA HKA Mtsikanayu ndi njinga simungapitirire kukhala naye paubwenzi. Mutha kutero mwakufuna kwanu, koma mudzanongoneza bondo mtsogolo muno chifukwa khalidwe la chimasomaso sindikuona akusiya. Ngati akuchita ukathyali muli paubwenzi, zidzatha bwanji mukadzamukwatira? Ndikudziwa kuti nzopweteka kusiyana ndi wokondedwa wanu, koma limbani mtima.
12
Boma la Dedza Layamba Kugawa Zipangizo Zotetezera Anthu Akhungu la Chialubino By Glory Kondowe oads/2019/06/gettyimages-534951278-612x612.jpg 612w" sizes="(max-width: 300px) 100vw, 300px" />Anthu akhungu ngati ili akusowa chitetezo Ntchito yogawa zipangizo zotetezera anthu omwe ali ndi khungu la chialubino(pachingerezi security alarms) yayamba mboma la Dedza. Pokhazikitsa ntchito-yi wachiwiri kwa mkulu woyanganira ntchito za apolisi mbomalo Assistant Supritendent Paul Zitha anati ntchito yobweretsa chitetezo kwa anthu omwe ndi akhungu la chialubino komanso kuteteza munthu aliyese ndi ya wina aliyese osati apolisi okha. Assistant Supritendent Zitha anapitiriza kupempha anthu kuti adzikhala a umodzi ponena kuti umodzi umabweretsa mtendere ku dera ngakhalenso ku dziko. Mwambo wokhazikitsa kugawa kwa zipangizozi unachitikira mmudzi mwa Nambirika kwa mfumu yayikulu Kachere mboma lomwelo la Dedza.
6
Kodi Idrissa Walesi akutani mu Mozambique? Mu 2012 ku Mighty Wanderers kudatchuka wosewera wa kumbuyo, Idrissa baba Walesi. Atangotchuka, Walesi adasowa ndipo zidamveka kuti wakwawira ku Mozambique. Chipitireni mu 2014, Walesi adachita zii! Kodi akusewera? Kapena wayamba geni? BOBBY KABANGO adamupeza mumzinda wa Nacala Provincia mdziko la Mozambique ndipo acheza motere; Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Idrissa Baba Walesi ulipo? Ah achimwene, ndilipo ine. Mwasowatu Ukutani mdziko la Mozambique? Walesi akudya bwino ku Mozambique Pajatu chibwerereni kuno mu 2014 ntchito yanga ndi yampira basi. Kuchokera pa nthawiyo ndakhala ndikusewera timu ya Desportivo mpaka lero pamene ndasintha timu. Koma umasewera nthawi yonseyi? Kapena ku training kokha? Haha mwandinyozatu achimwene. Ndakhala ndikusewera pafupifupi gemu iliyonse. Chaka changothachi adandisankha ku timu kwathu kuti ndatchinga bwino kumbuyo. Chibwerereni ku Mozambique, timu yako yasewera bwanji? Chaka chathachi ndiye sizidayende, tathera pa nambala 12 ndi mapointi 29. Chachitika nchiyani kuti uchoke ku timuyi? Tidali pa mgwirizano wa zaka ziwiri, mgwirizano watha koma adandipempha kuti ndisewererebe timuyi koma ndakana chifukwa timu yomwe ndapita panoyi idandilonjeza zochuluka. Timu yanji? Ndipo uzilandira zingati? Ferroviario De Nacala yomwe idathera pa nambala 8. Achimwene mpaka ndinene malipiro? Aah ayi koma inu nokha mutha kudziwa koma musalembe. Koma ndayamba timu imeneyi chaka chatha ndipo tili pa mgwirizano wa chaka chimodzi kuchokera pa 26 February 2016.
15
Boma Lakhululukira Akayidi 184 ="" width="546" height="306" />Wakhululukira akayidi Mtsogoleri wa dziko lino wakhululukira akayidi okwanira 184 opezeka mu ndende zosiyanasiyana za mdziko muno. Malingana ndi chikalata chomwe unduna woona zachitetedzo cha dziko watulutsa, mtsogoleri wa dziko linoyu wachita izi ngati njira imodzi yosangalira nyengo ya kubadwa kwa Yesu Khristu. Akayidi omwe akhululukidwa-wa ndi omwe awonetsa khalidwe labwino komanso omwe anapalamula milandu ingono-ingono.
7
Alangiza Mafumu Athetse Zikhalidwe Zoipa Wolemba: Glory Kondowe Group Villageman Kingstone Likoya ya kwa mfumu yaikulu Mlumbe mboma la Zomba lachinayi yapempha mafumu komanso makolo kuti adzikhala patsogolo pothetsa zikhalidwe zoipa zomwe zimasokoneza kaganizidwe ka ana komanso maphunziro awo. Group Likoya yati zimakhala zomvetsa chisoni kupeza mafumu komanso makolo asakulabadira za makhalidwe achikunja omwe ana achichepere akuonetsa masiku ano. Pamenepa mfumuyi yadzudzula ina mwa miyambo yomwe akuti ndi yomwe ikuchititsa ana kukhala osokonekera. Zimangochitika kuti ena zimakhala ngati bizinesi komabe timalangiza kuti chonde tayetsetsani kuti anawo muziwawuza zokhazokha zomwe zili zofunika kwambiri koma kwinako tisamawonjeze kufikako kumamuwuza mwana ngati ameneyo zomwe zimakhara zowopsya, anatero Group Likoya. Mwazina iwo apempha mafumu anzawo ati aziyenda ndi momwe dziko likuyendera kaamba koti maphunziro ndi omwenso angakweze chitukuko cha dziko lino.
14
TB imakhudza ziwalo zonse Kusiyana ndi nthenda zina, nthenda ya chifuwa chachikulu ya TB imakhudza chiwalo china chilichonse, kupatula zikhadabo ndi tsitsi, watero woona za nthendayi ku unduna wa zaumoyo, James Mpunga. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Iye adati izi zili chomwecho chifukwa tizilombo toyambitsa nthendayi totchedwa microbacterium timatha kulowa mchiwalo china chilichonse cha thupi. Mpunga: Chofunika nkusadukiza mankhwala Ichi nchifukwa chake zizindikiro zakenso zimakhala zochuluka. Mwachitsanzo, kukhosomola, kupweteka kwa pachifuwa, nthawi zina kutulutsa makhololo a magazi, kutuluka thukuta makamaka usiku, kutentha kwa thupi, komanso kupweteka kwa msana. Chifukwa cha ichi, kawirikawiri sikelo ya wodwala imatha kutsika mosavuta, iye adatero. Mpunga adati ngakhale nthenda ya TB imaika anthu pachiopsezo, ndi nthenda yosavuta kuchiza, chachikulu ndi kuyezetsa mwamsanga kuti munthu ayambe kulandira mankhwala komanso kumamwa mankhwala mosadumphitsa ndi mosalekera panjira kufikira munthu atachira. Iye adati chifukwa cha ichi, ndi anthu ochepa okha omwe amamwalira ndi nthendayi ndipo nkhani yaikulu imakhala kunyalanyaza chabe. Munthu odumphizadumphiza kumwa mankhwala amakhala pachiopsezo chosadzachira ndi mankhwalawa, iye adatero. Mpunga adaonjezanso kuti munthu wodwala nthendayi amayenera kulandira chisamaliro choyenera ngati odwala wina aliyense ndipo kuonjezera apa, amayenera kupatsidwa upangiri wa momwe angamamwere mankhwala komanso pa zomwe akuyenera kuchita kuti asapatsire anzake omwe alibe nthendayi. Iye adafotokoza kuti wodwala nthendayi amayenera kumaphimba kukamwa pokhosomola komanso sakuyenera kumakhala pamodzi ndi anthu mmalo othinana ndiopanda mazenera chifukwa potero, akhonza kupatsira anthu enawo mosavuta. Nthendayi ndi yopeweka ndipo njira yodalirika ndi kusapuma mpweya wa munthu yemwe ali ndi nthendayi chifukwa tizilombo toyambitsa nthendayi timafala mwachangu kudzera mumpweya omwe timapuma, iye adatero.
6
Bishop Apempha Abwenzi a Amalitiri Akonde Masacramenti Wolemba: Thokozani Chapola /uploads/2019/09/bishop-stima.jpg 319w" sizes="(max-width: 459px) 100vw, 459px" />Bishop Stima: Akhristu amayenera adziyeretse kuti alandire zaulere zochuluka Episcope wa dayosizi ya Mangochi ambuye Mortfort Stima alimbikitsa abwenzi a maritiri aku Uganda kuti akhale zitsanzo zabwino kwa ena pokonda moyo wa ma sacramenti. Ambuye Stima alankhula izi lero (loweruka) pamene anatsogolera mwambo wa misa yothokoza Mulungu kaamba kowayendetsa bwino mamembala a bungwe la abwenzi a amalitiri aku uganda pa ulendo wawo wa mdziko la Uganda. Iwo ati munthu amene amapita ku malo oyerawa akuyenera kukhala okonzekera bwino kuti akapeze zaulere zochuluka. Pamwambowu bungwe la abwenzi a Amalitiri a ku Uganda lapereka mabatire awiri ku Radio Maria Malawi ndipo malinga ndi wapampando wa gululi mayi Grace Kalanda achita izi pothokoza ntchito imene wailesiyi imagwira pofalitsa mauthenga okhudza ulendo wa ku Uganda. Mmawu ake mkulu woyendetsa ntchito za Radio maria malawi a Louis Phiri ayamikira bungweli kaamba ka chidwi chake pothandiza wailesiyi mu zosowa zake.
13
Bwanji wodwala chikuku amasamalidwira kutchire? Tsaka: Akachira amakhalandi mphamvu zotakata Makono ano munthu wodwala chikuku amasamalidwa pakhomo kapena kuchipatala ndipo malangizo amene kale ankatsatidwa adalekeka. Kalelo, wodwala chikuku ankakabisidwa kunkhalango kuti asakumane ndi munthu wotentha thupi. Awiriwa akangokumana matenda akuti amakula msinkhu. Kuthengoko kumachitikanji? Nanga wotentha thupi amadana ndi wodwalayu bwanji? BOBBY KABANGO adali mmudzi mwa Mphonde kwa Senior Chief Ngabu ku Chikhwawa ndipo akucheza ndi Eni Tsaka motere: Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Tidziwane wawa. Dzina langa ndi Eni Tsaka, ndi dzina lomwe makolo adandipatsa ndithu, ena amaganiza ngati ndidadzipatsa ndekha. Ndine mlimi wa thonje komanso mapira ndi mchewere. Ndakhalitsa mdziko la South Africa moti ndidadzakhazikika mdziko muno mu 1974. Komatu dzuwa kuno, mukumva bwanji? Lero bolani, palibe dzuwa apa kusiyanitsa ndi masiku ena. Tinangozolowera, nchifukwa munandipeza nditavula malaya. Kuno malaya sitikhalanawo chidwi chifukwa cha kutenthaku. Tikumva kuti kuno miyambo yakalekale ikuchitikabe, nzoona? Pali choletsa kuti miyambo isachitike kodi? Mwina ndimve kwa inu ngati pali choletsa komanso chifukwa chomwe akuletsera. Koma ikuchitika? Kwambiri. Nchifukwa ndikuti pali choletsa? Ife tikutsata zomwe makolo ankachita komanso adatiuza kuti tizichita. Za miyambo ndi zikhulupiriro sitidzasiya. Kukakamira zachikale bwanji? Kodi zachikale zisiyike chifukwa mwapita kusukulu? Vuto lake mukapita kusukulu mukumaona ngati miyambo ya makolo njopanda ntchito. Kaamba ka izi tikuvulala. Iyi ndi miyambo komanso zikhulupiriro za makolo athu, sitingasiye ndipo sitidzasiya. Tamva kuti wotentha thupi sakumana ndi wodwala chikuku, nzoona? Ndi zenizeni zomwe mwauzidwazo. Munthu wodwala chikuku ndi mdani ndi wotentha thupi ndipo sayenera akumane, ndi ngozi imeneyi. Kutentha thupi nkutani? Kutentha thupi kutanthauza kuti wagonana ndi mwamuna kapena mkazi. Zikachitika ndiye kuti watentha thupi? Zimatero kumene. Thupi silimatentha popanda munthu wolitenthetsa, pamayenera pakhale wina amene amachititsa thupi lija kuti lichite juuu! Ndipo izi zimachitika ngati mwamuna kapena mkazi wachita motero. Mawu amenewa akuchokera pati? Akuchokera pantchito yomwe mwamuna ndi mkazi amachita, pajatu ntchito imeneyi imachititsa thupi kutentha. Mawuwatu akuchokera pamenepo. Ndiye akatentha sayenera kukumana ndi wodwalayu? Ndipo asakumane, ndi ngozi iyi. Kuno tikupangabe zimenezi. Kukumana kwake kotani? Tiyerekeze kuti mnyumbamu mwagona wodwala, wotentha thupi asayandikirenso pakhomopo ndipo azingolambalala. Mphepo yokhayo ingathe kupha wodwalayu chifukwa mphepo yake imakhala yamoto. Ndiye mumamusamala bwanji wodwalayu? Mukadziwa kuti nthenda yafika timamutengera kuthengo loyandikana ndi nyumba yake komwe amakakhala mpaka atachira koma madzulo okha timamubweretsa. Amakakhala ndi yani kuthengoko? Nanga imakhala nthawi yanji yomwe mumamubweretsa? Kuthengoko kumakhala makolo ake ndi ena achibale, ochepa koma. Awa ndiwo amamusamala pomupatsa chakudya komanso kumumwetsa mankhwala achikukuwo. Usiku anthu atagona mpomwe timabwera naye kunyumba ndipo mbandakucha timamutengeranso kuthengoko. Mumamupatsa mankhwala anji? Timatenga makungwa a mtengo wa theza ndiye timawanyika. Pakapita kanthawi amafewa ndiye amananda. Zikafika pamenepa timamuika kukhutu ndi mmaso koma zonsezi zichitikire kuthengoko. Mukalondoloza zonse matendawo sachedwa kuchira. Sizitheka kuti wodwalayu thupi lakenso ndi lotentha? Aaaa! Inu munthu akudwala ndiye angakhalenso ndi nthawi kapena mphamvu zotenthetsa thupi? Sizingatheke koma akachira ndiye amakhala ndi mphamvu zotakata momwe angathere. Koma amachira ndi zomwe mwanenazi? Zimatheka, taona anthu akuchira koma akapanda kutsata mwambo ndi kumachita zinthu limodzi ndi wotentha thupi ndiye sipatha masiku mumva wamwalira. Koma ndi mwambo wabwino? Kwambiri ndipo sumamva kuti wina wamwalira chifukwa cha matenda amenewa koma vuto ndi chizungu. Talowetsa chizungu kwambiri nchifukwa tikuyesa zikhulupiriro za makolo ngati zachabe.
7
PMS Yakhutira ndi Ntchito Yophunzitsa ana a Tilitonse pa Radio Maria Ofesi yowona za mabungwe a utumiki wa a Papa mdziko muno ya Pontifical Mission Societies (PMS) yati ndi yokhutira ndi momwe maphunziro a mpingo pakati pa ana akuyendera kudzera pa Radio Maria Malawi. Mkulu wa ku ofesiyi bambo Vincent Mwakhwawa anena izi polankhula ndi mtolankhani wathu pomwe amathilira ndemanga pa za momwe maphunziro a ana Tilitonse akuyendera chiwakhadzikitsileni pa wailesiyi. Iwo apempha aphunzitsi a anawa pamodzi ndi makolo awo kuti adzipereke pa ntchito yolimbikitsa anawa kuti adzimvera ndi kutenga nawo mbai pa maphunzirowa kudzera pa Radio Maria. Maphunziro amene tikuchita pa Radio Maria akupindula kwambiri kaamba koti mu nthawi ino yomwe kuli mliri wa Coronavirus ana sangathe kusonkhana pamodzi, choncho tikupempha makolo komanso ana onse kuti alimbikitse anawa kutenga nawo gawo mu maphunzirowa kudzera pa wailesi ya Amayi Maria, anatero bambo Mwakhwawa. Mwazina bambo Mwakhwawa ati pambuyo pa maphuzirowa anawa azafunsidwa mayeso omwe ana amene azachite bwino azalandila mphoto zosiyanasiyana.
13
Papa Wapempha Akhristu Ayike Chikhulupiriro Mwa Mulungu Mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse Papa Francisco wapempha akhristu mu mpingowu kuti ayike chikhulupiriro chawo mwa Mulungu kaamba koti ndi yemwe angathetse mavuto amwe amakumana nawo. Papa Francisco walankhula izi mu zolankhulalankhula zomwe amakhala nazo lachitatu lililonse ku likulu la mpingowu ku Vatican. Iye wati ankhristu atengere chitsanzo cha Batumeyo wankhungu yemwe anachiritsidwa ku vuto losaona atakhulupilira yesu khristu choncho wapempha ankhristu kuti azikhala ndi chidwi choitana yesu khristu kuti awachiritse ku nthenda komanso mavuto omwe akukumana nawo potengera chisanzo cha Batumeyo-yu. Mwazina wati Yesu Khristu ndi yekhayo amene angawachotsere anthu mdima wa tchimo ndi kuwakhululukira.
13
Dayosizi ya Chikwawa Yayamba Kuphunzitsa Akhristu Kapewedwe ka COVID-19 Mpingo wa katolika mu dayosizi ya Chikwawa wakhazikitsa ntchito yophunzitsa akhristu ake njira zabwino zopewera nthenda ya COVID-19 yomwe ikufala kamba kachilombo kotchedwa Coronavirus. Malinga ndi malipoti, ntchitoyi inayamba kale ndipo mmodzi mwa azachipatala omwe anayitanidwa kuti adzafalitse uthengawu mkulu wa anamwino pa chipatala cha boma la Chikwawa, a Lusayo Malango. Mukulankhula kwawo a Malango alimbikitsa akhristu-wa kuti azitsatira njira za ukhondo, monga kusamba mmanja bwino ndi sopo, komanso apewe mchitidwe wobisa anthu amene akulowa mdziko muno kuchokera ku mayiko kumene nthendayi yafala kale. A Malango apereka malangizo-wa tsiku lamulungu ku Limana la St. Monica ku parish ya St. Michaels mu dayosizi ya Chikwawa. Monga akhristu a limana la St. Monica titenge maphunziro omwe aperekedwa pano kuti tikalimbikitse izi mmakomo mwathu pokhala a ukhondo monga kusamba mmanja ndi sopo ndi kupewa kugwira maso, mphuno ngakhalenso pakamwa tisanasambe mmanja kuti tisatenge kachilomboka, anatero a Malango. Padakalipano nthambi ya zaumoyo mbomalo yapereka mankhwala a Chlorine ku ma tchalitchi ndi malimana kuti athandizire njira zolimbikitsa ukhondo pofuna kupewa Coronavirus.
6
Nanga wapolisi ataphofomoka? Masiku ano sichikhala chachilendo kuona apolisi atakwera galimoto mosayenera. Ngakhale ntchito yawo nkuonetsetsa kuti malamulo akutsatidwa, ngakhale pamsewu, apolisiwo ndiwo amakhala oyamba kuphwanya malamulowo. Kodi anthu wamba atakwera galimoto monga achitira apa apolisi, sangakalowe kozizira? Mwinatu iwowa ali ndi mphamvu kuposa lamulo.
7
Mafumu akhumudwa ndi kuvula amayi Mafumu komanso anthu mdziko muno ati ndiokhumudwa ndi zomwe oganiziridwa kuti ndi mavenda mmizinda wa Lilongwe, Blantyre ndi Mzuzu msabatayi povula mbulanda amayi omwe adavala mabuluku kapena siketi zazifupi. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Ndemangazi zati apolisi afufuze ndi kugwira omwe adachita chipongwechi. Malipoti osatsimikizika ochokera ku Mzuzu Lachitatu amati kumenekonso ena adavula amayi ena kumalo okwerera basi ndipo pomwe nthawi imakwana 12 koloko nkuti apolisi ali balala. Mafumuwa ati apolisi sakuyenera kunyengerera ndipo yemwe agwidwe akuyenera kukalandira chilango. T/A Kaomba ya mboma la Kasungu idati ngati munthu sadavale moyenera ndibwino kuwauza ena amudzudzule, osati kumuvula. Zandikwiyitsa. Ngati sadavale bwino akadapeza amayi ena kuti akawadzudzule; uku nkuchititsa manyazi dziko, adatero Kaomba. Senior Chief Tengani ya mboma la Nsanje yati kuvula amayi silingakhale yankho ngakhale mayiyo atavala molakwika chotani, kotero boma likuyenera kuchitapo kanthu. Ife mafumu timalipitsa ovala molakwika. Wina akakuwa mnzake kuti sanavale bwino, mafumu timalipitsa wokuwayo. Otero amalipa nkhuku. Koma wina atavula mayi ndiye kuti mlandu uwu sitiweruza; tiuza apolisi kuti akafikitse nkhaniyi kubwalo lamilandu, adatero Tengani. Lachitatu mneneri wa boma, Patricia Kaliati adachititsa msonkhano wa atolankhani mumzinda wa Lilongwe momwe adadzudzula mchitidwewu. Iye adati mayi aliyense yemwe waona zokhomazi awadziwitse.
1
Kanengo Parish Yayimitsa Maulendo Onse a Kunyanja Wolemba: Thokozani Chapola Parish ya St. Francis Kanengo mu arch-diocese ya Lilongwe yayamba yaletsa maulendo onse a mabungwe a ku parish-yi opita ku nyanja, potsatira imfa yomira mmadzi ya mmodzi mwa achinyamata mu parish-yi. Wapampando wa parishiyi mayi Chrissy Madeya alengeza za kusinthaku pa mwambo wa nsembe ya ukaristia lamulungu lapitali. Iwo ati achita izi kuti ayambe afufuza kaye ndi kupeza njira zokhazikika zothetsera ngozi za mtunduwu ku parishiyo. Pamenepa mayi Madeya alangiza magulu ndi mabungwe onse a mu parishiyi kuti ayambe ayimitsa kaye maulendo onse omwe anakonzedwa okhudza ku nyanja. Nkhaniyi ati siyinasangalatse akhristu ena a mparishiyi poganizira kuti ena anali atayamba kale kukonzekera maulendo awo opitanso kunyanja mmasiku akubwerawa chakachi chisanathe. Loweruka lapitali, achinyamata a mphakati wa 9B ku parishiyi anapita kunyanja mboma la Salima kukasangalala ngati imodzi mwa zinthu zomwe anakonza kuti zichitike mchakachi. Achinyamatawa anazindikira kuti mmodzi mwa iwo wamira pa nthawi imene amanyamuka kuti adzibwelera ndipo mnyamatayu ati anamupeza atafa kale mmadzimo. Malinga ndi zomwe achinyamatawa afotokozera Radio Maria Malawi, malemuyu analedzera kwambiri ndipo kenako analowa mmadzi kuti asambire ndipo ndi pomwe anamira ndi kufa.
6
Kafukufuku wa cashgate sadayankhe Mabungwe omwe si aboma ati zotsatira za kafukufuku wa kubedwa kwa ndalama za boma (cashgate) kulikulu la dziko lino zomwe boma latulutsa sabata ino zangokanda pamwamba pa nkhani zikuluzikulu zomwe Amalawi amayembekezera. Mabungwewa ati imodzi mwa nkhani zikuluzikulu zomwe zotsatira za kafukufukuyu sizidachite bwino ndi kubisa maina a anthu komanso makampani omwe akukhudzidwa ndi nkhaniyi. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC John Kapito, mkulu wa bungwe loona za anthu ogula ndi kugwiritsa ntchito katundu wosiyanasiyana, yemwenso amakonda kulankhulapo pankhani za mmene zinthu zikuyendera mdziko muno, wati zotsatirazo zikadatchula maina a anthu ndi makampani okhudzidwa kuti anthu adziwe. Munthu aliyense yemwe akutsatira bwino za nkhaniyi akuyembekezera kudziwa anthu ndi makampani omwe adasakaza chuma chawo koma zotsatirazi zangokhazikika pa kuchuluka kwa ndalama zosokonekerazo ndi momwe zidasokonekerera basi zomwe anthu adamva kale, watero Kapito. Boma lidapereka mphamvu kukampani ya ku Britain ya Baker Tilly Business Services kuti ichite kafukufuku wakuya pankhaniyi ndipo idapeza kuti ndalama zonse zomwe zidasokonekera ndi K13.6 biliyoni. Malingana ndi zotsatira zomwe zatulutsidwazo kampaniyi idalephera kuulutsa maina a anthu ndi makampani okhudzidwa poopa kusokoneza milandu ya nkhaniyi yomwe pakalipano ili kukhoti. Pakadalipano milandu yokwana 70 ili mmabwalo a milandu momwe anthu osiyanasiyana ogwira ntchito mboma akuwafunsa kuti alongosole bwino za mmene adapezera chuma chankhaninkhani ndi ena omwe adapezeka ndi ndalama zambiri. Nduna ya zachuma Maxwell Mkwezalamba wati kafukufukuyo sadalondole pandalama zomwe zidasokonekera ati chifukwa ochita kafukufukuyo adafukula mbali zina zomwe samayenera kukhudzako. Ndalama zenizeni zomwe zidasokonekera ndi K6.1 biliyoni osati K13.6 biliyoni monga mmene zotsatira za kafukufukuyu zikusonyezera. Akatswiri omwe amachita kafukufukuyu adapeza K13.6 biliyoni chifukwa adalowerera mmadera ena omwe samafunika kukhudzamo, watero Mkwezalamba polongosola. Kutengera nyuzipepala ya The Nation ya Lachiwiri lapitali akatswiri omwe adachita kafukufukuyu adzudzula banki yaikulu ya Reserve Bank of Malawi ndi mabanki angonoangono polephera ntchito yawo ndi kulekerera ndalama zambiri zikupita mmadzi. Kafukufukuyu wati mwa maakaunti 554 a kubanki aboma akatswiri ochita kafukufukuyu adaloledwa kuunika maakaunti 11 okha zomwe mabugwe ati nzogwetsa mphwayi kukhulupirira zotsatira za kafukufukuyo. Mmodzi mwa akuluakulu a mabungwe omwe si aboma Lucky Mbewe wa bungwe loona kuti achinyamata akupatsidwa mphamvu zokwanira zotenga nawo mbali pachitukuko wati boma silikuonetsa chidwi pankhani ya kusokonekera kwa ndalamaku. Iye wati ngati nzika za dziko lino, Amalawi ali ndi ufulu wodziwa chilichonse pankhaniyi ndipo wapempha kuti boma lisinthe mmene likutengera nkhaniyi ndi kupanga zakupsa kuti Amalawi akhale ndi chikulupiriro mboma lawo.
7
Kwelepeta Apempha Anthu Ake Asiye Ndale Wolemba: Thokozani Chapola Phungu wa dera la Zomba Malosa, mayi Grace Kwelepeta wapempha anthu a mdera lake kuti asiye ndale ndi kugwirana manja popititsa patsogolo chitukuko cha deralo. Phunguyu amalankhula izi pa phwando lomwe anakonzera anthu a mdera lake pofuna kuwathokoza pomusankha pa udindo wa phungu wa derali pa chisankho chomwe chapitachi. Kwelepeta yemwenso ndi wachiwiri kwa nduna yowona za kusasiyana pakati pa amayi ndi abambo, ana, olumala ndi chisamaliro cha anthu walonjeza kuti apereka galimoto la mtundu wa ambulance kuti izithandiza mderalo. Nthawi ya ndale inatha ndipo ino ndi nthawi ya chitukuko. Tikalimbikira ndale dera lino silitukuka ayi, anatero mayi Kwelepeta. Mmawu ake Group Village Headman Mtogolo, anagwirizana ndi phunguyu pa nkhani ya mgwirizano mderalo ngakhale anthu ali osiyana zipani za ndale. Ngati tikufuna kuti chitukuko chiyende tikuyenera kugwira ntchito limodzi ndi phungu wathu ndiye ndikuona kuti zimenezi ndi zoona ndipo ndi zofunika kwambiri, inatero mfumu Mtogolo. Mfumuyi yati anthu a mdera lake ndi okonda chitukuko ndipo alimbikitsa anthu ake kuti agwirane manja ndi phunguyu kuti athetse mavuto ochuluka omwe ali mderalo.
10
Maepiskopi a Malawi, Zambia, Zimbabwe ayambitsa Bungwe Lawo Ma episkopi a mpingo wa katolika mmaiko a Malawi, Zambia komanso Zimbabwe agwirizana zoyambitsa bungwe lawo. Ma episkopiwa agwirizana izi pa mkumano wawo omwe unachitikira mdziko la Zambia kuyambira pa 3 mpaka pa 5 February 2020. Maepiskopi a ku Malawi, Zambia ndi Zimbabwe Malinga ndi zokambiranazi, kuchita izi kuthandiza kwambiri kupititsa patsogolo mpingo wakatolika mmaiko atatuwa kuti utukuke koposa. Ma episkopiwa ati akuchita izi motsata malamulo a mpingo wa katolika canon law gawo 341. Mtsogoleri wa dziko la Zambia, Edgar Lungu wayamikira maganizo a ma episkopi a mpingo wa katolika a maiko a Malawi, Zambia ndi Zimbabwe ogwilira ntchito limodzi. Polankhula lolemba pomwe amatsegulira msonkhano wa ma episkopi-wa omwe ukuchitikira mdziko la Zambia, a Lungu anati ali ndi chikhulupiliro kuti ubale omwe ulipo pakati pa atsogoleri a mpingowu mmaikowa uthandiza pokweza ntchito za chitukuko mmaiko onsewa ndipo iye ayika chidwi pothandiza mpingowu mu njira zosiyanasiyana. Omwe anachita mkumanowu ndi wapampando wa bungwe la maepiskopi mdziko la Zambia la Zambia Conference of Catholic Bishops, Bishop George Cosmass Zumaire Lungu, wapampando wa ngwe la maepiskopi mdziko la Malawi Archbishop Thomas Luke Msusa komanso wapampando wa bungwe la maepiskopi mdziko la Zimbabwe Archbishop Robert Ndhlovu.
13
Joyce Banda akumana ndi mafumu, otsutsa azizwa Joyce Banda akumana ndi mafumu, otsutsa azizwa Mtsogoleri wa dziko lino Joyce Banda Lachinayi adakumana ndi mafumu a mdziko muno, zomwe zidachititsa otsutsa boma ena kuzizwa. Banda adakumana ndi mafumuwo kunyumba ya boma ya Sanjika mumzinda wa Blantyre. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Koma mneneri wa chipani cha UDF Ken Ndanga adati chipanicho chakhala chikudabwa ndi momwe Banda amachitira zokhudza mafumu. Tikudziwa kuti iyi ndi njira yakuti mafumu akhale mbali yake pomwe chisankho chili pamphuno, adatero Ndanga. Ndipo mneneri wa DPP Nicholas Dausi adati akudabwa kuti Banda akuchita zimene ankadzudzula nazo mtsogoleri wakale wa dziko lino Bingu wa Mutharika. Bingu akaitana mafumu, Banda amati si bwino. Mmalo mowasiya mafumu kuunikira momwe kalembera wa chisankho akuyendera, akuwaitanitsa kunyumba ya boma, adatero Dausi. Pomwe timasindikiza Tamvani Lachinayi nkuti zisanadziwike kuti Banda ndi mafumuwo amakambirana chiyani. Mneneri wa kunyumba ya boma Steven Nhlane, adanena msonkhanowo usadachitike kuti samadziwa zomwe mtsogoleri wa dziko lino ndi mafumuwo amakambirana. Naye mneneri wa unduna wa maboma aangono Maganizo Mazeze samadziwa zomwe amakambirana.
8
Zipolowe atamangidwa Mutharika Kumangidwa kwa anthu 11 omwe akukhudzidwa ndi nkhani yofuna kulanda boma Bingu wa Mutharika atamwalira sikudakomere anthu ena amene adachita zipolowe mmadera osiyanasiyana. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Pamene Peter Mutharika adapita kukadzipereka kulikulu la polisi mchigawo cha kumwera Lolemba, anthu ambiri otsatira chipani cha DPP adakhamukira kumeneko, komwe adakhambitsana ndi apolisi. Apolisi adabalalitsa anthuwo ndi utsi wokhetsa misozi mpaka mtsogoleri wogwirizirayu atamutengera ku Lilongwe. Ndipo pamene akuluakuluwa amayembekezeka kukaonekera ku bwalo la milandu kuti akapatsidwe belo Lachiwiri, owatsatira adali kuphwanya galimoto zina, kuotcha mateyala ndi kuponya miyala. Izi zidachititsa kuti ozengedwa mlanduwo asapite kubwalolo. Izi zidachititsa mneneri wa chipani cha DPP Nicholas Dausi, yemwe ndi mmodzi mwa oimbidwa mlanduwo, kuti aloze chala kuti ochita zipolowewo si a DPP. Tikudziwa kuti akuchita izi kuti tisapatsidwe belo. Tipemphe masapota athu kuti akaona aliyense atavala T-Shirt yatsopano ya DPP ndipo akuyambitsa zipolowe amugwire ndipo amutengere kupolisi, adatero Dausi, kuuza wailesi ya Zodiak. Iye adati adagonekedwa mkachipinda kakangono kupolisi ya Lumbadzi momwe mudali udzudzu wosaneneka ndipo adagona pasimenti opanda chofunda. Atangomangidwa, angapo mwa akuluakuluwo adadwala. Awa ndi Goodall Gondwe yemwe adakomoka, Patricia Kaliati amene magazi ake amathamanga. Omangidwa ena ndi Jean Kalirani, Kondwani Nankhumwa, Symon Vuwa Kaunda, Henry Mussa, Bright Msaka komanso Necton Mhura. Mlanduwo ukukhudzanso yemwe adali mlangizi wa Bingu pa za malamulo Allan Ntata yemwe padakali pano ali kunja kwa dziko lino. Iwo akuimiriridwa pamilanduyo ndi Frank Mbeta, Kalekeni Kaphale, Samuel Tembenu, Noel Chalamanda ndi Chancy Gondwe. Ena mwa omwe adapita kubwalo la milandu kukaonetsa kuti ali pambuyo pa oimbidwa milanduwo ndi mkazi wa Bingu, Callista Mutharika, mwana wake womupeza Duwa komanso nduna zina zakale.
11
MERA Yakhazikitsa Ndondomeko Zatsopano Unduna woona za chilengedwe, mphamvu za magetsi ndi migodi wayamikira bungwe loona za mulingo wa mphamvu ndi magetsi mdziko muno la Malawi Energy Regulatory Authority (MERA) kamba ka ndondomeko zomwe limatsata pogwira ntchito zake zomwe ati zikuthandiza kupititsa patsogolo chuma cha dziko lino. Kumtsaira: Wayamikira bungwe la MERA Nduna mu undunawu a Binton Kuntsaila anena izi lachinayi mu mzinda wa Lilongwe pomwe bungwe la MERA limakhazikitsa ndondomeko zomwe litsate pogwira ntchito zake kuyambira chaka chino mpaka chaka cha 2024. Ndondomekozi zili mmagawo awiri; ina yothandiza makasitomala omwe afuna thandizo ku bungweli, Customer Service Charter; komanso ina yomwe bungweli layikamo ma plan ake a zaka zomwe zikubwerazi Strategic Plan pachingerezi. A Kumtsaila ati malamulo omwe bungweli linakhazikitsa posachedwapa okhudza zamagetsi athandiza kuti anthu omwe amagwiritsa ntchito magetsi azikhala otetezeka. Chitukuko cha dziko sichingapite patsogolo opanda mphamvu za magetsi. Ndondomeko yomwe yakhazikitsidwayi ithandiza kukonza mavuto omwe analipo. Sitikufuna zisakasa zama filling station zomwe ena amamanga pakatipa, anatero a Kumtsaila. Polankhulanso wapampando wa board ya bungweli bishop Dr. Joseph Bvumbwe ati ndondomeko yatsopanoyi yakonza zina zomwe sizidayende bwino mu ndondomeko ya mmbuyomu. Pali zina zina zomwe timadzudzulidwa kuti sitikuchita bwino koma panalibe ndondomeko zake zoyendetsera zimenezo tsopano takhazikitsa ndondomeko zomwe zizitsogolera bungwe lathu, anatero bishop Bvumbwe. Iwo ati kudzera mu ndondomekoyi, anthu ofuna kuyamba kugulitsa mafuta azipatsidwa chilolezo pakatha mwezi umodzi komanso akawunikira kaye bwino malo amene akufuna kumanga malo ake ochitira malndawo.
2